قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا

صفحہ نمبر:close

external-link copy
36 : 33

وَمَا كَانَ لِمُؤۡمِنٖ وَلَا مُؤۡمِنَةٍ إِذَا قَضَى ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥٓ أَمۡرًا أَن يَكُونَ لَهُمُ ٱلۡخِيَرَةُ مِنۡ أَمۡرِهِمۡۗ وَمَن يَعۡصِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلٗا مُّبِينٗا

Ndipo sikoyenera kwa wokhulupirira wachimuna ndi wokhulupirira wachikazi, Allah ndi Mtumiki Wake akalamula chinthu, iwo nkukhala ndi chisankho pa zinthu zawo. Ndipo amene akunyoza Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu wasokera; kusokera koonekera.[323] info

[323] Ndime iyi ikunenetsa kuti sikoyenera kwa Msilamu kutsata maganizo ake pa chinthu chimene Allah ndi Mtumiki walamulapo lamulo, koma afunika kutsatira lamulo la Allah ndi Mtumiki, ndipo asakhale ndi chifuniro pa zinthu zomwe nza chipembedzo koma agonjere zimene Allah walamula ndi Mtumiki Wake. Kunyoza lamulo la Allah ndi Mtumiki kumachititsa kuti munthu atayike.

التفاسير:

external-link copy
37 : 33

وَإِذۡ تَقُولُ لِلَّذِيٓ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِ وَأَنۡعَمۡتَ عَلَيۡهِ أَمۡسِكۡ عَلَيۡكَ زَوۡجَكَ وَٱتَّقِ ٱللَّهَ وَتُخۡفِي فِي نَفۡسِكَ مَا ٱللَّهُ مُبۡدِيهِ وَتَخۡشَى ٱلنَّاسَ وَٱللَّهُ أَحَقُّ أَن تَخۡشَىٰهُۖ فَلَمَّا قَضَىٰ زَيۡدٞ مِّنۡهَا وَطَرٗا زَوَّجۡنَٰكَهَا لِكَيۡ لَا يَكُونَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ حَرَجٞ فِيٓ أَزۡوَٰجِ أَدۡعِيَآئِهِمۡ إِذَا قَضَوۡاْ مِنۡهُنَّ وَطَرٗاۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ مَفۡعُولٗا

Ndipo (kumbuka) pamene udamuuza yemwe Allah adampatsa mtendere (pomuongolera ku Chisilamu, ndipo) iwenso udampatsa mtendere (pomulera ndi kumpatsa ufulu, yemwe ndi Zaid Bun Haritha, udati kwa iye): “Gwirizana ndi mkazi wako, ndipo wopa Allah.” Ukubisa mu mtima mwako chimene Allah afuna kuchisonyeza poyera (chomwe ndi kuti Allah akulamula kumkwatira mkazi ameneyo akamuleka Zaid Bun Haritha kuti chichoke chizolowezi choti mwana wongomulera chabe nkumuyesa mwana wako weniweni). Ndipo ukuopa anthu (kuti akudzudzula pa zimenezo), pomwe woyenera kumuopa ndi Allah. Choncho pamene Zaid adamaliza chilakolako chake pa mkazi ameneyo, tidakukwatitsa iwe kuti pasakhale masautso pa okhulupirira pokwatira akazi a ana awo akungowalera chabe ngati (anawo) atamaliza zilakolako zawo pa akaziwo, ndipo lamulo la Allah ndilochitika, (palibe chingalepheretse kuti lisachitike).[324] info

[324] Polamula chinthu kuti chichitike kapena chisachitike, pafunika kuti iwe wolamula ukhale woyamba kutsata malamulowo. Ngati sutero, ndiye kuti malamulo akowo sangakhale ndi mphamvu. Mu ndime iyi muli chilolezo chomukwatira mkazi yemwe wasiyidwa ukwati ndi mwana yemwe adangoleredwa chabe ndi munthu amene amatcha mwanayo kuti ndi mwana wake chifukwa chomulera. Kalelo zoterezi sizimaloledwa. Choncho Mtumiki (s.a.w) adauzidwa kuti achite iye mwini zimenezi pofuna kuthetsa chikhalidwecho.

التفاسير:

external-link copy
38 : 33

مَّا كَانَ عَلَى ٱلنَّبِيِّ مِنۡ حَرَجٖ فِيمَا فَرَضَ ٱللَّهُ لَهُۥۖ سُنَّةَ ٱللَّهِ فِي ٱلَّذِينَ خَلَوۡاْ مِن قَبۡلُۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ قَدَرٗا مَّقۡدُورًا

Palibe tchimo pa Mneneri pa zimene Allah wamulamula. Chimenechi ndichizolowezi cha Allah (njira ya Allah) pa amene adanka kale. Ndipo lamulo la Allah ndi chikonzero (chomwe) chidakonzedwa. (Ndipo sichisinthidwa). [325] info

[325] Ndime iyi ikumuuza Mtumiki (s.a.w) kuti palibe vuto pa iye ngakhale tchimo kapena kudzudzulidwa pa chomwe Allah wamulamula kuchichita monga kukwatira akazi ambiri. Ayuda amamunyoza ndi kumudzudzula chifukwa chokwatira akazi ambiri. Koma Allah adawayankha ndi mawu ake oti: “Iyi ndi njira ya Allah yomwe idalipo pa Aneneri akale! Daud adakwatira akazi 100. Ndipo Sulaimani akazi 300.

التفاسير:

external-link copy
39 : 33

ٱلَّذِينَ يُبَلِّغُونَ رِسَٰلَٰتِ ٱللَّهِ وَيَخۡشَوۡنَهُۥ وَلَا يَخۡشَوۡنَ أَحَدًا إِلَّا ٱللَّهَۗ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ حَسِيبٗا

(Aneneri) amene amafikitsa uthenga wa Allah (kwa anthu) uku akumuopa Iye, ndipo samamuopa aliyense koma Allah (yekha). Ndipo Allah Akukwana kukhala wowerengera (zochita za akapolo Ake).[326] info

[326] Ndime iyi ikumuuza Mtumiki kuti amene adamulamula kuti awatsanzire pa zimene ankachita ndi iwo amene ankafikitsa uthenga wa Allah kwa anthu, ndipo samaopa kudzudzulidwa ndi aliyense pa chomwe Allah wawalamula kuchita, koma ankangoopa Allah Yekha. Choncho nawenso tsanzira khalidwe lawo ndi kuopa Allah Yekha.

التفاسير:

external-link copy
40 : 33

مَّا كَانَ مُحَمَّدٌ أَبَآ أَحَدٖ مِّن رِّجَالِكُمۡ وَلَٰكِن رَّسُولَ ٱللَّهِ وَخَاتَمَ ٱلنَّبِيِّـۧنَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٗا

Muhammad (s.a.w) sali tate wa aliyense mwa amuna anu, koma iye ndi Mtumiki wa Allah, ndiponso wotsiriza mwa Aneneri. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.[327] info

[327] (“Khaatamu Nabiyyina) “Mneneri wotsirizira” tanthauzo lake ndi kuti Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndimneneri womalizira; palibe mneneri wina pambuyo pake mpaka kutha kwadziko lapansi. Ayah imeneyi ikutsutsa zonena za Akadiyani ndi enanso omwe akumutcha mtsogoleri wawo kuti ndi mneneri.

التفاسير:

external-link copy
41 : 33

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ ذِكۡرٗا كَثِيرٗا

E inu amene mwakhulupirira! Mkumbukireni Allah; kumkumbukira kwambiri. info
التفاسير:

external-link copy
42 : 33

وَسَبِّحُوهُ بُكۡرَةٗ وَأَصِيلًا

Ndipo mulemekezeni m’mawa ndi madzulo.[328] info

[328] Allah wasankha nthawi ziwiri kuti zikhale zochulukitsa kumtamanda ndi kumulemekeza chifukwa chakuti zimenezi ndi nthawi zabwino zimene angelo amatsika kuchokera kumwamba.

التفاسير:

external-link copy
43 : 33

هُوَ ٱلَّذِي يُصَلِّي عَلَيۡكُمۡ وَمَلَٰٓئِكَتُهُۥ لِيُخۡرِجَكُم مِّنَ ٱلظُّلُمَٰتِ إِلَى ٱلنُّورِۚ وَكَانَ بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ رَحِيمٗا

Iye ndi Amene akukuchitirani chifundo (ndi kukufunirani zabwino) nawonso Angelo Ake (akukupemphelerani kwa Allah) kuti akutulutseni mu mdima ndi kukuikani m’kuunika. Ndipo (Iye) Ngwachisoni zedi kwa okhulupirira. info
التفاسير: