[201] M’chaka chachisanu nchimodzi (6) chakusamuka, Mtumiki (s.a.w) pamodzi ndi omtsatira ake ochuluka zedi adapita ku Makka ncholinga chokachita mapemphero a Umra. Koma Aquraish adamuletsa kulowa mu mzinda wa Makka podziganizira kuti iwo ndiwo oyang’anira Kaaba.