[347] Arabu adali ndi chizolowezi chakupatukana ndi mkazi ponena mawu akuti: “Ndikukuyerekeza ngati mayi wanga.” Choncho amangokhala naye mkazi uja, osamkhudza ndiponso osamulola kuti akwatiwe ndi mwamuna wina. Samamchitiranso zimene munthu amachitira mkazi wake monga kumveka ndi kumdyetsa. Msilamu wina adamsiya mkazi masiyidwe onga amenewa ndipo mkazi uja adapita kukakambirana naye Mtumiki (s.a.w). Choncho Chisilamu chidaletsa machitidwe onga amenewa.