Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro bya Qur'an Ntagatifu mu rurimi rw'igi Chewa - Khaled Ibrahim Betala.

numero y'urupapuro:close

external-link copy
102 : 4

وَإِذَا كُنتَ فِيهِمۡ فَأَقَمۡتَ لَهُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَلۡتَقُمۡ طَآئِفَةٞ مِّنۡهُم مَّعَكَ وَلۡيَأۡخُذُوٓاْ أَسۡلِحَتَهُمۡۖ فَإِذَا سَجَدُواْ فَلۡيَكُونُواْ مِن وَرَآئِكُمۡ وَلۡتَأۡتِ طَآئِفَةٌ أُخۡرَىٰ لَمۡ يُصَلُّواْ فَلۡيُصَلُّواْ مَعَكَ وَلۡيَأۡخُذُواْ حِذۡرَهُمۡ وَأَسۡلِحَتَهُمۡۗ وَدَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَوۡ تَغۡفُلُونَ عَنۡ أَسۡلِحَتِكُمۡ وَأَمۡتِعَتِكُمۡ فَيَمِيلُونَ عَلَيۡكُم مَّيۡلَةٗ وَٰحِدَةٗۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن كَانَ بِكُمۡ أَذٗى مِّن مَّطَرٍ أَوۡ كُنتُم مَّرۡضَىٰٓ أَن تَضَعُوٓاْ أَسۡلِحَتَكُمۡۖ وَخُذُواْ حِذۡرَكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا

Ndipo ngati uli pamodzi (ndi Asilamu pankhondo) ndikuwatsogolera Swala, ndiye kuti gulu limodzi la iwo liimilire pamodzi ndi iwe ndikupemphera uku atagwirizira zida zawo. Ndipo akamaliza kulambira kwawo, apite kumbuyo kwanu (kuti akulondereni) ndipo lidze gulu lina lomwe silidapemphere, lipemphere nawe pamodzi; nawonso achenjere ndikugwirizira zida zawo (nkupemphera), chifukwa chakuti omwe sadakhulupirire akufuna kuti mutanyalanyaza zida zanu ndi katundu wanu angokuukirani nthawi imodzi. Koma sikulakwa kwa inu mutaika pansi zida zanu chifukwa chakuvutitsidwa ndi mvula kapena ngati mukudwala. Koma chenjeranaoni. Ndithudi Allah wawakonzera chilango choyalutsa osakhulupirira.[139] info

[139] Swala yopemphera pagulu (jamaa) akuilimbikitsa zedi ngakhale kuti anthu ali pakati pa nkhondo. Ngati nthawi ya Swala yakwana akuwauza kuti apemphere pagulu, koma asapemphere onse nthawi imodzi. Anthuwo agawike m’magulu awiri. Gulu lina liyang’ane komwe kuli adani, ndipo gulu lina likhale likupemphera pamodzi ndi (Imamu) mtsogoleri wawo. Komatu Swala akunkhondo amaswali raka ziwiriziwiri (Swala iliyonse) kupatula Swala ya Magharibi. Tsono Imamu adzapemphera raka imodzi ndi awo omwe akupemphera nawo. Akaimilira kuti apemphere raka yachiwiri, aja omwe anali kupemphera naye aimilire ndi kupemphera raka yotsalayo mwachangu atamsiya imamu ali chiimilire. Ndipo apite kukalowa m’malo mwa anzawo omwe anali kuyang’ana komwe kuli adani. Tsono anzawowo adze nkudzapemphera ndi Imamu. Imamu akamaliza raka yake yachiwiri, iwo aimilire nkumaliza raka yawo yachiwiri. Komatu popempherapo zida zawo zikhale atazikoleka m’matupi mwawo pokhapokha ngati pali zifukwa zoikitsa zidazo pansi, zomwe azitchula kumapeto a ndimeyo

التفاسير:

external-link copy
103 : 4

فَإِذَا قَضَيۡتُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ قِيَٰمٗا وَقُعُودٗا وَعَلَىٰ جُنُوبِكُمۡۚ فَإِذَا ٱطۡمَأۡنَنتُمۡ فَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَۚ إِنَّ ٱلصَّلَوٰةَ كَانَتۡ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ كِتَٰبٗا مَّوۡقُوتٗا

Mukamaliza Swala, pitirizani kumkumbukira Allah muli chiimire, chikhalire kapena mutagona chammbali. Ngati mutapeza chitetezo (chifukwa chakuti nkhondo palibe), pempherani Swala zanu mwa chilamulo. Ndithudi, Swala ndilamulo lokhala ndi nthawi kwa okhulupirira.[140] info

[140] Nkofunika nthawi zonse Msilamu kukumbukira Allah.osati panthawi yokha yopemphera koma amkumbukire m’chikhalidwe chake chonse ndi m’zochita zake zonse. Nthawi zonse apewe zomwe Allah waletsa ndi kutsata malamulo ake.

التفاسير:

external-link copy
104 : 4

وَلَا تَهِنُواْ فِي ٱبۡتِغَآءِ ٱلۡقَوۡمِۖ إِن تَكُونُواْ تَأۡلَمُونَ فَإِنَّهُمۡ يَأۡلَمُونَ كَمَا تَأۡلَمُونَۖ وَتَرۡجُونَ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا يَرۡجُونَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمًا

Ndipo musachite ulesi kutsata anthu (omwe ndi adani), ngati mukumva kupweteka, iwonso akumva kupweteka monga momwe inu mukumvera kupweteka. Koma inu mukuyembekezera kwa Allah chomwe iwo sakuyembekezera. Ndipotu Allah Ngodziwa, Ngwanzeru.[141] info

[141] Apa akuwalamula Asilamu kuti amenyere chipembedzo chawo ngakhale atapeza mavuto amtundumtundu. Chifukwa chomwe akupezera mavutowo nchachikulu zedi kuposa mavutowo palibe chinthu chachikulu chimene munthu angachipeze chabe popanda kuvutikira.

التفاسير:

external-link copy
105 : 4

إِنَّآ أَنزَلۡنَآ إِلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ بِٱلۡحَقِّ لِتَحۡكُمَ بَيۡنَ ٱلنَّاسِ بِمَآ أَرَىٰكَ ٱللَّهُۚ وَلَا تَكُن لِّلۡخَآئِنِينَ خَصِيمٗا

Ndithudi, takuvumbulutsira buku mwa choonadi kuti uweruzire pakati pa anthu, monga momwe Allah wakuphunzitsira. Ndipo usakhale mtetezi wa achinyengo. info
التفاسير: