[257] Omasulira Qur’an adati:- Adalowa kuphangako nthawi yam’bandakucha, ndipo Allah adawaukitsa madzulo. Ichi nchifukwa chake ena ankati akhala theka la tsiku poganizira kuti adakhalamo usana umodzi, pomwe ena amati adakhala tsiku lathunthu. Kenako nati Allah ndi amene akudziwa nyengo imene takhalamo. Ndime iyi ndiumboni waukulu wotsimikiza kuti mizimu ya anthu abwino sidzaona kutalika nyengo yokhalira m’manda.