Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Al-Morsalaat   Vers:

Al-Mursalât

وَٱلۡمُرۡسَلَٰتِ عُرۡفٗا
Ndikulumbilira mphepo yomwe ikuomba motsatizana.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَٱلۡعَٰصِفَٰتِ عَصۡفٗا
Ndi mphepo yamkuntho ikamakuntha.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلنَّٰشِرَٰتِ نَشۡرٗا
Ndi mphepo yobalalitsa mitambo ndi mvula.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَٱلۡفَٰرِقَٰتِ فَرۡقٗا
Ndi ma Ayah osiyanitsa pakati pachoona ndi chonama;
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَٱلۡمُلۡقِيَٰتِ ذِكۡرًا
Ndi angelo opereka chivumbulutso kwa aneneri.
Arabische uitleg van de Qur'an:
عُذۡرًا أَوۡ نُذۡرًا
Kuti chichotse madandaulo kapena chikhale chenjezo;
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّمَا تُوعَدُونَ لَوَٰقِعٞ
Ndithu zimene mukulonjezedwa (kuti chimaliziro chidzakhalapo) zidzachitikadi (popanda chipeneko),
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَإِذَا ٱلنُّجُومُ طُمِسَتۡ
Pamene nyenyezi zidzafafanizidwa (kuwala kwake ndi kuchotsedwa m’malo mwake).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ فُرِجَتۡ
Ndiponso pamene thambo lidzang‘ambidwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ نُسِفَتۡ
Ndi pamenenso mapiri adzachotsedwa m’malo mwake ndi kuperedwa (kukhala fumbi).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِذَا ٱلرُّسُلُ أُقِّتَتۡ
Ndi pamene atumiki adzasonkhanitsidwa pa nthawi yake, (kuti apereke umboni ku mibadwo yawo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِأَيِّ يَوۡمٍ أُجِّلَتۡ
Kodi nditsiku lanji azichedwetsera (zinthu zikuluzikulu kuti zidzachitike)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِيَوۡمِ ٱلۡفَصۡلِ
Nditsiku loweruza (pakati pa zolengedwa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِ
Nchiyani chingakudziwitse za tsiku la chiweruzirolo?
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَلَمۡ نُهۡلِكِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Kodi sitidawaononge (anthu) akale (chifukwa cha machimo awo, monga anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ نُتۡبِعُهُمُ ٱلۡأٓخِرِينَ
Kenako titsatiza ena (okana Allah m’kuonongekako monga tidawachitira oyamba),
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَذَٰلِكَ نَفۡعَلُ بِٱلۡمُجۡرِمِينَ
Chomwecho tiwachitiranso ochimwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Al-Morsalaat
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala - Index van vertaling

Vertaald door Khalid Ibrahim Bitala.

Sluit