Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - 齐切瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·白塔俩

external-link copy
14 : 29

وَلَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا نُوحًا إِلَىٰ قَوۡمِهِۦ فَلَبِثَ فِيهِمۡ أَلۡفَ سَنَةٍ إِلَّا خَمۡسِينَ عَامٗا فَأَخَذَهُمُ ٱلطُّوفَانُ وَهُمۡ ظَٰلِمُونَ

Ndipo ndithu tidamtuma Nuh kwa anthu ake ndipo adakhala nawo zaka chikwi chimodzi kupatulapo zaka makumi asanu. (Koma m’nthawi yonseyi sadatsatire ulaliki wake). Choncho chigumula chidawapeza (ndipo adamira onse), uku ali odzichitira zoipa.[302] info

[302] M’ndime iyi, Allah akumthondoza Mtumiki Wake, Muhammad (s.a.w) pomufotokozera kuti kusakhulupilira kwa anthu akowa sichinthu chachilendo. Nawonso amene adalipo kale adamtsutsa Nuh ngakhaie kuti adalalikira kwa nthawi yayitali mpaka chigumula chidawamiza onse. Nawonso anthu akowa aonongedwa monga momwe zidalili ndi anthu a Nuh. Choncho usatekeseke ndi kusakhulupilira kwawo.

التفاسير: