Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala

Número de página:close

external-link copy
34 : 8

وَمَا لَهُمۡ أَلَّا يُعَذِّبَهُمُ ٱللَّهُ وَهُمۡ يَصُدُّونَ عَنِ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ وَمَا كَانُوٓاْ أَوۡلِيَآءَهُۥٓۚ إِنۡ أَوۡلِيَآؤُهُۥٓ إِلَّا ٱلۡمُتَّقُونَ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ

(Kodi iwo Aquraish) ali ndi chinthu chanji (chabwino chimene) chingamuletse Allah kuwalanga? Pomwe iwo akuwatsekereza anthu kulowa mu Msikiti Wopatulika. Iwo sanayenere kukhala ouyang’anira (Msikitiwo). Palibe angauyang’anire koma olungama, koma anthu ambiri sadziwa.[201] info

[201] M’chaka chachisanu nchimodzi (6) chakusamuka, Mtumiki (s.a.w) pamodzi ndi omtsatira ake ochuluka zedi adapita ku Makka ncholinga chokachita mapemphero a Umra. Koma Aquraish adamuletsa kulowa mu mzinda wa Makka podziganizira kuti iwo ndiwo oyang’anira Kaaba.

التفاسير:

external-link copy
35 : 8

وَمَا كَانَ صَلَاتُهُمۡ عِندَ ٱلۡبَيۡتِ إِلَّا مُكَآءٗ وَتَصۡدِيَةٗۚ فَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَ بِمَا كُنتُمۡ تَكۡفُرُونَ

Ndipo mapemphero awo pa nyumba yopatulikayo sadali kanthu, koma kuyimba miluzi ndi kuomba m’manja. Choncho (adzauzidwa): “Lawani chilango chifukwa chakusakhulupirira kwanu.” info
التفاسير:

external-link copy
36 : 8

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ لِيَصُدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ فَسَيُنفِقُونَهَا ثُمَّ تَكُونُ عَلَيۡهِمۡ حَسۡرَةٗ ثُمَّ يُغۡلَبُونَۗ وَٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ إِلَىٰ جَهَنَّمَ يُحۡشَرُونَ

Ndithu osakhulupirira akupereka chuma chawo (pa nkhondo yolimbana ndi Asilamu) ndi cholinga choti awatsekeleze anthu kuyenda pa njira ya Allah. Choncho adzapitiriza kupereka chumacho kenako chidzakhala chowadandaulitsa, ndipo adzagonjetsedwa. Ndipo omwe sanakhulupirire adzasonkhanitsidwa ku Jahannam. info
التفاسير:

external-link copy
37 : 8

لِيَمِيزَ ٱللَّهُ ٱلۡخَبِيثَ مِنَ ٱلطَّيِّبِ وَيَجۡعَلَ ٱلۡخَبِيثَ بَعۡضَهُۥ عَلَىٰ بَعۡضٖ فَيَرۡكُمَهُۥ جَمِيعٗا فَيَجۡعَلَهُۥ فِي جَهَنَّمَۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ

Kuti Allah alekanitse oipa ndi abwino, ndi kuti awayike ena mwa oipawo pamwamba pa anzawo, potero nkuwaunjika oipawo mulu umodzi, kenako nawaponya ku Jahannam. Iwowa ndi anthu otaika. info
التفاسير:

external-link copy
38 : 8

قُل لِّلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ إِن يَنتَهُواْ يُغۡفَرۡ لَهُم مَّا قَدۡ سَلَفَ وَإِن يَعُودُواْ فَقَدۡ مَضَتۡ سُنَّتُ ٱلۡأَوَّلِينَ

Nena kwa osakhulupirira kuti: “Ngati asiya (zochita zawo zoipa), adzakhululukidwa zimene zidatsogola. Koma ngati abwereza (kuwazunza Asilamu, tiwalanga) ndithudi njira ya Allah yomwe idachitika kwa anthu akale inadutsa (powalanga akasiya kutsata malamulo a Allah). info
التفاسير:

external-link copy
39 : 8

وَقَٰتِلُوهُمۡ حَتَّىٰ لَا تَكُونَ فِتۡنَةٞ وَيَكُونَ ٱلدِّينُ كُلُّهُۥ لِلَّهِۚ فَإِنِ ٱنتَهَوۡاْ فَإِنَّ ٱللَّهَ بِمَا يَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ

Ndipo menyanani nawo osakhulupirira kufikira shirik itatha ndipo chipembedzo chonse chikhale cha Allah. Ndipo ngati asiya, ndithu Allah Ngoona zomwe akuchita. info
التفاسير:

external-link copy
40 : 8

وَإِن تَوَلَّوۡاْ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَوۡلَىٰكُمۡۚ نِعۡمَ ٱلۡمَوۡلَىٰ وَنِعۡمَ ٱلنَّصِيرُ

Koma ngati apitiriza kunyoza kwawo, dziwani kuti Allah ndi Mtetezi wanu, Mtetezi wokoma mtima koposa, ndi Mthandizi wabwino. info
التفاسير: