Ndipo m’menemo (m’buku la Taurat) tidawalamula kuti: “Munthu aphedwe chifukwa chopha mnzake, ndi kuti diso kwa diso, mphuno kwa mphuno; khutu kwa khutu; dzino kwa dzino, ndiponso kubwezerana mabala.” Koma amene wakhululuka ndiye kuti dipo likhala kwa iye. Ndipo amene saweruza ndi chimene Allah wavumbulutsa iwowo ndiwo anthu ochita zoipa.