Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Khalid Ibrahim Betyala

Numero di pagina:close

external-link copy
52 : 7

وَلَقَدۡ جِئۡنَٰهُم بِكِتَٰبٖ فَصَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ عِلۡمٍ هُدٗى وَرَحۡمَةٗ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ

Ndithudi, tawabweretsera buku lomwe talifotokoza mwanzeru, lomwe ndichiongoko ndi chifundo kwa anthu okhulupirira. info
التفاسير:

external-link copy
53 : 7

هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّا تَأۡوِيلَهُۥۚ يَوۡمَ يَأۡتِي تَأۡوِيلُهُۥ يَقُولُ ٱلَّذِينَ نَسُوهُ مِن قَبۡلُ قَدۡ جَآءَتۡ رُسُلُ رَبِّنَا بِٱلۡحَقِّ فَهَل لَّنَا مِن شُفَعَآءَ فَيَشۡفَعُواْ لَنَآ أَوۡ نُرَدُّ فَنَعۡمَلَ غَيۡرَ ٱلَّذِي كُنَّا نَعۡمَلُۚ قَدۡ خَسِرُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ وَضَلَّ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يَفۡتَرُونَ

Kodi chiliponso chomwe akudikilira osati zotsatira zake (za bukulo)? Ndipo tsiku lakudza zotsatira zake, adzanena amene kale sadalilabadire: “Ha! Atumiki a Mbuye wathu adadzadi ndi choonadi (tsopano tikuvomereza). Kodi tingakhale nawo ife aomboli oti atiombole (kwa Mbuye wathu), kapena tingabwezedwe kuti tikachite (zabwino) osati zija tinkachita?” Zoonadi adziononga okha, ndipo zawasowa zabodza zomwe adali kupeka. info
التفاسير:

external-link copy
54 : 7

إِنَّ رَبَّكُمُ ٱللَّهُ ٱلَّذِي خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ فِي سِتَّةِ أَيَّامٖ ثُمَّ ٱسۡتَوَىٰ عَلَى ٱلۡعَرۡشِۖ يُغۡشِي ٱلَّيۡلَ ٱلنَّهَارَ يَطۡلُبُهُۥ حَثِيثٗا وَٱلشَّمۡسَ وَٱلۡقَمَرَ وَٱلنُّجُومَ مُسَخَّرَٰتِۭ بِأَمۡرِهِۦٓۗ أَلَا لَهُ ٱلۡخَلۡقُ وَٱلۡأَمۡرُۗ تَبَارَكَ ٱللَّهُ رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ

Ndithudi, Mbuye wanu ndi Allah Yemwe adalenga thambo ndi nthaka m’masiku asanu ndi limodzi. Kenako adakhazikika pa Arsh (Mpando Wake wachifumu). Amauchita usiku kuti uvindikire usana, zimatsatana mwamsangamsanga. Ndipo dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi nzofewetsedwa, (zikuyenda mogonjera) ndi Lamulo Lake. Dziwani kuti kulenga ndi kulamula Nkwake. Ndithudi, watukuka Allah Mbuye Wazolengedwa (zonse). info
التفاسير:

external-link copy
55 : 7

ٱدۡعُواْ رَبَّكُمۡ تَضَرُّعٗا وَخُفۡيَةًۚ إِنَّهُۥ لَا يُحِبُّ ٱلۡمُعۡتَدِينَ

Mpempheni Mbuye wanu modzichepetsa ndi mwakachetechete. Ndithu Iye sakonda opyola malire. info
التفاسير:

external-link copy
56 : 7

وَلَا تُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ بَعۡدَ إِصۡلَٰحِهَا وَٱدۡعُوهُ خَوۡفٗا وَطَمَعًاۚ إِنَّ رَحۡمَتَ ٱللَّهِ قَرِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ

Ndipo musaononge pa dziko pambuyo popakonza. Mpempheni (Allah) mwamantha ndi mwakhumbo. Ndithu chifundo cha Allah chili pafupi kwa (anthu Ake ) ochita zabwino.[184] info

[184] Chifundo cha Allah chimawafika anthu omwe amachitiranso chifundo anzawo. Ndipo amene sachitira anzawo chifundo sangapezenso chifundo cha Allah. Choncho tiyeni tilimbikire kuthandiza ofooka ndi osowa chithandizo. Ngati sititero ndiye kuti chifundo cha Allah chidzakhala kutali nafe.

التفاسير:

external-link copy
57 : 7

وَهُوَ ٱلَّذِي يُرۡسِلُ ٱلرِّيَٰحَ بُشۡرَۢا بَيۡنَ يَدَيۡ رَحۡمَتِهِۦۖ حَتَّىٰٓ إِذَآ أَقَلَّتۡ سَحَابٗا ثِقَالٗا سُقۡنَٰهُ لِبَلَدٖ مَّيِّتٖ فَأَنزَلۡنَا بِهِ ٱلۡمَآءَ فَأَخۡرَجۡنَا بِهِۦ مِن كُلِّ ٱلثَّمَرَٰتِۚ كَذَٰلِكَ نُخۡرِجُ ٱلۡمَوۡتَىٰ لَعَلَّكُمۡ تَذَكَّرُونَ

Ndipo Iye ndi Yemwe amatumiza mphepo kuti ikhale nkhani yosangalatsa patsogolo pa chifundo Chake (mvula), kufikira mphepoyo itasenza mitambo yolemera yomwe tikuitumiza ku dziko lakufa. Ndipo kupyolera mwa iyo tikutsitsa madzi ndipo ndimadzio tikutulutsa mitundu yonse ya zipatso. Momwemo ndimo tidzawaukitsira akufa. (Zonsezi) nkuti inu mukumbukire. [185] info

[185] Mmene Allah amaiukitsira nthaka youma ndi madzi amvula, nameretsa mmera wosiyanasiyana, momwemonso ndimo adzawaukitsira akufa. Palibe chimene chingamkanike.

التفاسير: