क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - ख़ालिद अबराहीम बेताला

पृष्ठ संख्या:close

external-link copy
3 : 5

حُرِّمَتۡ عَلَيۡكُمُ ٱلۡمَيۡتَةُ وَٱلدَّمُ وَلَحۡمُ ٱلۡخِنزِيرِ وَمَآ أُهِلَّ لِغَيۡرِ ٱللَّهِ بِهِۦ وَٱلۡمُنۡخَنِقَةُ وَٱلۡمَوۡقُوذَةُ وَٱلۡمُتَرَدِّيَةُ وَٱلنَّطِيحَةُ وَمَآ أَكَلَ ٱلسَّبُعُ إِلَّا مَا ذَكَّيۡتُمۡ وَمَا ذُبِحَ عَلَى ٱلنُّصُبِ وَأَن تَسۡتَقۡسِمُواْ بِٱلۡأَزۡلَٰمِۚ ذَٰلِكُمۡ فِسۡقٌۗ ٱلۡيَوۡمَ يَئِسَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن دِينِكُمۡ فَلَا تَخۡشَوۡهُمۡ وَٱخۡشَوۡنِۚ ٱلۡيَوۡمَ أَكۡمَلۡتُ لَكُمۡ دِينَكُمۡ وَأَتۡمَمۡتُ عَلَيۡكُمۡ نِعۡمَتِي وَرَضِيتُ لَكُمُ ٱلۡإِسۡلَٰمَ دِينٗاۚ فَمَنِ ٱضۡطُرَّ فِي مَخۡمَصَةٍ غَيۡرَ مُتَجَانِفٖ لِّإِثۡمٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ

Kwaletsedwa kwa inu (kudya) chakufa chokha, liwende, nyama ya nkhumba, chomwe chazingidwa m’dzina osati la Allah, chomwe chafa ndi kubanika, chomwe chafa ndi kumenyedwa, ndi chimene chafa pakugwa kuchokera pamwamba, chimene chafa polasidwa ndi nyanga (yachinzake), chomwe chafa pakujiwa ndi chilombo (cha m’thengo) kupatula chomwe mwachipeza chili rnoyobe nkuchizinga ndi chimene chazingidwa paguwa la mafano; ndiponso (nkoletsedwa kwa inu) kufuna kudziwa zobisika pochita maula. Zonsezi ndi uchimo. Lero amene sadakhulupirire ataya mtima (za kugonjetsa) chipembedzo chanu. Choncho musawaope, koma opani Ine. Lero ndakukwaniritsirani chipembedzo chanu ndipo ndakwaniritsa pa inu chisomo changa. Ndakusankhirani Chisilamu kukhala chipembedzo chanu. Koma amene wasimidwa chifukwa chanjala, popanda kupendekera kumachimo, (nkudya zoletsedwazi, palibe kanthu). Ndithu Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[156] info

[156] Nyama imene aizinga ndi cholinga china, osati ncholinga cha Allah monga:-
(1) Nyama imene aizinga chifukwa chotsirika nyumba kuti ziwanda zisamavutitsemo, kapena nyama imene aizinga pofuna kutsirika mudzi, kapena kuti chaka chino tikapanda kuzinga nyama kubwera matsoka akutiakuti
(2) Nyama imene aizinga pofuna kusangalatsa chiwanda cham’nyumba kapena cham’munda.
(3) Nyama imene aizinga pofuna kutsirika ukwati kuti ulimbe kapena pofuna kutsirika yemwe wabwera kuulendo kuti asamlodze.
(4) Nyama imene aizinga ncholinga choti akataye bwino maliro, ndi kuti mzimu wamalirowo usavutitse anthu pamudzi; nyama zonse zimene zazingidwa ndizolinga monga izi tatchulazi, nzoletsedwa kuzidya. Ndipo kunena koti: “Chimene chafa ndikumenyedwa ncholetsedwa koma pokhapokha mutachipeza chili moyobe nimuchizinga,” tanthauzo lake nkuti nyama imene imadyedwa ngati itafa pazifukwa zina zilizonse, monga kugundidwa ndi galimoto ndi zina zotero ndipo nyamayo sinaferetu kotero kuti nkutheka kuizinga, nyama yotero njololedwa kudya.

التفاسير:

external-link copy
4 : 5

يَسۡـَٔلُونَكَ مَاذَآ أُحِلَّ لَهُمۡۖ قُلۡ أُحِلَّ لَكُمُ ٱلطَّيِّبَٰتُ وَمَا عَلَّمۡتُم مِّنَ ٱلۡجَوَارِحِ مُكَلِّبِينَ تُعَلِّمُونَهُنَّ مِمَّا عَلَّمَكُمُ ٱللَّهُۖ فَكُلُواْ مِمَّآ أَمۡسَكۡنَ عَلَيۡكُمۡ وَٱذۡكُرُواْ ٱسۡمَ ٱللَّهِ عَلَيۡهِۖ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَۚ إِنَّ ٱللَّهَ سَرِيعُ ٱلۡحِسَابِ

Akukufunsa (Asilamu) chomwe chaloledwa kwa iwo (kudya). Nena: “Chaloledwa kwa inu chilichonse chabwino. Ndi (chimene chagwidwa ndi) nyama kapena mbalame zaukali zomwe mwaziphunzitsa kusaka. Muziphunzitse zimene Allah wakuphunzitsani. Choncho idyani chimene zakugwilirani, ndipo chitchulireni dzina la Allah pochikhwirizira. Ndipo opani Allah. Ndithudi Allah Ngwachangu pakuwerengera.[157] info

[157] Mbalame ndi nyama zimene zaloledwa kuzisaka mwaulenje kupyolera mwambalame kapena mwanyama zinzake zomwe anaziphunzitsa kusaka, ndipo mbalamezo kapena nyamazo nkufa chifukwa chakulumidwa ndi mbalame kapena nyama zosakazo, zikuloledwa kuzidya ngakhale kuti sanazizinge. Koma ngati atazipeza zikalipobe ndi moyo, azizinge.

التفاسير:

external-link copy
5 : 5

ٱلۡيَوۡمَ أُحِلَّ لَكُمُ ٱلطَّيِّبَٰتُۖ وَطَعَامُ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ حِلّٞ لَّكُمۡ وَطَعَامُكُمۡ حِلّٞ لَّهُمۡۖ وَٱلۡمُحۡصَنَٰتُ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ وَٱلۡمُحۡصَنَٰتُ مِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ مِن قَبۡلِكُمۡ إِذَآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ أُجُورَهُنَّ مُحۡصِنِينَ غَيۡرَ مُسَٰفِحِينَ وَلَا مُتَّخِذِيٓ أَخۡدَانٖۗ وَمَن يَكۡفُرۡ بِٱلۡإِيمَٰنِ فَقَدۡ حَبِطَ عَمَلُهُۥ وَهُوَ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ مِنَ ٱلۡخَٰسِرِينَ

Lero mwaloledwa zonse zabwino ndi chakudya cha omwe adapatsidwa buku nchololedwa kwa inu, ndiponso chakudya chanu nchololedwa kwa iwo, ndipo (mukuloledwa kuwakwatira) akazi abwino a mwa okhulupirira ndi akazi abwino a mwa omwe adapatsidwa ma buku kale, ngati mwawapatsa chiwongo chawo m’njira yomanga nawo ukwati, osati mochita nao chiwerewere, osatinso mochita nao zibwenzi. Ndipo amene akane kukhulupirira, ndiye kuti yaonongeka ntchito yake; ndipo iye tsiku lachimaliziro adzakhala mwa oluza (otaiyika).[158] info

[158] Chakudya chozingidwa sichingakhale chovomerezeka kwa Asilamu pokhapokha chitazingidwa ndi Asilamu. Izi zili ngati atatsatira malamulo akazingidwe, osati kupotokola khosi, kapena kumenya ndimyala kapena chibonga. Tsono chakudya chozingidwa nchovomerezeka kwa Msilamu kuchidya ngakhale chitakonzedwa ndi achikunja (akafiri) ngati:- (a) simudaone kuti athiramo najisi (uve) (b) Sichili chakudya choletsedwa. Nkovomerezeka kwa mwamuna wa Chisilamu kukwatira:- (a) Mkazi wa Chiyuda (b) Mkazi wa Chikhrisitu ngati makolo awo adali Ayuda kapena Akhrisitu chisilamu chisanadze.
N.B! Koma awa a Mishoni omwe alowa m’Chikhrisitu posachedwapa nkosaloledwa kuwakwatira pokhapokha atayamba alowa m’Chisilamu Tsono mkazi wa Chisilamu nkosaloledwa kukwatiwa ndi myuda kapena mkhrisitu. Ndipo apa apitirizanso machitidwe achiwerewere chomangira nyumba ndi chapatchire. Munthu akafuna kukwatira mkazi atsate mfundo zikudzazi kuti ukwati wakewo ukhale wovomerezeka pa malamulo a Chisilamu:- (a) Mkazi alole kukwatiwa ndi mwamunayo. (b) Myang’aniri wa wamkazi apereke kwa munthu chilolezo choti akwatitsire mkazi uja, kapena amkwatitse iye mwini pomuuza mkwati kuti “Ndakukwatitsa uje mwana wa uje.’’ (c) Mkwati avomereze kuti: “Ndavomera kumkwatira uje, mwana wa uje’.’ (d) Pakhale anthu aamuna oikira umboni osachepera pa awiri. Anthuwo akhale aulemu wawo pamaso pa anthu. (e) Chiperekedwe chiongo. (f) Iwerengedwe khutba ya ukwati.

التفاسير: