وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - خالد ئیبراهيم بيتالا

ژمارەی پەڕە:close

external-link copy
95 : 4

لَّا يَسۡتَوِي ٱلۡقَٰعِدُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ غَيۡرُ أُوْلِي ٱلضَّرَرِ وَٱلۡمُجَٰهِدُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡۚ فَضَّلَ ٱللَّهُ ٱلۡمُجَٰهِدِينَ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ عَلَى ٱلۡقَٰعِدِينَ دَرَجَةٗۚ وَكُلّٗا وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡحُسۡنَىٰۚ وَفَضَّلَ ٱللَّهُ ٱلۡمُجَٰهِدِينَ عَلَى ٱلۡقَٰعِدِينَ أَجۡرًا عَظِيمٗا

Sangafanane okhulupirira omwe akukhala osapita kunkhondo pomwe sali ovutika, ndi amene akumenya nkhondo yoyera pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo. Allah wawatukula pa ubwino ndi pa nyota amene akuchita Jihâd ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo kuposa okhala. Koma onsewo Allah wawalonjeza zabwino. Koma wawapambanitsa ochita Jihâd malipiro aakulu kuposa ongokhala. info
التفاسير:

external-link copy
96 : 4

دَرَجَٰتٖ مِّنۡهُ وَمَغۡفِرَةٗ وَرَحۡمَةٗۚ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمًا

Adzapata nyota zazikulu zochokera kwa Iye ndi chikhululuko ndi chisoni. Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi. info
التفاسير:

external-link copy
97 : 4

إِنَّ ٱلَّذِينَ تَوَفَّىٰهُمُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ ظَالِمِيٓ أَنفُسِهِمۡ قَالُواْ فِيمَ كُنتُمۡۖ قَالُواْ كُنَّا مُسۡتَضۡعَفِينَ فِي ٱلۡأَرۡضِۚ قَالُوٓاْ أَلَمۡ تَكُنۡ أَرۡضُ ٱللَّهِ وَٰسِعَةٗ فَتُهَاجِرُواْ فِيهَاۚ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَسَآءَتۡ مَصِيرًا

Ndithudi amene angelo atenga miyoyo yawo, ali odzichitira okha zoipa (posasamuka ku Makka), adzawauza kuti: “Mudachitanji (pachipembedzo chanu?)” Iwo adzati: “Tidali ofooka ndi oponderezedwa padziko; (choncho sitidathe kuchita mapemphero athu).” (Angelo) adzati: “Kodi dziko la Allah silidali lotambasuka kotero kuti inu nkusamukira kwina m’menemo?” Iwowo malo awo ndi Jahannam. Taonani kuipa kwa malo obwerera.[136] info

[136] (Ndime 97-99) Kalelo Mtumiki (s.a.w) atasamukira ku Madina pamodzi ndi omtsatira ake, Asilamu adawalamula kuti asamukire ku Madinako kusiya nyumba zawo, chuma chawo, abale awo ndi ana awo. Izi zidali chonchi chifukwa iwo akanakhalabe m’midzi yawo pansi pautsogoleri wa anthu osakhulupilira sakanatha kukwaniritsa malamulo a Chisilamu. Tero Chisilamu chake sichikanakhala ndi ntchito. Ndipo Chisilamu chopanda ntchito si Chisilamunso. Tero nchifukwa chake apa akuwadzudzula amene sanasamuke kuti adzafa ndi imfa yoipa kupatula okhawo amene sanapeze njira yosamukira ku Madina chifukwa chakufooka kwa matupi awo. Amenewa madandaulo awo akhoza kuwavomera. Koma chachikulu nkuti ayesetse kusamukira ku Madina.

التفاسير:

external-link copy
98 : 4

إِلَّا ٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلرِّجَالِ وَٱلنِّسَآءِ وَٱلۡوِلۡدَٰنِ لَا يَسۡتَطِيعُونَ حِيلَةٗ وَلَا يَهۡتَدُونَ سَبِيلٗا

Kupatula omwe adali ofooka kwenikweni amuna, akazi ndi ana omwe sangathe kuchita ndale yamtundu uliwonse, ndipo sangathe kulondola njira (yonkera ku Madina). info
التفاسير:

external-link copy
99 : 4

فَأُوْلَٰٓئِكَ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَعۡفُوَ عَنۡهُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَفُوًّا غَفُورٗا

Choncho iwo ndithudi Allah angawafafanizire machimo, pakuti Allah Ngofafaniza machimo, Wokhululuka. info
التفاسير:

external-link copy
100 : 4

۞ وَمَن يُهَاجِرۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ يَجِدۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُرَٰغَمٗا كَثِيرٗا وَسَعَةٗۚ وَمَن يَخۡرُجۡ مِنۢ بَيۡتِهِۦ مُهَاجِرًا إِلَى ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ ثُمَّ يُدۡرِكۡهُ ٱلۡمَوۡتُ فَقَدۡ وَقَعَ أَجۡرُهُۥ عَلَى ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا

Ndipo amene angasamuke pa njira ya Allah (chifukwa cha chipembedzo chake,) apeza malo ambiri m’dzikomo othawira ndikupeza bwino. Ndipo amene angatuluke m’nyumba mwake kuti asamuke chifukwa cha Allah ndi Mtumiki Wake, kenako nkumpeza imfa (m’njira), ndithu malipiro ake atsimikizika kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[137] info

[137] Apa akuwalimbikitsa za kusamuka ndi kuwauza kuti kumene akupitako akapeza bwino. Akuwalimbikitsanso okalamba ndi odwala kuti asamuke. Ngati atafera pa njira kuwerengedwa kuti adasamukabe ndipo adzapeza mphoto yonga ya yemwe adasamuka nkukakhala ku Madina pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kukathandiza kukamenya nkhondo yoteteza Chisilamu kwa adani. Ndichimodzomodzi munthu akapita ku Makka kukachita Hajj ndipo nkumwalira Hajjiyo asanachite, kapena asanamalize zina zofunika pa Hajj, kwa Allah amamuwerenga kuti wachita mapemphero a Hajj. Komabe abale ake akhoza kukamchitiranso mapemphero a Hajj.

التفاسير:

external-link copy
101 : 4

وَإِذَا ضَرَبۡتُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَلَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٌ أَن تَقۡصُرُواْ مِنَ ٱلصَّلَوٰةِ إِنۡ خِفۡتُمۡ أَن يَفۡتِنَكُمُ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْۚ إِنَّ ٱلۡكَٰفِرِينَ كَانُواْ لَكُمۡ عَدُوّٗا مُّبِينٗا

Ndipo ngati mukuyenda pa dziko, sikulakwa kwa inu kufupikitsa Swala ngati mukuopa kuti angakusokonezeni omwe sadakhulupirire. Ndithudi, osakhulupirira ndi adani anu oonekera.[138] info

[138] Pamene Asilamu adawalamulira zakusamuka, adawafupikitsira Swala chifukwa cha mavuto am’njira monga kuti (a) Swala zokhala ndi raka zinayi akhoza kuziswali ndi raka ziwiriziwiri. (b) Akhoza kuswali katatu kokha patsiku m’malo mwakasanu. Izi zili motere: Swala ya Dhuhr nkuiphatikiza pamodzi ndi Swala ya Asr; kuzipemphera panthawi ya Dhuhr kapena kuzipemphera panthawi ya Asr. Swala ya Maghrib nkuipemphera pamodzi ndi Swala ya Isha. Adzayamba kupemphera Swala ya Maghrib raka zitatu kenako nkupemphera Isha raka ziwiri. Koma Swala ya Subh yokha njomwe imapempheredwa payokha ndiponso m’nthawi yake. Lamuloli analikhazikitsa pamene Asilamu adali ndi mantha ndi masautso am’njira. Ndipo lidasiidwa momwemo losasinthika mpaka lero m’nthawi yomwe anthu akukwera galimoto, sitima ndi ndege.

التفاسير: