ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا

رقم الصفحة:close

external-link copy
46 : 8

وَأَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَلَا تَنَٰزَعُواْ فَتَفۡشَلُواْ وَتَذۡهَبَ رِيحُكُمۡۖ وَٱصۡبِرُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلصَّٰبِرِينَ

Ndipo mumvereni Allah ndi Mtumiki Wake, musakangane (kuopera kuti) mungakhale olephera (ndi kutaya mtima), ndikuchoka mphamvu zanu. Koma pitirizani kupirira. Ndithudi, Allah ali pamodzi ndi anthu opirira. info
التفاسير:

external-link copy
47 : 8

وَلَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ خَرَجُواْ مِن دِيَٰرِهِم بَطَرٗا وَرِئَآءَ ٱلنَّاسِ وَيَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ وَٱللَّهُ بِمَا يَعۡمَلُونَ مُحِيطٞ

Ndipo musakhale ngati anthu amene anatuluka m’nyumba zawo modzikweza ndi modzionetsera kwa anthu, ndikuwasekereza anthu kuyenda pa njira ya Allah. Koma Allah ndi Wodziwa kwambiri zimene akuchita. info
التفاسير:

external-link copy
48 : 8

وَإِذۡ زَيَّنَ لَهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ أَعۡمَٰلَهُمۡ وَقَالَ لَا غَالِبَ لَكُمُ ٱلۡيَوۡمَ مِنَ ٱلنَّاسِ وَإِنِّي جَارٞ لَّكُمۡۖ فَلَمَّا تَرَآءَتِ ٱلۡفِئَتَانِ نَكَصَ عَلَىٰ عَقِبَيۡهِ وَقَالَ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّنكُمۡ إِنِّيٓ أَرَىٰ مَا لَا تَرَوۡنَ إِنِّيٓ أَخَافُ ٱللَّهَۚ وَٱللَّهُ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ

Ndipo (kumbukira) pamene satana adawakometsera zochita zawo zoipa (aja osakhulupirira) nati: “Lero palibe aliyense mwa anthu amene angakugonjetseni, ndipo ine ndine mtetezi wanu.” Koma pamene magulu awiri ankhondo anaonana (anakumana pamaso ndi pamaso) satana anabwerera pambuyo (kuthawa) nati: “Ine ndikudzipatula mwa inu. Ndithu ine ndikuona zimene inu simukuziona. Ndithu ine ndikuopa Allah.” Ndipo Allah Ngwaukali polanga. info
التفاسير:

external-link copy
49 : 8

إِذۡ يَقُولُ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ وَٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٌ غَرَّ هَٰٓؤُلَآءِ دِينُهُمۡۗ وَمَن يَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱللَّهِ فَإِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ

(Kumbukirani) pamene achiphamaso ndi amene ali ndi matenda m’mitima mwawo amanena: “Anthu awa chipembedzo chawo (cha Chisilamu) chawanyenga.” Komatu amene akuyadzamira kwa Allah ndithudi Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya. info
التفاسير:

external-link copy
50 : 8

وَلَوۡ تَرَىٰٓ إِذۡ يَتَوَفَّى ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ يَضۡرِبُونَ وُجُوهَهُمۡ وَأَدۡبَٰرَهُمۡ وَذُوقُواْ عَذَابَ ٱلۡحَرِيقِ

Ndipo ukadaona angelo pamene akuchotsa miyoyo ya anthu amene sadakhulupirire (pa imfa yawo) uku akumenya kunkhope zawo ndi kumisana yawo (uku akunena): “Lawani chilango cha Moto woocha. (Ukadaziona zoopsa kwabasi).” info
التفاسير:

external-link copy
51 : 8

ذَٰلِكَ بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيكُمۡ وَأَنَّ ٱللَّهَ لَيۡسَ بِظَلَّٰمٖ لِّلۡعَبِيدِ

“Izo ndi chifukwa cha (machimo) amene manja anu anawatsogoza, ndipo Allah sali opondereza akapolo (Ake).”[203] info

[203] Mizimu ya osakhulupilira ikamachotsedwa, imachotsedwa mwamasautso kwambiri. Koma amene ali pafupi ndi wakufayo saona zimenezi pakuti ife sititha kuiona mizimu ndi zonse zokhudzana ndi mizimu. Ife timangoona thupi lawakufayo poliona thupilo likuzunzika. Kuzunzika kwa mzimu sindiko kuzunzika kwa thupi. Choncho kuzunzika komwe kukunenedwa apa nkuzunzika kwa mzimu komwe kumaapeza anthu osakhulupilira. Komatu masautso athupi amene amawapeza anthu ena panthawi ya imfa pophuphaphupha, sasonyeza kusalungama kwa munthuyo. Koma amasonyeza mphamvu zomwe zidali m’thupi mwa munthuyo. Sizikhudzana ndi kulungama kwake ndi kusalungama kwake. Mungawaone anthu oipa akufa ndi imfa yodekha pomwe amene adali abwino akufa ndi imfa yophuphaphupha ndikudzimenyamenya. Choncho kuphuphaphupha kumeneko nkwathupi chifukwa chokhala ndi mphamvu. Choncho tisadodome pomwe tiona munthu wabwino akuphuphaphupha.

التفاسير:

external-link copy
52 : 8

كَدَأۡبِ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ وَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡۚ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ فَأَخَذَهُمُ ٱللَّهُ بِذُنُوبِهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ قَوِيّٞ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ

(Khalidwe lawo awa lili ) ngati khalidwe la anthu a Farawo ndi omwe adalipo patsogolo pawo. Anazikana zizindikiro za Allah, choncho Allah anawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndithudi Allah Ngwamphamvu, Wolanga moopsa. info
التفاسير: