قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - شىيشىيۋاچە تەرجىمىسى - خالىد ئىبراھىم بىيتالا

بەت نومۇرى:close

external-link copy
114 : 4

۞ لَّا خَيۡرَ فِي كَثِيرٖ مِّن نَّجۡوَىٰهُمۡ إِلَّا مَنۡ أَمَرَ بِصَدَقَةٍ أَوۡ مَعۡرُوفٍ أَوۡ إِصۡلَٰحِۭ بَيۡنَ ٱلنَّاسِۚ وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ ٱبۡتِغَآءَ مَرۡضَاتِ ٱللَّهِ فَسَوۡفَ نُؤۡتِيهِ أَجۡرًا عَظِيمٗا

Palibe ubwino m’zambiri zimene akunong’onezana kupatula amene akulamulira ena kupereka sadaka, kapena kuchita zabwino, kapenanso kuyanjanitsa pakati pa anthu (pakunong’onezana mawu). Amene angachite zimenezi, chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah, tidzampatsa malipiro aakulu. info
التفاسير:

external-link copy
115 : 4

وَمَن يُشَاقِقِ ٱلرَّسُولَ مِنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُ ٱلۡهُدَىٰ وَيَتَّبِعۡ غَيۡرَ سَبِيلِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ نُوَلِّهِۦ مَا تَوَلَّىٰ وَنُصۡلِهِۦ جَهَنَّمَۖ وَسَآءَتۡ مَصِيرًا

Ndipo amene anyoza Mtumiki pambuyo pomuonekera chiongoko, nkutsata njira yosakhala ya okhulupirira, timtembenuzira kumene watembenukira mwini wakeko. Ndipo tidzamulowetsa ku Jahannam. Taonani kuipa malo ofikira. info
التفاسير:

external-link copy
116 : 4

إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَغۡفِرُ أَن يُشۡرَكَ بِهِۦ وَيَغۡفِرُ مَا دُونَ ذَٰلِكَ لِمَن يَشَآءُۚ وَمَن يُشۡرِكۡ بِٱللَّهِ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا

Ndithudi, Allah sakhululuka (uchimo) womphatikiza ndi chinthu china, (pochiyesa kuti ndi mnzake wa Allah). Koma Iye amakhululukira machimo ena omwe sali amenewo kwa yemwe wamfuna. Ndipo yemwe angamphatikize Allah (ndi milungu yabodza), ndithudi, wasokera kusokera konka nako kutali (ndi njira yachoonadi). info
التفاسير:

external-link copy
117 : 4

إِن يَدۡعُونَ مِن دُونِهِۦٓ إِلَّآ إِنَٰثٗا وَإِن يَدۡعُونَ إِلَّا شَيۡطَٰنٗا مَّرِيدٗا

Sapembedza Allah koma mafano achikazi, ndiponso sapembedza china koma satana wonyoza (wamachimo) info
التفاسير:

external-link copy
118 : 4

لَّعَنَهُ ٱللَّهُۘ وَقَالَ لَأَتَّخِذَنَّ مِنۡ عِبَادِكَ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا

(Yemwe) Allah adamtembelera. Ndipo iye (satana) adati (kwa Allah): “Ndithudi, ndikadzipezera gawo lodziwika mwa akapolo anu.”[148] info

[148] Iblis pamene adampirikitsa kumwamba iye adauza Allah kuti akazikometsera zolengedwa zake machimo. Allah adamuuza kuti sangathe kuzisokereza mwamphamvu, mozikakamiza, zifune zisafune. Aliyense amene akamtsata ndiye kuti akamtsata mwachifuniro chake. Sikuti mogonjetsedwa ndi mphamvu za satana kotero kuti iye sangathe kulimbana naye iyayi. Satana alibe mphamvu zokakamizira anthu.

التفاسير:

external-link copy
119 : 4

وَلَأُضِلَّنَّهُمۡ وَلَأُمَنِّيَنَّهُمۡ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُبَتِّكُنَّ ءَاذَانَ ٱلۡأَنۡعَٰمِ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُغَيِّرُنَّ خَلۡقَ ٱللَّهِۚ وَمَن يَتَّخِذِ ٱلشَّيۡطَٰنَ وَلِيّٗا مِّن دُونِ ٱللَّهِ فَقَدۡ خَسِرَ خُسۡرَانٗا مُّبِينٗا

“Ndipo ndikawasokeretsa ndi kuwapatsa ziyembekezo (zabodza) ndithu ndikawalamula kuti azikadula makutu a ziweto, ndipo ndikawalamulanso kuti azikasintha chilengedwe cha Allah.” Ndipo amene angamulole satana kukhala mtetezi wake kusiya Allah, ndiye kuti wataika koonekera.[149] info

[149] (1) Kukhala ndi chiyembekezo choti Allah adzawakhululukira pakuti iye ngokhululuka, Ngwachifundo. (2) Kuti ukachita zakutizakuti kapena ukawerenga duwa yakutiyakuti machimo ako onse adzakufafanizira ngakhale kuti udakwatula zinthu za anthu. (3) Kuti wolemekezeka uje adzatiwombola ngati tilumikizana naye. (4) Kuti mneneri wakutiwakuti adzaitana omtsatira ake kuti akalowe ku Munda wa mtendere. (5) Kuti Mtumiki sadzakhala wokondwa kuona anthu ake akuponyedwa ku Moto. (6) Kukhala ndi chiyembekezo choti ngati munthu ndiwe Msilamu basi sukalowa ku Jahannam. Ndipo satanayu amanyenganso Akhrisitu kuti ngati akhulupilira Isa (Yesu) basi sakalowa ku Moto. Ndipo Ayuda amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati akhulupilira m’chipembedzo cha chiyuda sakalowa ku Moto. Nawonso opembedza moto ndi Abudha amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati atsata chibudha basi apulumuka.

التفاسير:

external-link copy
120 : 4

يَعِدُهُمۡ وَيُمَنِّيهِمۡۖ وَمَا يَعِدُهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ إِلَّا غُرُورًا

(Satana) akuwalonjeza ndikuwapatsa chiyembekezo (pa zinthu zomwe sizingachitike). Ndithudi, satana sawalonjeza china koma chinyengo basi. info
التفاسير:

external-link copy
121 : 4

أُوْلَٰٓئِكَ مَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُ وَلَا يَجِدُونَ عَنۡهَا مَحِيصٗا

Iwowo malo awo ndi ku Jahannam ndipo sadzapeza pothawira kutuluka mmenemo. info
التفاسير: