Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ.

Ash-Sharh

external-link copy
1 : 94

أَلَمۡ نَشۡرَحۡ لَكَ صَدۡرَكَ

Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)? info
التفاسير:

external-link copy
2 : 94

وَوَضَعۡنَا عَنكَ وِزۡرَكَ

Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako). info
التفاسير:

external-link copy
3 : 94

ٱلَّذِيٓ أَنقَضَ ظَهۡرَكَ

Mtolo umene udalemetsa msana wako? info
التفاسير:

external-link copy
4 : 94

وَرَفَعۡنَا لَكَ ذِكۡرَكَ

Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455] info

[455] Allah wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina. Ndipo ndichopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola, ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa nyengo zonse ndi pamalo paliponse.

التفاسير:

external-link copy
5 : 94

فَإِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرًا

Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri). info
التفاسير:

external-link copy
6 : 94

إِنَّ مَعَ ٱلۡعُسۡرِ يُسۡرٗا

Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri). info
التفاسير:

external-link copy
7 : 94

فَإِذَا فَرَغۡتَ فَٱنصَبۡ

Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456] info

[456] Tanthauzo lake nkuti: “Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe Allah wakutuma kuti ulalikire, chita mapemphero ambiri. Umthokoze Mbuye wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho.” Mneneri (s.a.w) adali kulimbikira kwambiri pochita mapemphero mwakuti amaima ndi kumapemphera kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.

التفاسير:

external-link copy
8 : 94

وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرۡغَب

Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako. info
التفاسير: