وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - خالد ئیبراهيم بيتالا

ژمارەی پەڕە:close

external-link copy
116 : 3

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَن تُغۡنِيَ عَنۡهُمۡ أَمۡوَٰلُهُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُهُم مِّنَ ٱللَّهِ شَيۡـٔٗاۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ

Ndithudi, amene sakhulupirira, chuma chawo ngakhale ana awo, sizidzawathandiza chilichonse kwa Allah. Ndipo iwo ndi anthu a ku Moto basi; adzakhala mmenemo nthawi yaitali. info
التفاسير:

external-link copy
117 : 3

مَثَلُ مَا يُنفِقُونَ فِي هَٰذِهِ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا كَمَثَلِ رِيحٖ فِيهَا صِرٌّ أَصَابَتۡ حَرۡثَ قَوۡمٖ ظَلَمُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ فَأَهۡلَكَتۡهُۚ وَمَا ظَلَمَهُمُ ٱللَّهُ وَلَٰكِنۡ أَنفُسَهُمۡ يَظۡلِمُونَ

Fanizo la chimene akupereka mwaulere pa moyo uwu wa dziko lapansi, chili ngati mphepo yomwe mkati mwake muli chisanu chaukali, chagwera pa munda wa anthu omwe adadzichitira okha zoipa, n’kuuonongeratu. Si Allah amene adawachitira zoipa, koma iwo okha adadzichitira zoipa.[80] info

[80] Tsono amene savomereza Allah potsatira malamulo ake ndi kusiya zomwe lye adaletsa, ngakhale atachita zabwino zotani sakamlipira pa tsiku lachimaliziro. Ngati nkofunika kuti amulipire, ndiye kuti amulipiliratu pompano pa dziko lapansi.

التفاسير:

external-link copy
118 : 3

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ بِطَانَةٗ مِّن دُونِكُمۡ لَا يَأۡلُونَكُمۡ خَبَالٗا وَدُّواْ مَا عَنِتُّمۡ قَدۡ بَدَتِ ٱلۡبَغۡضَآءُ مِنۡ أَفۡوَٰهِهِمۡ وَمَا تُخۡفِي صُدُورُهُمۡ أَكۡبَرُۚ قَدۡ بَيَّنَّا لَكُمُ ٱلۡأٓيَٰتِۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ

E inu amene mwakhulupirira! Musawachite omwe sali mwa inu kukhala abwenzi; owauza chinsinsi, iwo sasiya kukuchitirani choipa. Amakonda zimene zikukuvutitsani. Chidani chawo (pa inu) chaonekera m’milomo yawo. Ndipo zimene zikubisa zifuwa zawo, nzazikulu zedi. Ndithudi, takufotokozerani zizindikiro zonse ngati inu muli anthu ozindikira.[81] info

[81] Chimodzi mwa zinthu zazikulu chomwe chimachititsa kuti zochita za anthu zitheke kapena kuti zilongosoke, ndiko kuzikonza zinthuzo mwa chinsinsi. Zioneke pamaso pa anthu zili zothaitha kuzikonza. Chifukwa pali anthu ambiri oipa maganizo omwe safuna kuti zinthu za anzawo zilongosoke. Iwo amafunitsitsa kuti aziononge zisanachitike. Ndipo nchifukwa chake apa akuletsa kuwaululira zachinsinsi anthu omwe sali Asilamu, kapena kuwachita kukhala abwenzi enieni.
Komatu sikuti apa akuletsa ubwenzi wakuti: “Muli bwanji? Tili bwino”. Ndiponso sakuletsa kuwachitira zabwino ndi zachilungamo, monga momwe afotokozera pandime yachisanu nchitatu yam’surat Mumtahina. (Qur’an 60:8)

التفاسير:

external-link copy
119 : 3

هَٰٓأَنتُمۡ أُوْلَآءِ تُحِبُّونَهُمۡ وَلَا يُحِبُّونَكُمۡ وَتُؤۡمِنُونَ بِٱلۡكِتَٰبِ كُلِّهِۦ وَإِذَا لَقُوكُمۡ قَالُوٓاْ ءَامَنَّا وَإِذَا خَلَوۡاْ عَضُّواْ عَلَيۡكُمُ ٱلۡأَنَامِلَ مِنَ ٱلۡغَيۡظِۚ قُلۡ مُوتُواْ بِغَيۡظِكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ

Ha! Inu ndinu amene muwakonda (adani anu) pomwe iwo sakukondani ngakhale inu mukukhulupirira mabuku onse! Akakumana nanu amanena (mwachiphamaso): “Takhulupirira.” Koma akakhala kwa okha, amakulumirani nsonga za zala chifukwa chaukali. Nena: “Mwalirani ndiukali wanuwo ndithudi, Allah akudziwa za m’zifuwa (mwanu).” info
التفاسير:

external-link copy
120 : 3

إِن تَمۡسَسۡكُمۡ حَسَنَةٞ تَسُؤۡهُمۡ وَإِن تُصِبۡكُمۡ سَيِّئَةٞ يَفۡرَحُواْ بِهَاۖ وَإِن تَصۡبِرُواْ وَتَتَّقُواْ لَا يَضُرُّكُمۡ كَيۡدُهُمۡ شَيۡـًٔاۗ إِنَّ ٱللَّهَ بِمَا يَعۡمَلُونَ مُحِيطٞ

Ngati chabwino chikakufikirani, amaipidwa nacho; koma choipa chikakugwerani amachikondwelera. Koma ngati inu mupirira ndi kuopa Allah, ndale zawo sizingakuvutitseni chilichonse. Ndithu Allah akudziwa bwino zonse zimene iwo akuchita.[82] info

[82] M’ndime iyi akuwauza kuti asaope ufiti ngakhale kulodzedwa. Koma ayadzamire kwa Allah basi. Chimene Allah wafuna chimachitika. Palibe amene angachitsekereze. Choncho m’bale wanga moyo wako ukhale wokhazikika. Ngati ufuna kuchita chinthu usaope mfiti, wadumbo ndi mdani. dziwa kuti chimene Allah walemba sichingafafanizidwe.

التفاسير:

external-link copy
121 : 3

وَإِذۡ غَدَوۡتَ مِنۡ أَهۡلِكَ تُبَوِّئُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ مَقَٰعِدَ لِلۡقِتَالِۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ

(Kumbukira) pamene unachoka m’mawa kusiya banja lako kuti uwakonzere Asilamu malo omenyanira (nkhondo). Ndipo Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[83] info

[83] Apa akunena nkhani ya nkhondo yachiwiri yaikulu kwabasi pambiri ya Chisilamu, nkhondo ya Uhudi. Nkhondo imeneyi Asilamu adakumana ndi masautso akulu chifukwa cha Asilamu ena amene adaswa lamulo la Mtumiki (s.a.w). Ndiponso chifukwa cha anthu ena omwe adalowa Chisilamu mwachiphamaso, (achiphamaso) omwe adapita ku nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) koma adakathawa kunkhondoko. Ndipo adali ochuluka gawo limodzi mwa magawo atatu a Asilamu (1/3). Pothawapo adathawa ochuluka kuposa nambala yatchulidwayi. Koma ena mwa iwo adabwerera nkudzalumikizananso ndi gulu la nkhondo la Mtumiki (s.a.w).

التفاسير: