क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - ख़ालिद अबराहीम बेताला

पृष्ठ संख्या:close

external-link copy
32 : 5

مِنۡ أَجۡلِ ذَٰلِكَ كَتَبۡنَا عَلَىٰ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ أَنَّهُۥ مَن قَتَلَ نَفۡسَۢا بِغَيۡرِ نَفۡسٍ أَوۡ فَسَادٖ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَكَأَنَّمَا قَتَلَ ٱلنَّاسَ جَمِيعٗا وَمَنۡ أَحۡيَاهَا فَكَأَنَّمَآ أَحۡيَا ٱلنَّاسَ جَمِيعٗاۚ وَلَقَدۡ جَآءَتۡهُمۡ رُسُلُنَا بِٱلۡبَيِّنَٰتِ ثُمَّ إِنَّ كَثِيرٗا مِّنۡهُم بَعۡدَ ذَٰلِكَ فِي ٱلۡأَرۡضِ لَمُسۡرِفُونَ

Pachifukwa chazimenezo, tidawalamula ana a Israyeli kuti amene wapha munthu popanda iye (wophedwayo) kupha munthu, kapena kuchita chisokonezo pa dziko, ali ngati wapha anthu onse. Ndipo amene wamuleka munthu ali ndi moyo, ali ngati awapatsa moyo anthu onse. Ndithudi, atumiki Athu adawadzera iwo ndi zisonyezo zoonekera. Koma ndithu ambiri a iwo, pambuyo pa zimenezo, adapitirizabe kuononga pa dziko. info
التفاسير:

external-link copy
33 : 5

إِنَّمَا جَزَٰٓؤُاْ ٱلَّذِينَ يُحَارِبُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَيَسۡعَوۡنَ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَسَادًا أَن يُقَتَّلُوٓاْ أَوۡ يُصَلَّبُوٓاْ أَوۡ تُقَطَّعَ أَيۡدِيهِمۡ وَأَرۡجُلُهُم مِّنۡ خِلَٰفٍ أَوۡ يُنفَوۡاْ مِنَ ٱلۡأَرۡضِۚ ذَٰلِكَ لَهُمۡ خِزۡيٞ فِي ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابٌ عَظِيمٌ

Ndithu mphoto ya amene akulimbana ndi Allah ndi Mtumiki Wake (pochita zomwe waletsa) ndi kudzetsa chionongeko pa dziko, aphedwe kapena apachikidwe pa mtanda, kapena adulidwe manja awo ndi miyendo yawo mosemphanitsa (dzanja lakumanja ndi phazi lakumanzere, ndipo dzanja lakumanzere ndi phazi lakumanja); kapena apirikitsidwe mdzikomo. Uku ndikuyaluka kwawo pa dziko lapansi. Ndipo iwo pa tsiku lachimaliziro adzalandira chilango chachikulu.[164] info

[164] Apa atchula chilango chowapatsa anthu owononga, amene amafwamba anthu m’njira zawo. Anthu otere alandire zilango izi:- (a) Ngati akungopha oyenda m’njiramo popanda kuwatengera chuma chawo akawapha, iwo akagwidwa chiweruzo chawo nkuphedwa nawonso. (b) Ngati akupha ndi kulanda chuma, atagwidwa chiweruzo chawo nkuphedwa. Ndipo akaphedwa choncho awapachike pa mtanda kwamasiku atatu asanawaike m’manda. Kapena choyamba awaweruze kuti apachikidwe ali moyo. Ndipo akatsala pang’ono kufa, awatsitse ndi kuwamaliza. (c) Ngati amangolanda chuma chokha popanda kupha, akagwidwa chiweruzo chawo nkuti adulidwe dzanja lakudzanjadzanja aliyense ndi phazi lakumanzere. Kapena dzanja lamanzere ndi phazi ladzanjadzanja (d) Ngati saapha ndiponso salanda chuma, koma amangovutitsa anthu ndi kuwaopseza, chiweruzo chawo nkuwachotsa m’dzikomo kuwapititsa kwina nkuwapatsa ukaidi kumeneko, kapena kuwanjata m’dziko momwemo.

التفاسير:

external-link copy
34 : 5

إِلَّا ٱلَّذِينَ تَابُواْ مِن قَبۡلِ أَن تَقۡدِرُواْ عَلَيۡهِمۡۖ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ

Kupatula amene alapa musanawagwire. Ndipo dziwani kuti Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha. info
التفاسير:

external-link copy
35 : 5

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱبۡتَغُوٓاْ إِلَيۡهِ ٱلۡوَسِيلَةَ وَجَٰهِدُواْ فِي سَبِيلِهِۦ لَعَلَّكُمۡ تُفۡلِحُونَ

E inu amene mwakhulupirira! Muopeni Allah ndipo funafunani njira zokufikitsani kwa Iye. Menyani nkhondo pa njira yake kuti mupambane. info
التفاسير:

external-link copy
36 : 5

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَوۡ أَنَّ لَهُم مَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا وَمِثۡلَهُۥ مَعَهُۥ لِيَفۡتَدُواْ بِهِۦ مِنۡ عَذَابِ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ مَا تُقُبِّلَ مِنۡهُمۡۖ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ

Ndithudi, aja amene sadakhulupirire, akadakhala ndi zonse za m’dziko ndi zina zonga izo kuti azipereke monga dipo kuti apulumuke kuchilango cha tsiku lachimaliziro (Qiyâma) sizikadavomerezedwa kwa iwo. Ndipo iwo adzapeza chilango chopweteka. info
التفاسير: