আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

পৃষ্ঠা নং:close

external-link copy
52 : 4

أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ لَعَنَهُمُ ٱللَّهُۖ وَمَن يَلۡعَنِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ نَصِيرًا

Iwo ndi omwe Allah wawatembelera. Ndipo amene Allah wamtembelera, simungathe kumpezera wompulumutsa. info
التفاسير:

external-link copy
53 : 4

أَمۡ لَهُمۡ نَصِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُلۡكِ فَإِذٗا لَّا يُؤۡتُونَ ٱلنَّاسَ نَقِيرًا

Kodi ali ndi gawo la ufumu (wa Allah? Nchifukwa ninji akunyasidwa munthu wina akaninkhidwa utumiki)? Zikadatero ndiye kuti sakadawapatsa anthu ngakhale kochepa kwambiri monga khokho la tende.[128] info

[128] Ndime 53-54 zikusonyeza kuti zonse zimene Ayuda ankawachitira Asilamu nchifukwa chadumbo basi. Ankawawidwa nawo mitima chifukwa choti Asilamu apeza chisomo cha Allah. Palibe chinthu chimene chimaletsa anthu kutsata choonadi kuposa dumbo. Ngati utamchitira dumbo munthu sungalole kutsata langizo lake lililonse ngakhale litakhala lopindulitsa pano pa dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro Dumbo ndi lomwe likuletsa anthu ambiri kutsata choonadi. Choncho tiyeni tipewe khalidwe limeneli kuti titsatire choonadi paliponse pamene chachokera. Ndikutinso tipeze mtendere m’mitima mwathu. Dziwani kuti dumbo nlomwe lidamchititsa Iblis kukhala wotembeleredwa.

التفاسير:

external-link copy
54 : 4

أَمۡ يَحۡسُدُونَ ٱلنَّاسَ عَلَىٰ مَآ ءَاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦۖ فَقَدۡ ءَاتَيۡنَآ ءَالَ إِبۡرَٰهِيمَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَءَاتَيۡنَٰهُم مُّلۡكًا عَظِيمٗا

Kodi akuchitira anthu dumbo pa zomwe Allah wawapatsa ndi ufulu wake? Choncho tidalipatsa banja la Ibrahim buku ndi nzeru. Ndipo tidawapatsa ufumu waukulu. info
التفاسير:

external-link copy
55 : 4

فَمِنۡهُم مَّنۡ ءَامَنَ بِهِۦ وَمِنۡهُم مَّن صَدَّ عَنۡهُۚ وَكَفَىٰ بِجَهَنَّمَ سَعِيرًا

Choncho alipo ena mwa iwo amene anazikhulupirira izi, ndiponso alipo ena mwa iwo omwe adziika nazo kutali. Ndipo Jahannam ikukwanira kukhala Moto waukali wowatentha. info
التفاسير:

external-link copy
56 : 4

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا سَوۡفَ نُصۡلِيهِمۡ نَارٗا كُلَّمَا نَضِجَتۡ جُلُودُهُم بَدَّلۡنَٰهُمۡ جُلُودًا غَيۡرَهَا لِيَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَزِيزًا حَكِيمٗا

Ndithu amene sadakhulupirire zizindikiro Zathu, tidzawalowetsa ku Moto. Nthawi iliyonse yomwe makungu awo adzikapselera tidzidzawasinthira makungu ena kuti adzapitirize kulawa chilango. Ndithudi, Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.[129] info

[129] (Ndime 56-57) Apa akutchula za malipiro a anthu ochita zabwino ndi malipiro a anthu ochita zoipa umu ndi momwe ulili ulaliki wa Qur’an. Qur’an ikafotokoza za anthu ochita zoipa imatsatiza pompo kufotokoza zotsatira za anthu ochita zabwino. Pamenepa akunena kuti aliyense adzalandira malipiro a zochita zake, abwino kapena oipa. Sakawomboledwa chifukwa cha ubwino wa munthu wina. Zochita zake ndizo zikamuombola kapena kukamponya kuchionongeko.

التفاسير:

external-link copy
57 : 4

وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ سَنُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ لَّهُمۡ فِيهَآ أَزۡوَٰجٞ مُّطَهَّرَةٞۖ وَنُدۡخِلُهُمۡ ظِلّٗا ظَلِيلًا

Ndipo amene akhulupirira ndi kuchita zabwino, Tidzawalowetsa m’minda momwe mitsinje ikuyenda pansi (ndi patsogolo) pake. Adzakhala mmenemo muyaya. Ndipo iwo adzapeza mmenemo akazi oyeretsedwa (ku uve wamtundu uliwonse) ndi kuwalowetsa ku mithunzi yabwino kwambiri. info
التفاسير:

external-link copy
58 : 4

۞ إِنَّ ٱللَّهَ يَأۡمُرُكُمۡ أَن تُؤَدُّواْ ٱلۡأَمَٰنَٰتِ إِلَىٰٓ أَهۡلِهَا وَإِذَا حَكَمۡتُم بَيۡنَ ٱلنَّاسِ أَن تَحۡكُمُواْ بِٱلۡعَدۡلِۚ إِنَّ ٱللَّهَ نِعِمَّا يَعِظُكُم بِهِۦٓۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ سَمِيعَۢا بَصِيرٗا

Ndithudi, Allah akukulamulani kubweza kwa eni zomwe mwakhulupirika nazo. Ndipo pamene mukuweruza pakati pa anthu, weruzani mwachilungamo. Ndithu malangizo amene Allah akukulangizani, ngabwino kwambiri. Ndithudi, Allah Ngwakumva, Ngoona.[130] info

[130] Pali anthu ena amene amati anzawo akawasungitsa zinthu kuti akhulupirike pa zimenezo, mwini zinthu uja akafa kapena kuti panalibe umboni wokwanira, amazitenga zinthuzo poganizira kuti palibe chomwe chingawavute popeza mwini zinthuzo adamwalira ndipo umboni wokwanira palibe. Chikhalidwe chotere si cha Chisilamu, Chisilamu sichifuna machitidwe otere.

التفاسير:

external-link copy
59 : 4

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَ وَأُوْلِي ٱلۡأَمۡرِ مِنكُمۡۖ فَإِن تَنَٰزَعۡتُمۡ فِي شَيۡءٖ فَرُدُّوهُ إِلَى ٱللَّهِ وَٱلرَّسُولِ إِن كُنتُمۡ تُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ ذَٰلِكَ خَيۡرٞ وَأَحۡسَنُ تَأۡوِيلًا

E inu amene mwakhulupirira! Mumvereni Allah ndiponso mumvereni Mtumiki, ndi omwe ali ndi udindo pa inu. Ngati Mutatsutsana pa chinthu chilichonse, chibwezeni kwa Allah ndi Mtumiki Wake, ngatidi mukukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, kutero ndibwino; ndipo zotere zili ndi zotsatira zabwino.[131] info

[131] Aliyense amene amdzoza utsogoleri nkofunika kuti anthu amumvere ngati iye akulamula zabwino. Pagulu la anthu ngati sipakhala mtsogoleri womumvera, ndiye kuti pamapezeka zisokonezo ndi ziwawa kotero kuti zinthu zawo siziyenda bwino. Chisilamu sichiloleza machitidwe achipolowe ndi ziwawa. Chisilamu chimakonda bata ndi mtendere ndi kuti pasapezeke anthu ena owachenjelera anzawo. Komatu atsogoleriwo awamvere akalamula mwa chilungamo popanda kulakwira Allah. Koma ngati akulakwira Allah asawamvere. Pamenepo atsate chomwe Allah wawalamula ndi Mtumiki Wake.

التفاسير: