আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

পৃষ্ঠা নং:close

external-link copy
34 : 4

ٱلرِّجَالُ قَوَّٰمُونَ عَلَى ٱلنِّسَآءِ بِمَا فَضَّلَ ٱللَّهُ بَعۡضَهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ وَبِمَآ أَنفَقُواْ مِنۡ أَمۡوَٰلِهِمۡۚ فَٱلصَّٰلِحَٰتُ قَٰنِتَٰتٌ حَٰفِظَٰتٞ لِّلۡغَيۡبِ بِمَا حَفِظَ ٱللَّهُۚ وَٱلَّٰتِي تَخَافُونَ نُشُوزَهُنَّ فَعِظُوهُنَّ وَٱهۡجُرُوهُنَّ فِي ٱلۡمَضَاجِعِ وَٱضۡرِبُوهُنَّۖ فَإِنۡ أَطَعۡنَكُمۡ فَلَا تَبۡغُواْ عَلَيۡهِنَّ سَبِيلًاۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيّٗا كَبِيرٗا

Amuna ndiayang’aniri pa akazi chifukwa choti Allah watukula ena pa ulemelero pamwamba pa ena, chifukwa cha chuma chawo chimene apereka. Choncho, akazi abwino ndi omwe ali omvera, odzisunga ngakhale amuna awo palibe pakuti Allah wawalamula kudzisunga. Ndipo akazi omwe mukuopa mnyozo wawo, achenjezeni; ndipo kenako achokereni pamphasa, (apo ayi), akwapuleni (kukwapula kosavulaza), koma ngati akukumverani, musawafunire njira yowavutitsira. Ndithu Allah ndi yemwe ali Wapamwamba, Wamkulu (kuposa inu nonse).[122] info

[122] Apa akuti amuna ndi amene akhale ndi ulamuliro pa akazi awo, powatsogolera ku miyambo yabwino. Osati kuti mkazi adzitukumule kwa mwamuna wake poti iye ngophunzira zedi kapena wanzeru zochuluka kotero kuti mwamuna m’nyumba osamuyesa kanthu. Ngati atero ndiye kuti sakhala Asilamu owona. M’ndimeyi atchulamonso makhalidwe ofunika kuti akazi akhale nawo. Ndipo atchulamo malangizo olangira nawo mkazi ngati samvera. Choyamba amchenjeze ndi mawu. Ngati kuchenjezako sikunathandize, asagone naye limodzi pamphasa. Ndipo ngati akupitirizabe kuchita mnyozo akupatsidwa chilolezo mwamuna kuti amlange pommenya mwakumuopyeza, osati kumenya komgulula nako mano. Komabe mahadisi a Mtumiki (s.a.w) akunena kuti asanaganize zommenya ayeseyese kumkonza ponena naye mofewa ndi kumuonetsa kulakwa kwake. Ngati atalephera zonsezi, aitane anthu kuti adzawayanjanitse m’njira yabwino. Naonso anthuwo akhale ndi cholinga choyanjanitsa osati kupasula. Amunanso akuwachenjeza apa kuti iwo ndi amene ali ndi nyonga ndi udindo. Allah ndiye Wamkulu kuposa iwo amunawo. Mawu oti “Hafizatu Lilighaibi” maulama ena akuwatanthauzira kuti “Akhale osunga chinsinsi,” chimene chili pakati pa iwo ndi amuna awo ndi zonse zomwe zimachitika m’nyumba, pakuti nthawi zambiri akazi sakhalira kuulula za m’nyumba.

التفاسير:

external-link copy
35 : 4

وَإِنۡ خِفۡتُمۡ شِقَاقَ بَيۡنِهِمَا فَٱبۡعَثُواْ حَكَمٗا مِّنۡ أَهۡلِهِۦ وَحَكَمٗا مِّنۡ أَهۡلِهَآ إِن يُرِيدَآ إِصۡلَٰحٗا يُوَفِّقِ ٱللَّهُ بَيۡنَهُمَآۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا خَبِيرٗا

Ndipo (inu aweruzi) ngati muopa mkangano pakati pawo (pa mwamuna ndi mkazi wake), tumizani nkhoswe ya kuchimuna ndi nkhoswe ya kuchikazi. Ngati iwo atafuna kuyanjanitsa, Allah awapatsa mphamvu zoyanjanitsira pakati pawo (okanganawo). Allah Ngodziwa nkhani zobisika, ndiponso Ngodziwa nkhani zoonekera. info
التفاسير:

external-link copy
36 : 4

۞ وَٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ وَلَا تُشۡرِكُواْ بِهِۦ شَيۡـٔٗاۖ وَبِٱلۡوَٰلِدَيۡنِ إِحۡسَٰنٗا وَبِذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱلۡجَارِ ذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡجَارِ ٱلۡجُنُبِ وَٱلصَّاحِبِ بِٱلۡجَنۢبِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِ وَمَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ مَن كَانَ مُخۡتَالٗا فَخُورًا

Ndipo mpembedzeni Allah, ndipo musamphatikize ndi chilichonse; ndipo achitireni zabwino makolo awiri, ndi achibale, ndi ana amasiye ndi masikini ndi mnansi woyandikana naye nyumba, ndi wapadera wogundizana naye nyumba, ndi mnzako wokhala naye limodzi, ndi wapaulendo yemwe alibe choyendera, ndi omwe manja anu akumanja apeza (adzakazi). Ndithudi, Allah sakonda wodzitukumula ndi wodzitama.[123] info

[123] M’ndime iyi akuwalamula anthu kuti apembedze Allah yekha ndi kumpempha Iye Yekha. Asapembedzenso china chilichonse, chamoyo kapena chakufa. Ndikuti awachitire zabwino makolo ake ndi onse amene awatchula m’ndimeyi. Sibwino kuthandiza anthu akumbali pomwe anthu omwe uli nawo pafupi sunawathandizepo.

التفاسير:

external-link copy
37 : 4

ٱلَّذِينَ يَبۡخَلُونَ وَيَأۡمُرُونَ ٱلنَّاسَ بِٱلۡبُخۡلِ وَيَكۡتُمُونَ مَآ ءَاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦۗ وَأَعۡتَدۡنَا لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا

Omwe amachita umbombo ndi kulamula anthu kuchita umbombo ndi kubisa zabwino zomwe Allah wawapatsa. Komatu osakhulupirira tawakonzera chilango choyalutsa.[124] info

[124] Kubisa zonse zomwe Allah wawapatsa kuli monga munthu kukhala ndi maphunziro koma osaphunzitsa anthu kotero kuti nkufa nawo popanda kuphunzitsapo aliyense. Kutero sibwino. Koma akafuna kukalowa m’Munda wa mtendere wa Allah nkofunika kuti achite zinthu zabwino ncholinga chokondweretsa Allah. Osati kuti anthu amuone ndi kumtama. Amene akuchita chinthu chabwino ncholinga choti anthu amtamande, sakalandira mphoto iliyonse pa tsiku lachimaliziro.

التفاسير: