Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ.

At-Tâghabun

external-link copy
1 : 64

يُسَبِّحُ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۖ لَهُ ٱلۡمُلۡكُ وَلَهُ ٱلۡحَمۡدُۖ وَهُوَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ

Zonse zakumwamba ndi zam’dziko lapansi zikulemekeza Allah (ndi kumyeretsa ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero Wake; ufumu Ngwake ndipo kutamandidwa kwabwino Nkwake. Ndipo Iye ali ndi mphamvu pa chilichonse. info
التفاسير:

external-link copy
2 : 64

هُوَ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ فَمِنكُمۡ كَافِرٞ وَمِنكُم مُّؤۡمِنٞۚ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٌ

Iye ndiamene adakulengani (nonsenu popanda kuchokera ku chilichonse) choncho mwa inu alipo wosakhulupirira ndiponso mwa inu alipo wokhulupirira. Ndipo Allah Ngopenya zonse zimene mukuchita (ndipo adzakulipirani nazo). info
التفاسير:

external-link copy
3 : 64

خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ بِٱلۡحَقِّ وَصَوَّرَكُمۡ فَأَحۡسَنَ صُوَرَكُمۡۖ وَإِلَيۡهِ ٱلۡمَصِيرُ

Adalenga thambo ndi nthaka mwachoonadi ndipo adakujambulani majambulidwe abwino; ndipo kobwerera nkwa Iye (pa tsiku lachiweruziro). info
التفاسير:

external-link copy
4 : 64

يَعۡلَمُ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَيَعۡلَمُ مَا تُسِرُّونَ وَمَا تُعۡلِنُونَۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ

(Allah) akudziwa za kumwamba ndi za m’dziko lapansi, ndiponso akudziwa zimene mukuzibisa ndi zimene mukuzilengeza (zochita ndi zoyankhula); Allah Ngodziwa za m’zifuwa. info
التفاسير:

external-link copy
5 : 64

أَلَمۡ يَأۡتِكُمۡ نَبَؤُاْ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَبۡلُ فَذَاقُواْ وَبَالَ أَمۡرِهِمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ

Kodi siidakufikeni nkhani ya omwe sadakhulupirire kale? Adalawa (zowawa) za zoipa za zinthu zawo (pa dziko lapansi). Ndipo chilango chowawa chidzakhala pa iwo (tsiku lachimaliziro). info
التفاسير:

external-link copy
6 : 64

ذَٰلِكَ بِأَنَّهُۥ كَانَت تَّأۡتِيهِمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ فَقَالُوٓاْ أَبَشَرٞ يَهۡدُونَنَا فَكَفَرُواْ وَتَوَلَّواْۖ وَّٱسۡتَغۡنَى ٱللَّهُۚ وَٱللَّهُ غَنِيٌّ حَمِيدٞ

Zimenezo nchifukwa chakuti atumiki awo amawadzera ndi zozizwitsa koma iwo amanena (mwachipongwe): “Ha! Anthu anzathu (onga ife) angationgole?” Choncho sadakhulupirire (utumiki wawo) ndipo adanyoza (choonadi) potero Allah adawasiya (ndi kupanda chikhulupiliro kwawo) ndipo Allah Ngokwanira ndiponso Ngoyamikidwa. info
التفاسير:

external-link copy
7 : 64

زَعَمَ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ أَن لَّن يُبۡعَثُواْۚ قُلۡ بَلَىٰ وَرَبِّي لَتُبۡعَثُنَّ ثُمَّ لَتُنَبَّؤُنَّ بِمَا عَمِلۡتُمۡۚ وَذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٞ

Amene sadakhulupirire akumazinamiza kuti sadzaukitsidwa ku imfa. Nena (kwa iwo iwe Mtumiki{s.a.w}): “Sizili choncho pali Mbuye wanga, ndithu mudzaukitsidwa ku imfa, ndipo mudzauzidwa zimene mumachita (pa dziko lapansi). Zimenezo kwa Allah nzosavuta (kuzichita).” info
التفاسير:

external-link copy
8 : 64

فَـَٔامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَٱلنُّورِ ٱلَّذِيٓ أَنزَلۡنَاۚ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٞ

Khulupirirani Allah ndi Mtumiki Wake, ndi dangalira limene talivumbulutsa (Qur’an). Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita. info
التفاسير:

external-link copy
9 : 64

يَوۡمَ يَجۡمَعُكُمۡ لِيَوۡمِ ٱلۡجَمۡعِۖ ذَٰلِكَ يَوۡمُ ٱلتَّغَابُنِۗ وَمَن يُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ وَيَعۡمَلۡ صَٰلِحٗا يُكَفِّرۡ عَنۡهُ سَيِّـَٔاتِهِۦ وَيُدۡخِلۡهُ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ

(Kumbukirani) tsiku limene adzakusonkhanitsani chifukwa cha tsiku lakusonkhana (zolengedwa zonse), limenelo ndi tsiku lolephera; ndipo amene akhulupirira mwa Allah ndi kuchita zabwino, amfafanizira zoipa zake, ndipo akamulowetsa m’minda momwe pansi pake pakuyenda mitsinje; adzakhala m’menemo muyaya; kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.[365] info

[365] Tsiku lolephera: Akafiri adzakhala olephera chifukwa cha kusakhulupilira kwawo. Nawonso Asilamu aulesi adzakhala olephera chifukwa cha kusakwaniritsa kwawo malamulo a Allah.

التفاسير:

external-link copy
10 : 64

وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَآ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِ خَٰلِدِينَ فِيهَاۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ

Koma amene sadakhulupirire natsutsa zozizwitsa Zathu (zimene zidaperekedwa kwa Aneneri Athu;) iwowo ndi anthu a ku Moto; adzakhala mmenemo nthawi yaitali, amenewo ndiwo mabwelero oipa. info
التفاسير:

external-link copy
11 : 64

مَآ أَصَابَ مِن مُّصِيبَةٍ إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِۗ وَمَن يُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ يَهۡدِ قَلۡبَهُۥۚ وَٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٞ

Palibe vuto lililonse lingapezeke pokhapokha Allah atafuna; ndipo amene akhulupirira Allah, (Allah) aongola mtima wake (kuti ukhale wokhutira ndi chiweruzo cha Allah). Ndipo Allah Ngodziwa chinthu chilichonse. info
التفاسير:

external-link copy
12 : 64

وَأَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَۚ فَإِن تَوَلَّيۡتُمۡ فَإِنَّمَا عَلَىٰ رَسُولِنَا ٱلۡبَلَٰغُ ٱلۡمُبِينُ

Choncho mverani Allah ndipo mverani Mtumiki, ngati munyozera (ndi zanu), ndithu udindo wa Mtumiki Wathu ndikufikitsa uthenga omveka. info
التفاسير:

external-link copy
13 : 64

ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ

Allah, palibe wina wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Ndipo kwa Allah Yekha, okhulupirira atsamire. info
التفاسير:

external-link copy
14 : 64

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِنَّ مِنۡ أَزۡوَٰجِكُمۡ وَأَوۡلَٰدِكُمۡ عَدُوّٗا لَّكُمۡ فَٱحۡذَرُوهُمۡۚ وَإِن تَعۡفُواْ وَتَصۡفَحُواْ وَتَغۡفِرُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ

E inu amene mwakhulupirira! Ndithu ena mwa akazi anu ndi ana anu ndiadani anu (chifukwa chakuti amakuchotsani kumbali yomvera Allah pofuna kuti mukwaniritse zofuna zawo). Chenjerani nawo. Ngati muwakhululukira ndi kunyalanyaza ndi kubisa zolakwa zawo ndibwino kwambiri, ndithu Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.[366] info

[366] (Ndime 14-15) Pakufunika kuti munthu akhale ndi muyeso wabwino. Chinthu chilichonse achipatse choyenera chake. Nthawi zambiri kumapezeka kuti munthu amalakwira Allah chifukwa cha kufunitsitsa chuma, kapena chifukwa chofuna kukondweretsa ana ake ndi mkazi wake ndi kunyalanyaza malamulo a Allah. Choncho apa, chuma chake, ana ake ndi mkazi wake amasanduka adani ake okamuika m’mavuto kwa Allah. Nkofunika kwa munthu kukondweretsa Allah ndi kumkonda asanakondweretse ndi kukonda china chilichonse.

التفاسير:

external-link copy
15 : 64

إِنَّمَآ أَمۡوَٰلُكُمۡ وَأَوۡلَٰدُكُمۡ فِتۡنَةٞۚ وَٱللَّهُ عِندَهُۥٓ أَجۡرٌ عَظِيمٞ

Ndithu chuma chanu ndi ana anu ndimayesero (kwa inu); koma kwa Allah kuli malipiro akulu (kwa yemwe wasankha kumvera Allah). info
التفاسير:

external-link copy
16 : 64

فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ مَا ٱسۡتَطَعۡتُمۡ وَٱسۡمَعُواْ وَأَطِيعُواْ وَأَنفِقُواْ خَيۡرٗا لِّأَنفُسِكُمۡۗ وَمَن يُوقَ شُحَّ نَفۡسِهِۦ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ

Choncho muopeni Allah mmene mungathere, mverani (zophunzitsa Zake) ndipo tsatirani (malamulo Ake) komanso perekani zimene wakupatsani zikhala zabwino kwa inu. Dzichitireni nokha zabwino. Ndipo amene watchinjirizidwa ku umbombo wa mtima wake, iwowo ndiwo opambana. info
التفاسير:

external-link copy
17 : 64

إِن تُقۡرِضُواْ ٱللَّهَ قَرۡضًا حَسَنٗا يُضَٰعِفۡهُ لَكُمۡ وَيَغۡفِرۡ لَكُمۡۚ وَٱللَّهُ شَكُورٌ حَلِيمٌ

Ngati mungamkongoze Allah ngongole yabwino aiwonjezera kwa inu (malipiro ake) ndipo akukhululukirani (zolakwa zanu.) Ndipo Allah Ngolandira kuthokoza, Ngoleza. info
التفاسير:

external-link copy
18 : 64

عَٰلِمُ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ

Ngodziwa zobisika ndi zoonekera, Ngwamphamvu zopambana, Ngwanzeru zakuya. info
التفاسير: