Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala

Puslapio numeris:close

external-link copy
15 : 10

وَإِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِمۡ ءَايَاتُنَا بَيِّنَٰتٖ قَالَ ٱلَّذِينَ لَا يَرۡجُونَ لِقَآءَنَا ٱئۡتِ بِقُرۡءَانٍ غَيۡرِ هَٰذَآ أَوۡ بَدِّلۡهُۚ قُلۡ مَا يَكُونُ لِيٓ أَنۡ أُبَدِّلَهُۥ مِن تِلۡقَآيِٕ نَفۡسِيٓۖ إِنۡ أَتَّبِعُ إِلَّا مَا يُوحَىٰٓ إِلَيَّۖ إِنِّيٓ أَخَافُ إِنۡ عَصَيۡتُ رَبِّي عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ

Ndipo Ayah Zathu zomveka bwino zikawerengedwa kwa iwo, akunena amene sayembekezera kukumana ndi Ife: “Bwera ndi Qur’an (yogwirizana ndi zofuna zathu) osati iyi, kapena uyisinthe (pang’ono).” Nena: “Nkosatheka kwa ine kuisintha mwachifuniro changa. Sinditsata koma zimene zikuvumbulutsidwa kwa ine. Ndithu ine ndikuopa chilango cha tsiku lalikulu ngati ndinyoza Mbuye wanga.” info
التفاسير:

external-link copy
16 : 10

قُل لَّوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا تَلَوۡتُهُۥ عَلَيۡكُمۡ وَلَآ أَدۡرَىٰكُم بِهِۦۖ فَقَدۡ لَبِثۡتُ فِيكُمۡ عُمُرٗا مِّن قَبۡلِهِۦٓۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ

Nena: “Allah akadafuna, sindikadakuwerengerani Qur’aniyi ndiponso sakadakudziwitsani Qur’aniyo, ndidakhala pakati panu moyo wanga (zaka zambiri) isadavumbulutsidwe, (simudandimve ndikunena chilichonse cha utumiki). Kodi mulibe nzeru?” info
التفاسير:

external-link copy
17 : 10

فَمَنۡ أَظۡلَمُ مِمَّنِ ٱفۡتَرَىٰ عَلَى ٱللَّهِ كَذِبًا أَوۡ كَذَّبَ بِـَٔايَٰتِهِۦٓۚ إِنَّهُۥ لَا يُفۡلِحُ ٱلۡمُجۡرِمُونَ

Ndani woipitsitsa woposa yemwe akumpekera Allah bodza, ndi yemwe akutsutsa Ayah Zake? Ndithudi, sangapambane wochita zoipa. info
التفاسير:

external-link copy
18 : 10

وَيَعۡبُدُونَ مِن دُونِ ٱللَّهِ مَا لَا يَضُرُّهُمۡ وَلَا يَنفَعُهُمۡ وَيَقُولُونَ هَٰٓؤُلَآءِ شُفَعَٰٓؤُنَا عِندَ ٱللَّهِۚ قُلۡ أَتُنَبِّـُٔونَ ٱللَّهَ بِمَا لَا يَعۡلَمُ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَلَا فِي ٱلۡأَرۡضِۚ سُبۡحَٰنَهُۥ وَتَعَٰلَىٰ عَمَّا يُشۡرِكُونَ

Ndipo iwo akupembedza milungu yina kusiya Allah, yomwe singathe kuwapatsa masautso (ngati atasiya kuipembedza) ndiponso siyingathe kuwapatsa chithandizo (ngati atalimbika kuipembedza) ndipo akunena: “Iwo (mafanowo) ndi aomboli athu kwa Allah.” Nena: “Kodi mukumuuza Allah zomwe sakudziwa kumwamba ndi pansi? Wapatukana Allah Ndipo watukuka kuzimene akum’phatikiza nazo.” info
التفاسير:

external-link copy
19 : 10

وَمَا كَانَ ٱلنَّاسُ إِلَّآ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ فَٱخۡتَلَفُواْۚ وَلَوۡلَا كَلِمَةٞ سَبَقَتۡ مِن رَّبِّكَ لَقُضِيَ بَيۡنَهُمۡ فِيمَا فِيهِ يَخۡتَلِفُونَ

Ndipo ndithudi anthu kalero (m’nthawi ya Adam) adali mpingo umodzi (opembedza Allah), koma adasiyana (pambuyo pake). Ndipo pakadapanda liwu lochokera kwa Mbuye wako, lomwe lidatsogola (lakuti adzawalanga tsiku la Qiyâma), ndithu kukadaweruzidwa pakati pawo m’zomwe adali kusiyana.[218] info

[218] Ndithudi, anthu mchilengedwe chawo adali a mpingo umodzi wogonjera Allah mwa chilengedwe. Kenako Allah adawatumizira aneneri kuti awatsogolere kunjira Yake molingana ndi chilamulo chake Allah. Koma ngakhale zili tere anthu adali ndi ufulu mwa chilengedwe chawo kulandira choipa kapena chabwino. Potero, choipa chidawagonjetsa ena a iwo natsata zilakolako za satana. Nasiyana ndi anzawo chifukwa chazimenezo. Komatu padali lamulo la Allah la pachiyambi loti oipa sadzawalanga mwachangu koma kufikira nthawi yawo itakwana. Pakadapanda lamuloli ndiye kuti onse akadawalanga nthawi yomweyo.

التفاسير:

external-link copy
20 : 10

وَيَقُولُونَ لَوۡلَآ أُنزِلَ عَلَيۡهِ ءَايَةٞ مِّن رَّبِّهِۦۖ فَقُلۡ إِنَّمَا ٱلۡغَيۡبُ لِلَّهِ فَٱنتَظِرُوٓاْ إِنِّي مَعَكُم مِّنَ ٱلۡمُنتَظِرِينَ

Ndipo akunena: “Kukadakhala kuti chinatsitsidwa kwa iye chizindikiro (chotsimikizira uneneri wake) chochokera kwa Mbuye wake (chomwe takhala tikuchipempha nthawi ndi nthawi).” Nena (kwa iwo): “Ndithu kudziwa zobisika nkwa Allah Yekha. Choncho dikirani (chiweruzo cha Allah) inenso pamodzi nanu ndine mmodzi wa odikira.” info
التفاسير: