আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

পৃষ্ঠা নং:close

external-link copy
260 : 2

وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّ أَرِنِي كَيۡفَ تُحۡيِ ٱلۡمَوۡتَىٰۖ قَالَ أَوَلَمۡ تُؤۡمِنۖ قَالَ بَلَىٰ وَلَٰكِن لِّيَطۡمَئِنَّ قَلۡبِيۖ قَالَ فَخُذۡ أَرۡبَعَةٗ مِّنَ ٱلطَّيۡرِ فَصُرۡهُنَّ إِلَيۡكَ ثُمَّ ٱجۡعَلۡ عَلَىٰ كُلِّ جَبَلٖ مِّنۡهُنَّ جُزۡءٗا ثُمَّ ٱدۡعُهُنَّ يَأۡتِينَكَ سَعۡيٗاۚ وَٱعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ

Ndipo (kumbukira) pamene Ibrahim adati: “E Mbuye wanga!, Ndionetseni mmene mudzaaukitsire akufa.” (Allah) adati: “Kodi sunakhulupirirebe?” Adati: “Iyayi, (ndikukhulupirira), koma (ndikufuna kuona zimenezo) kuti mtima wanga ukhazikike.” (Allah) adati: “Choncho katenge mbalame zinayi; uzisonkhanitse kwa iwe (mpaka uyizindikire mbalame iliyonse mmene ilili, ndipo kenako uziduledule zonsezo zidutswazidutswa ndikuzisakaniza ndi kuzigawa mzigawo zinayi). Ndipo paphiri lililonse ukaikepo gawo limodzi la zimenezo, ndipo kenako uziitane. Zikudzera zikuthamanga. Ndipo dziwa kuti Allah ndi Mwini mphamvu zoposa, Ngwanzem zakuya.”[52] info

[52] Mneneri Ibrahim adalakalaka kuti aone mmene akufa adzaukira kuti chikhulupiliro chake chiwonjezeke mphamvu. Tero Allah adamulamula kuti azinge mbalame zinayi zosiyanasiyana mitundu. Kenako azisakanize ziwalo zake. Ziwalo za mbalame ina zilowe kumbalame ina. Tsono azigawe miyulu inayi. Mulu uliwonse akauike pa phiri lakelake. Kenako aziitane mbalame zija. Ndipo aona kuti chiwalo chilichonse chikuthamangira kumbalame yake, pompo zonsezo zikhalanso mbalame zamoyo monga momwe zidalili poyamba.

التفاسير:

external-link copy
261 : 2

مَّثَلُ ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ كَمَثَلِ حَبَّةٍ أَنۢبَتَتۡ سَبۡعَ سَنَابِلَ فِي كُلِّ سُنۢبُلَةٖ مِّاْئَةُ حَبَّةٖۗ وَٱللَّهُ يُضَٰعِفُ لِمَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٌ

Fanizo la amene akupereka chuma chawo pa njira ya Allah lili ngati fanizo la njere imodzi yomwe yatulutsa ngala zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala iliyonse nkukhalamo njere zana limodzi. Ndipo Allah amamuonjezera amene wamfuna (kuposera pamenepa). Ndipo Allah alinazo zambiri, Ngodziwa.[53] info

[53] (Ndime 261-267) zikulimbikitsa kupereka chuma pa njira zabwino ndiponso zikuonetsa ubwino umene woperekayo amalandira kwa Allah. Komatu woperekayo kuti apeze ubwino wa Allah pafunika izi:
(a) apereke chifukwa cha Allah osati ncholinga chodzionetsera kwa anthu,
(b) choperekacho chikhale chabwino. Ngati wapereka zomwe sizabwino ndiye kuti sangapeze mphoto yaikulu,
(c) asawakumbe amene akuwapatsawo.
(d) Asawavutitse. Ndipo ngati atachita zimenezi ndiye kuti sangapeze mphoto koma kungotaya chuma pachabe. Kumbwezera mawu abwino wopempha nkopindulitsa kuposa sadaka yotonzera.
(e) Chimene akuperekacho chikhale chaHalali (chololedwa).Osati chomwe adachipeza m’njira yosavomerezeka.

التفاسير:

external-link copy
262 : 2

ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ثُمَّ لَا يُتۡبِعُونَ مَآ أَنفَقُواْ مَنّٗا وَلَآ أَذٗى لَّهُمۡ أَجۡرُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ

(Anthu) amene akupereka chuma chawo pa njira ya Allah napanda kutsatiza pa zomwe aperekazo kukumba, ndiponso masautso, iwo ali ndi mphoto kwa Mbuye wawo ndipo pa iwo sipadzakhala mantha; ndiponso sadzadandaula. info
التفاسير:

external-link copy
263 : 2

۞ قَوۡلٞ مَّعۡرُوفٞ وَمَغۡفِرَةٌ خَيۡرٞ مِّن صَدَقَةٖ يَتۡبَعُهَآ أَذٗىۗ وَٱللَّهُ غَنِيٌّ حَلِيمٞ

Mawu abwino, ndi kukhululukira (amene wakulakwira) nzabwino zedi kuposa sadaka yotsatizidwa ndi masautso. Ndipo Allah ndiyemwe ali Wolemera kwambiri ndiponso Woleza (kwa zolengedwa Zake). info
التفاسير:

external-link copy
264 : 2

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تُبۡطِلُواْ صَدَقَٰتِكُم بِٱلۡمَنِّ وَٱلۡأَذَىٰ كَٱلَّذِي يُنفِقُ مَالَهُۥ رِئَآءَ ٱلنَّاسِ وَلَا يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۖ فَمَثَلُهُۥ كَمَثَلِ صَفۡوَانٍ عَلَيۡهِ تُرَابٞ فَأَصَابَهُۥ وَابِلٞ فَتَرَكَهُۥ صَلۡدٗاۖ لَّا يَقۡدِرُونَ عَلَىٰ شَيۡءٖ مِّمَّا كَسَبُواْۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡكَٰفِرِينَ

E inu amene mwakhulupirira! Musaononge sadaka zanu pokumba ndiponso popereka masautso, monga yemwe akupereka chuma chake modzionetsera kwa anthu, ndipo sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Choncho fanizo lake lili ngati thanthwe lomwe pamwamba pake pali dothi. Kenako nkulifikira chimvula (nkuchotsa dothi lonse lija), nkulisiya lopanda kanthu. Tero sadzatha kupeza chilichonse pazimene adachita. Ndipo Allah satsogolera anthu osakhulupirira. info
التفاسير: