Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ

Numéro de la page:close

external-link copy
63 : 11

قَالَ يَٰقَوۡمِ أَرَءَيۡتُمۡ إِن كُنتُ عَلَىٰ بَيِّنَةٖ مِّن رَّبِّي وَءَاتَىٰنِي مِنۡهُ رَحۡمَةٗ فَمَن يَنصُرُنِي مِنَ ٱللَّهِ إِنۡ عَصَيۡتُهُۥۖ فَمَا تَزِيدُونَنِي غَيۡرَ تَخۡسِيرٖ

(Iye) adati: “E inu anthu anga! Mukuona bwanji ngati ndili ndi chisonyezo choonekera chochokera kwa Mbuye wanga (chosonyeza kuona kwa zimenezi), nandipatsanso chifundo chochokera kwa Iye. Nanga ndi yani angandipulumutse ku chilango cha Allah ngati nditamunyoza? Choncho, simungandionjezere china chake koma kutaika basi.” info
التفاسير:

external-link copy
64 : 11

وَيَٰقَوۡمِ هَٰذِهِۦ نَاقَةُ ٱللَّهِ لَكُمۡ ءَايَةٗۖ فَذَرُوهَا تَأۡكُلۡ فِيٓ أَرۡضِ ٱللَّهِۖ وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابٞ قَرِيبٞ

“Ndipo E inu anthu anga! Iyi ngamira ya Allah ndi chisonyezo kwa inu. Ilekeni izidya panthaka ya Allah, ndipo musaikhudze ndi choipa kuopa kuti chilango chomwe chili pafupi chingakuonongeni.”[224] info

[224] Asamudu adampempha chozizwitsa Mneneri wawo Swalih chotsimikiza kuti iye adalidi Mneneri wa Allah. Chozizwitsa chomwe adampempha nkuti atulutse ngamira patanthwe. Choncho mwa mphamvu za Allah ngamira idatuluka m’tanthwemo. Ndipo adawauza kuti asaichitire choipa. Aisiye izingodzidyera m’dziko la Allah. Koma iwo adaipha, ndipo chilango cha Allah chidawatsikira.

التفاسير:

external-link copy
65 : 11

فَعَقَرُوهَا فَقَالَ تَمَتَّعُواْ فِي دَارِكُمۡ ثَلَٰثَةَ أَيَّامٖۖ ذَٰلِكَ وَعۡدٌ غَيۡرُ مَكۡذُوبٖ

Koma adaipha. Choncho (Swaleh) adati: “Sangalalani m’midzi yanuyi pamasiku atatu. (Kenako mulangidwa). Limenelo ndi lonjezo osati labodza.” info
التفاسير:

external-link copy
66 : 11

فَلَمَّا جَآءَ أَمۡرُنَا نَجَّيۡنَا صَٰلِحٗا وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَهُۥ بِرَحۡمَةٖ مِّنَّا وَمِنۡ خِزۡيِ يَوۡمِئِذٍۚ إِنَّ رَبَّكَ هُوَ ٱلۡقَوِيُّ ٱلۡعَزِيزُ

Choncho pamene lamulo Lathu lidadza (lakuononga midziyo), tidampulumutsa Swalih ndi anthu amene adakhulupirira naye, kukuyaluka kwa tsiku limenelo, mwa chifundo Chathu. Ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu, Ngopambana. info
التفاسير:

external-link copy
67 : 11

وَأَخَذَ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ ٱلصَّيۡحَةُ فَأَصۡبَحُواْ فِي دِيَٰرِهِمۡ جَٰثِمِينَ

Ndipo amene adadzichitira okha zoipa phokoso lalikulu lidawaononga, tero kudawachera m’nyumba zawo ali lambilambi (atafa). info
التفاسير:

external-link copy
68 : 11

كَأَن لَّمۡ يَغۡنَوۡاْ فِيهَآۗ أَلَآ إِنَّ ثَمُودَاْ كَفَرُواْ رَبَّهُمۡۗ أَلَا بُعۡدٗا لِّثَمُودَ

Ngati kuti iwo mudalibemo m’menemo. Mverani! Ndithu Asamudu adamkana Mbuye wawo. Choncho Asamudu adaonongeka. info
التفاسير:

external-link copy
69 : 11

وَلَقَدۡ جَآءَتۡ رُسُلُنَآ إِبۡرَٰهِيمَ بِٱلۡبُشۡرَىٰ قَالُواْ سَلَٰمٗاۖ قَالَ سَلَٰمٞۖ فَمَا لَبِثَ أَن جَآءَ بِعِجۡلٍ حَنِيذٖ

Ndipo ndithu atumiki athu (angelo) adadza kwa Ibrahim ndi uthenga wabwino. (Iwo) adati: “Mtendere!” (Iye) adayankha: “Mtendere (ukhale pa inu!)” Ndipo (Ibrahim) sadakhalitse (adafulumira) kudza nayo nyama yootcha ya thole (mwana wa ng’ombe). info
التفاسير:

external-link copy
70 : 11

فَلَمَّا رَءَآ أَيۡدِيَهُمۡ لَا تَصِلُ إِلَيۡهِ نَكِرَهُمۡ وَأَوۡجَسَ مِنۡهُمۡ خِيفَةٗۚ قَالُواْ لَا تَخَفۡ إِنَّآ أُرۡسِلۡنَآ إِلَىٰ قَوۡمِ لُوطٖ

Koma pamene adaona kuti manja awo sakuwatambasula kuchakudya adawadodoma, nadzadzidwa nawo mantha. (Iwo) Adati: “Usaope; ndithu ife tatumidwa kwa anthu a Luti (kuti tikawaononge ndiponso kukupatsa nkhani yabwino).” info
التفاسير:

external-link copy
71 : 11

وَٱمۡرَأَتُهُۥ قَآئِمَةٞ فَضَحِكَتۡ فَبَشَّرۡنَٰهَا بِإِسۡحَٰقَ وَمِن وَرَآءِ إِسۡحَٰقَ يَعۡقُوبَ

Ndipo (m’menemo nkuti) mkazi wake (wa Ibrahim) ali chiimire, ndipo adaseka. Kenaka tidamuuza uthenga wabwino (wakubadwa kwa) Ishaq ndipo pambuyo pa Ishaq, Ya’qub. info
التفاسير: