Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима

Бет рақами:close

external-link copy
187 : 2

أُحِلَّ لَكُمۡ لَيۡلَةَ ٱلصِّيَامِ ٱلرَّفَثُ إِلَىٰ نِسَآئِكُمۡۚ هُنَّ لِبَاسٞ لَّكُمۡ وَأَنتُمۡ لِبَاسٞ لَّهُنَّۗ عَلِمَ ٱللَّهُ أَنَّكُمۡ كُنتُمۡ تَخۡتَانُونَ أَنفُسَكُمۡ فَتَابَ عَلَيۡكُمۡ وَعَفَا عَنكُمۡۖ فَٱلۡـَٰٔنَ بَٰشِرُوهُنَّ وَٱبۡتَغُواْ مَا كَتَبَ ٱللَّهُ لَكُمۡۚ وَكُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ حَتَّىٰ يَتَبَيَّنَ لَكُمُ ٱلۡخَيۡطُ ٱلۡأَبۡيَضُ مِنَ ٱلۡخَيۡطِ ٱلۡأَسۡوَدِ مِنَ ٱلۡفَجۡرِۖ ثُمَّ أَتِمُّواْ ٱلصِّيَامَ إِلَى ٱلَّيۡلِۚ وَلَا تُبَٰشِرُوهُنَّ وَأَنتُمۡ عَٰكِفُونَ فِي ٱلۡمَسَٰجِدِۗ تِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِ فَلَا تَقۡرَبُوهَاۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ ءَايَٰتِهِۦ لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَّقُونَ

Kwaloledwa kwa inu mu usiku wosala kukumana ndi akazi anu. Iwo ali ngati chovala chanu, inunso muli ngati chovala chawo. Allah wadziwa kuti mudali kudzichitira chinyengo nokha. Choncho walandira kulapa kwanu ndipo wakukhululukirani. Tsopano khudzanani nawo ndipo funani chimene Allah wakulamulirani, ndipo idyani ndi kumwa mpaka udziwike bwinobwino kwa inu ulusi woyera kuchokera ku ulusi wakuda kum’bandakucha (kufikira mudziwe kuti kucha kwalowa, usiku watha). Kenako kwaniritsani kusala mpaka dzuwa litalowa. Ndipo musakhudzane nawo (akazi anu) pamene inu mukuchita mbindikiro m’misikiti. Amenewo ndi malire a Allah; choncho musaayandikire. Motere ndimo Allah akulongosolera mwatsatanetsatane zisonyezo zake kwa anthu kuti akhale oopa Allah (potsatira malamulo ake ndi kusiya zoletsedwa). [22] info

[22] Pachiyambi pomwe lamulo la kusala lidakhazikitsidwa adawaletsa anthu kukumana ndi akazi awo usiku pambuyo poti iwo agona tulo ngakhale kuti angogona pang’ono pokha. Kukumana ndi mkazi akumane asanagone. Tero lamuloli lidali lovuta kwambiri kwa iwo kulitsata. Ena a iwo adalakwa pang’ono. Choncho kudalengezedwa kuti: “Tsopano pali chilolezo choti akhoza kuchita chilichonse mpaka m’bandakucha. Ndipo kunena koti: “Funani chimene Allah wakulamulani”, ndikulilimbikitsa lamulo kuchilolezocho. Musati kuti poti kale adakuletsani kukumana ndi akazi anu pambuyo pogona tulo ndiye mupitirize kutero - iyayi. Koma tsatirani chilolezocho.
“Itikafu” ndikuchita chitsimikizo munthu chokhala mu msikiti kwamasiku akutiakuti kapena nthawi yakutiyakuti. Ndipo pempheroli limachitika nthawi zambiri m’mwezi wa Ramadan. Akachita chitsimikizocho (niya) saloledwa kutuluka mu msikitimo pokhapokha patakhala chifukwa chachikulu chotulukira, monga kupita kukadzithandiza.

التفاسير:

external-link copy
188 : 2

وَلَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ وَتُدۡلُواْ بِهَآ إِلَى ٱلۡحُكَّامِ لِتَأۡكُلُواْ فَرِيقٗا مِّنۡ أَمۡوَٰلِ ٱلنَّاسِ بِٱلۡإِثۡمِ وَأَنتُمۡ تَعۡلَمُونَ

Ndipo musadye chuma chanu pakati panu mwachinyengo pochipereka kwa oweruza (m’njira ya ziphuphu) ndi cholinga choti mudye gawo la chuma cha anthu mwa uchimo uku inu mukudziwa. info
التفاسير:

external-link copy
189 : 2

۞ يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلۡأَهِلَّةِۖ قُلۡ هِيَ مَوَٰقِيتُ لِلنَّاسِ وَٱلۡحَجِّۗ وَلَيۡسَ ٱلۡبِرُّ بِأَن تَأۡتُواْ ٱلۡبُيُوتَ مِن ظُهُورِهَا وَلَٰكِنَّ ٱلۡبِرَّ مَنِ ٱتَّقَىٰۗ وَأۡتُواْ ٱلۡبُيُوتَ مِنۡ أَبۡوَٰبِهَاۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ لَعَلَّكُمۡ تُفۡلِحُونَ

Akukufunsa za miyezi nena: “Imeneyi ndi miyeso ya nthawi yozindikilira anthu zinthu zawo ndi nthawi ya Hajj.” Ndipo Siubwino kulowera m’nyumba zanu mbali ya kumbuyo kwake, koma ubwino ndiwayemwe akuopa Allah. Ndipo lowerani m’nyumba podzera m’makomo ake. Opani Allah kuti inu mupambane.[23] info

[23] M’nthawi ya umbuli anthu ankati akalowa m’mapemphero a Hajj sadali kulowa m’nyumba zawo podzera pakhomo pa nyumba. Ndipo sadalinso kutulukira pakhomo koma amaboola chibowo kuseri kwa nyumba nkumalowerapo ndi kutulukirapo namaganiza kuti kutero ndimapemphero okondweretsa Allah. Tsono apa Allah akuletsa mchitidwe umenewo.

التفاسير:

external-link copy
190 : 2

وَقَٰتِلُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ٱلَّذِينَ يُقَٰتِلُونَكُمۡ وَلَا تَعۡتَدُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ ٱلۡمُعۡتَدِينَ

Ndipo menyanani nao nkhondo pa njira ya Allah (modziteteza) amene akukuthirani nkhondo. Koma musalumphe malire (powamenya amene sadakuputeni), ndithu Allah sakonda olumpha malire.[24] info

[24] lyi ndi imodzi mwa ndime zomwe zikufotokoza bodza la amene akunena kuti chisilamu chidafala ndi lupanga powathira anthu nkhondo mowakakamiza kuti alowe m’Chisilamu.
Limeneli, ndithu ndibodza lamkunkhuniza. Apa pakuonetsa kuti Allah akuwapatsa chilolezo asilamu kuti amenyane ndi amene akuwaputa. Palibe chilolezo kwa iwo chowamenyera anthu osawaputa.

التفاسير: