وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - خالد ئیبراهيم بيتالا

ژمارەی پەڕە:close

external-link copy
135 : 4

۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُونُواْ قَوَّٰمِينَ بِٱلۡقِسۡطِ شُهَدَآءَ لِلَّهِ وَلَوۡ عَلَىٰٓ أَنفُسِكُمۡ أَوِ ٱلۡوَٰلِدَيۡنِ وَٱلۡأَقۡرَبِينَۚ إِن يَكُنۡ غَنِيًّا أَوۡ فَقِيرٗا فَٱللَّهُ أَوۡلَىٰ بِهِمَاۖ فَلَا تَتَّبِعُواْ ٱلۡهَوَىٰٓ أَن تَعۡدِلُواْۚ وَإِن تَلۡوُۥٓاْ أَوۡ تُعۡرِضُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا

E inu amene mwakhulupirira! Khalani oimiritsa chilungamo, opereka umboni chifukwa cha Allah; ngakhale kuti ubwere ndi masautso kwa inu, kapena kwa makolo anu, kapena kwa abale anu, ngakhale ali olemera kapena osauka, (musayang’ane zimenezo). Allah ndiye woyenera kuyang’ana za awiriwo. Choncho musatsate zilakolako ndi kusiya chilungamo. Ngati mukhotetsa (umboni), kapena kupewa (kupereka umboni) ndithudi nkhani zonse zomwe mukuchita Allah akuzidziwa. info
التفاسير:

external-link copy
136 : 4

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ ءَامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلَّذِي نَزَّلَ عَلَىٰ رَسُولِهِۦ وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلَّذِيٓ أَنزَلَ مِن قَبۡلُۚ وَمَن يَكۡفُرۡ بِٱللَّهِ وَمَلَٰٓئِكَتِهِۦ وَكُتُبِهِۦ وَرُسُلِهِۦ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا

E inu amene mwakhulupirira! Khulupirirani Allah ndi Mtumiki Wake, ndi buku lomwe analivumbulutsa pa Mtumiki Wake, ndi mabuku omwe adawavumbulutsa kale. Ndipo amene akane Allah, angelo Ake, mabuku Ake, atumiki Ake ndi tsiku lachimaliziro, ndiye kuti wasokera; kusokera konkera nako kutali. info
التفاسير:

external-link copy
137 : 4

إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ ثُمَّ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ ثُمَّ ٱزۡدَادُواْ كُفۡرٗا لَّمۡ يَكُنِ ٱللَّهُ لِيَغۡفِرَ لَهُمۡ وَلَا لِيَهۡدِيَهُمۡ سَبِيلَۢا

Ndithudi, amene adakhulupirira, kenako nkusakhulupirira, nadzakhulupiriranso, kenako nkusakhulupiriranso, naonjezera kusakhulupirira, Allah sadzawakhululukira, ndipo sadzawawongolera m’njira (yabwino). info
التفاسير:

external-link copy
138 : 4

بَشِّرِ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ بِأَنَّ لَهُمۡ عَذَابًا أَلِيمًا

Auze achiphamaso kuti adzapeza chilango chowawa. info
التفاسير:

external-link copy
139 : 4

ٱلَّذِينَ يَتَّخِذُونَ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ أَيَبۡتَغُونَ عِندَهُمُ ٱلۡعِزَّةَ فَإِنَّ ٱلۡعِزَّةَ لِلَّهِ جَمِيعٗا

Omwe amaachita osakhulupirira kukhala abwenzi awo kusiya Asilamu. Kodi akufuna kupeza ulemelero kwa iwo? Ndithudi ulemelero wonse ngwa Allah; (suli m’manja mwa anthu). info
التفاسير:

external-link copy
140 : 4

وَقَدۡ نَزَّلَ عَلَيۡكُمۡ فِي ٱلۡكِتَٰبِ أَنۡ إِذَا سَمِعۡتُمۡ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ يُكۡفَرُ بِهَا وَيُسۡتَهۡزَأُ بِهَا فَلَا تَقۡعُدُواْ مَعَهُمۡ حَتَّىٰ يَخُوضُواْ فِي حَدِيثٍ غَيۡرِهِۦٓ إِنَّكُمۡ إِذٗا مِّثۡلُهُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ جَامِعُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡكَٰفِرِينَ فِي جَهَنَّمَ جَمِيعًا

Ndithudi Iye wakuvumbulutsirani m’buku (ili) kuti mukamva ma Ayah (ndime) a Allah akukanidwa ndi kuchitiridwa chipongwe, musakhale pamodzi nawo mpaka alowe m’zokamba zina. (Ngati mutakhala nawo) ndiye kuti mukhala chimodzimodzi ndi iwo. Ndithudi, Allah adzawasonkhanitsa achiphamaso ndi osakhulupirira onse m’moto wa Jahannam. info
التفاسير: