Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ.

Al-Hashr

external-link copy
1 : 59

سَبَّحَ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۖ وَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ

Zonse za kumwamba ndi za pansi zimalemekeza Allah (ndi kumuyeretsa ku khalidwe losayenera ndi ulemelero Wake). Ndipo Iye Ngopambana (salephera kanthu), Ngwaluntha (m’kakonzedwe Kake ndi m’zochita Zake). info
التفاسير:

external-link copy
2 : 59

هُوَ ٱلَّذِيٓ أَخۡرَجَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ مِن دِيَٰرِهِمۡ لِأَوَّلِ ٱلۡحَشۡرِۚ مَا ظَنَنتُمۡ أَن يَخۡرُجُواْۖ وَظَنُّوٓاْ أَنَّهُم مَّانِعَتُهُمۡ حُصُونُهُم مِّنَ ٱللَّهِ فَأَتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِنۡ حَيۡثُ لَمۡ يَحۡتَسِبُواْۖ وَقَذَفَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلرُّعۡبَۚ يُخۡرِبُونَ بُيُوتَهُم بِأَيۡدِيهِمۡ وَأَيۡدِي ٱلۡمُؤۡمِنِينَ فَٱعۡتَبِرُواْ يَٰٓأُوْلِي ٱلۡأَبۡصَٰرِ

Iye ndi Amene adatulutsa osakhulupirira ena mwa anthu a buku m’nyumba zawo mkusamusidwa koyamba (pa chilumba cha Arabu). Simunkaganizira kuti angatuluke (m’nyumba zawozo). Ndipo iwo amaganiza kuti malinga awo awateteza kwa Allah. Koma Allah adawalanga kupyolera mmene samayembekezera, ndipo adathira mantha oopsa m’mitima mwawo (potumiza Mtumiki Wake kwa iwo), adagumula nyumba zawo ndi manja awo ndi manja a okhulupirira. Choncho lingalirani (zimenezi) E inu eni nzeru! [353] info

[353] Ayah imeneyi ikulongosola nkhani ya kusamutsidwa kwa Ayuda otchedwa Bani Nadhir mu mzinda wa Madina. Ayuda adasamutsidwa mu mzinda wa Madina chifukwa cha kuswa mapangano okhalirana mwa mtendere ndi Asilamu.

التفاسير:

external-link copy
3 : 59

وَلَوۡلَآ أَن كَتَبَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِمُ ٱلۡجَلَآءَ لَعَذَّبَهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابُ ٱلنَّارِ

Ndipo kukadapanda kuti Allah adawalembera (pachiyambi) kusamuka (m’nyumba zawo), akadawalanga pa dziko pompano; koma chilango cha Moto chili pa iwo tsiku lachimaliziro. info
التفاسير: