[291] M’ndime iyi, Allah akuti akadawalekelera anthu oipa, omwe cholinga chawo nkudzetsa chisokonezo pa dziko, popanda kusankha anthu ena kuti alimbane nawo, ndiye kuti nyumba zopempheleramo Ayuda, Akhrisitu ndi Asilamu, zikadagumulidwa. Koma Allah amasankha anthu olungama kuti alimbane ndi anthu oipawo kuti choonadi cha Allah chisazime. Ndipo amene akuteteza choonadi cha Allah, Iye walonjeza kumthangata.