Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ

Numéro de la page:close

external-link copy
133 : 3

۞ وَسَارِعُوٓاْ إِلَىٰ مَغۡفِرَةٖ مِّن رَّبِّكُمۡ وَجَنَّةٍ عَرۡضُهَا ٱلسَّمَٰوَٰتُ وَٱلۡأَرۡضُ أُعِدَّتۡ لِلۡمُتَّقِينَ

Ndipo chimkereni mwachangu chikhululuko cha Mbuye wanu (kupyolera m’zochita zanu zabwino), ndi Munda (Wake) umene Kutambasuka kwake (mulifupi) kuli ngati kumwamba ndi pansi, (womwe) wakonzedwa kuti ukhale wa oopa Allah.[87] info

[87] Ndime iyi ikulimbikitsa anthu kuti akangaze kuchita zinthu zowapezetsa chikondi cha Allah.

التفاسير:

external-link copy
134 : 3

ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ فِي ٱلسَّرَّآءِ وَٱلضَّرَّآءِ وَٱلۡكَٰظِمِينَ ٱلۡغَيۡظَ وَٱلۡعَافِينَ عَنِ ٱلنَّاسِۗ وَٱللَّهُ يُحِبُّ ٱلۡمُحۡسِنِينَ

Omwe amapereka (zopereka zawo mwaulere) pamene akupeza bwino ngakhale pamene akuvutika; amenenso amabisa ukali wawo ndi okhululukira anthu. Ndipo Allah amakonda ochita zabwino.[88] info

[88] Ndime 134-135 zikutchula ena mwa makhalidwe omwe munthu atakhala nawo akalowa ku Munda wa mtendere.

التفاسير:

external-link copy
135 : 3

وَٱلَّذِينَ إِذَا فَعَلُواْ فَٰحِشَةً أَوۡ ظَلَمُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ ذَكَرُواْ ٱللَّهَ فَٱسۡتَغۡفَرُواْ لِذُنُوبِهِمۡ وَمَن يَغۡفِرُ ٱلذُّنُوبَ إِلَّا ٱللَّهُ وَلَمۡ يُصِرُّواْ عَلَىٰ مَا فَعَلُواْ وَهُمۡ يَعۡلَمُونَ

Ndi amene amati akachita uve (wamachimo), kapena kudzichitira okha zoipa, amakumbukira Allah nampempha chikhululuko pa machimo awo. Kodi ndindani angakhululuke machimo kupatula Allah; ndipo napanda kupitiriza machimo omwe achita uku akudziwa. info
التفاسير:

external-link copy
136 : 3

أُوْلَٰٓئِكَ جَزَآؤُهُم مَّغۡفِرَةٞ مِّن رَّبِّهِمۡ وَجَنَّٰتٞ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ وَنِعۡمَ أَجۡرُ ٱلۡعَٰمِلِينَ

Iwowo mphoto yawo ndi chikhululuko chochokera kwa Mbuye wawo, ndi minda yoyenda mitsinje pansi pake (ndi patsogolo pake), momwe akakhalamo nthawi yaitali. Taonani kukoma malipiro a ochita zabwino. info
التفاسير:

external-link copy
137 : 3

قَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِكُمۡ سُنَنٞ فَسِيرُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَٱنظُرُواْ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُكَذِّبِينَ

Zidapita njira za zilango zambiri zosiyanasiyana zomwe adapatsidwa amene adalipo patsogolo panu. Tero tayendani pa dziko ndi kuona momwe adalili mapeto a anthu otsutsa. info
التفاسير:

external-link copy
138 : 3

هَٰذَا بَيَانٞ لِّلنَّاسِ وَهُدٗى وَمَوۡعِظَةٞ لِّلۡمُتَّقِينَ

Uku ndi kulengeza poyera kwa anthu (onse); komanso chiongoko ndi ulaliki kwa (anthu) oopa Allah! info
التفاسير:

external-link copy
139 : 3

وَلَا تَهِنُواْ وَلَا تَحۡزَنُواْ وَأَنتُمُ ٱلۡأَعۡلَوۡنَ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ

Ndipo musafooke (pomenya nkhondo), ndiponso musadandaule (ndi mavuto amene akupezani) pakuti ndinu apamwamba, ngati mulidi okhulupirira. info
التفاسير:

external-link copy
140 : 3

إِن يَمۡسَسۡكُمۡ قَرۡحٞ فَقَدۡ مَسَّ ٱلۡقَوۡمَ قَرۡحٞ مِّثۡلُهُۥۚ وَتِلۡكَ ٱلۡأَيَّامُ نُدَاوِلُهَا بَيۡنَ ٱلنَّاسِ وَلِيَعۡلَمَ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَيَتَّخِذَ مِنكُمۡ شُهَدَآءَۗ وَٱللَّهُ لَا يُحِبُّ ٱلظَّٰلِمِينَ

Ngati mwavulazidwa, naonso anthuwo avulazidwanso molingana. Ndipo amenewo ndimasiku, timawapatsa anthu mosinthanasinthana. (Ichi chachitika) kuti Allah aonetse poyera amene akhulupirira (moona; choncho sadathawe konse); ndi kuti awachite ena mwa inu kukhala Shuhadaa (ofera pankhondo yoyera). Komatu Allah sakonda anthu ochita zoipa.[89] info

[89] M’ndime iyi Allah akukumbutsa Asilamu zinthu zosowetsa mtendere zomwe zidawapeza m’masiku a Uhudi powauza kuti monga iwo adavutitsidwa ndi adani awo, nawonso adaniwo adavutitsidwa. Umo ndi momwe zinthu zimachitikira mosinthasintha. Nthawi zina zigwera awa, kenako zigwera ena, malinga ndi zochita zawo. Allah sakondera.

التفاسير: