Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala

Broj stranice:close

external-link copy
106 : 4

وَٱسۡتَغۡفِرِ ٱللَّهَۖ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا

Ndipo mpemphe chikhululuko Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha. info
التفاسير:

external-link copy
107 : 4

وَلَا تُجَٰدِلۡ عَنِ ٱلَّذِينَ يَخۡتَانُونَ أَنفُسَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ مَن كَانَ خَوَّانًا أَثِيمٗا

Ndipo usawaikile kumbuyo omwe akudzichitira okha chinyengo. Allah sakonda yemwe ali wachinyengo, wamachimo. info
التفاسير:

external-link copy
108 : 4

يَسۡتَخۡفُونَ مِنَ ٱلنَّاسِ وَلَا يَسۡتَخۡفُونَ مِنَ ٱللَّهِ وَهُوَ مَعَهُمۡ إِذۡ يُبَيِّتُونَ مَا لَا يَرۡضَىٰ مِنَ ٱلۡقَوۡلِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِمَا يَعۡمَلُونَ مُحِيطًا

Akudzibisa kwa anthu (pochita za machimo) koma sakuzibisa kwa Allah pomwe Iye adali nawo pamodzi pamene adali kupangana usiku mawu osakondweretsa. Allah akudziwa bwinobwino zimene akuchita.[142] info

[142] Achiphamaso amabisa zochita zawo kwa anthu kuti asazione. Koma salabadira kuonedwa ndi Allah pomwe Allah Njemwe adzawalipira. Pomwe Allah akudziwa zonse zimene zikuyenda m’mitima mwawo ndiponso akumva ndi kuziona zonse zimene akuchita. Kunali kofunika kwa iwo kumuopa Allah amene ali ndi mphamvu zochitira chilichonse chimene wafuna.

التفاسير:

external-link copy
109 : 4

هَٰٓأَنتُمۡ هَٰٓؤُلَآءِ جَٰدَلۡتُمۡ عَنۡهُمۡ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا فَمَن يُجَٰدِلُ ٱللَّهَ عَنۡهُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ أَم مَّن يَكُونُ عَلَيۡهِمۡ وَكِيلٗا

Taonani! Inu ndi amene mwaayikira kumbuyo pa moyo wa pa dziko lapansi. Kodi ndani amene adzatsutsana ndi Allah pa iwo tsiku lachimaliziro, kapena ndani adzakhale mtetezi wawo.[143] info

[143] M’ndime iyi Allah akuletsa anthu kuti asakhalire kumbuyo anthu oipa koma awaleke kuti awalange chifukwa cha zoipa zawo ndi kuti amene adamuchitirapo zoipa apeze bwino muntima mwake. Choncho aweruzi amilandu achenjere kukhalira kumbuyo anthu oipa omwe ali nawo chitsimikizo kuti adachenjelera anzawo. Asaone ulemelero wa munthu mmene ulili ngakhale ali ndi chuma chotani. Koma m’malomwake akhalire kumbuyo amene ali oponderezedwa. Akatero adzapeza mphoto yomwe Allah walonjeza chifukwa cha kusonyeza choonadi poyera. Aweruzi akagwira njira imeneyi ndiye kuti adzapambana pano padziko lapansi mpaka patsiku la chiweruziro.

التفاسير:

external-link copy
110 : 4

وَمَن يَعۡمَلۡ سُوٓءًا أَوۡ يَظۡلِمۡ نَفۡسَهُۥ ثُمَّ يَسۡتَغۡفِرِ ٱللَّهَ يَجِدِ ٱللَّهَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا

Ndipo amene angachite choipa (povutitsa ena), kapena kudzichitira yekha zoipa, kenako nkupempha chikhululuko kwa Allah, adzampeza Allah ali Wokhululuka kwabasi, Wachisoni chosatha. [144] info

[144] Allah akuwalimbikitsa ochimwa: Kuti (a) atembenukire kwa Iye mwachangu ndi kusiya zimene akuchitazo. (b) Atsimikize mu mtima kuti sadzachitanso uchimowo. (c) Adandaule pa uchimo umene adauchitawo. (d) Awabwezere eni zinthu zomwe adazitenga mwachinyengo. (e) Akawapemphe kuti awakhululukire. Akakwaniritsa zonsezi ndiye kuti kulapa kwawo Allah akuvomera.

التفاسير:

external-link copy
111 : 4

وَمَن يَكۡسِبۡ إِثۡمٗا فَإِنَّمَا يَكۡسِبُهُۥ عَلَىٰ نَفۡسِهِۦۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا

Ndipo amene angachite tchimo, ndiye kuti akudzichitira yekha. Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.[145] info

[145] M’ndime iyi akuti munthu wochitira anthu anzake zoipa.akudzipha yekha pakuti Allah sadzamleka koma amkhaulitsa pompano pa dziko lapansi kapena pakutha kwa dziko.

التفاسير:

external-link copy
112 : 4

وَمَن يَكۡسِبۡ خَطِيٓـَٔةً أَوۡ إِثۡمٗا ثُمَّ يَرۡمِ بِهِۦ بَرِيٓـٔٗا فَقَدِ ٱحۡتَمَلَ بُهۡتَٰنٗا وَإِثۡمٗا مُّبِينٗا

Ndipo amene angachite cholakwa (chaching’ono) kapena tchimo (lalikulu) kenako nkumponyera nalo yemwe sadalakwe (momunamizira), ndithudi wasenza bodza lamkunkhuniza ndi uchimo woonekera.[146] info

[146] Pali anthu ena amene amaukwera uchimo. Kenako nkumnamizira wina wake. Munthu wamakhalidwe awa, chiweruzo chake chidzakhala choopsa tsiku lachimaliziro, ngakhale wadzipulumutsa pano pa dziko lapansi chifukwa chakuthyathyalika kwake. Kapena pompano pa dziko lapansi amachiona chomwe chinameta nkhanga mpala.

التفاسير:

external-link copy
113 : 4

وَلَوۡلَا فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ وَرَحۡمَتُهُۥ لَهَمَّت طَّآئِفَةٞ مِّنۡهُمۡ أَن يُضِلُّوكَ وَمَا يُضِلُّونَ إِلَّآ أَنفُسَهُمۡۖ وَمَا يَضُرُّونَكَ مِن شَيۡءٖۚ وَأَنزَلَ ٱللَّهُ عَلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَعَلَّمَكَ مَا لَمۡ تَكُن تَعۡلَمُۚ وَكَانَ فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ عَظِيمٗا

Ndipo pakadapanda ubwino wa Allah ndi chisoni chake pa iwe, ndithudi, gulu limodzi la iwo likadalinga kukusokeretsa. Ndipo iwo palibe yemwe akadamsokeretsa koma iwo okha basi. Ndipo sangathe kukuvutitsa ndi chilichonse. Ndipo Allah wakuvumbulutsira buku, kudzanso luntha. Ndipo wakuphunzitsa zomwe sudali kuzidziwa. Ndipo ubwino wa Allah umene uli pa iwe ngwaukulu zedi.[147] info

[147] Apa Allah akunena kuti palibe chisomo chimene Allah wapatsa munthu chachikulu ndi chopindulitsa kuposa luntha. Chilichonse chabwino cha pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro chimapezeka chifukwa cha kudziwa zinthu. Qur’an yonse ndi hadisi za Mtumiki zikulimbikitsa zakufunafuna luntha lodziwira zinthu zakuti zimkonzere munthu za dziko lapansi ndi za tsiku lachimaliziro, kotero kuti Qur’an ndi hadisizo zikunena kuti munthu apite kunja kunka nafunafuna maphunziro.

التفاسير: