Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима

Бет рақами:close

external-link copy
44 : 12

قَالُوٓاْ أَضۡغَٰثُ أَحۡلَٰمٖۖ وَمَا نَحۡنُ بِتَأۡوِيلِ ٱلۡأَحۡلَٰمِ بِعَٰلِمِينَ

(Iwo) adati: “Amenewa ndi maloto osakanikirana (simaloto omveka)! Ndipo ife sitili odziwa kumasulira maloto amtundu umenewu.” info
التفاسير:

external-link copy
45 : 12

وَقَالَ ٱلَّذِي نَجَا مِنۡهُمَا وَٱدَّكَرَ بَعۡدَ أُمَّةٍ أَنَا۠ أُنَبِّئُكُم بِتَأۡوِيلِهِۦ فَأَرۡسِلُونِ

Pamenepo amene adapulumuka mwa awiri aja adanena atakumbukira (pempho la Yûsuf) patapita nyengo (yaitali), adati: “Ine ndikuuzani tanthauzo lake. Choncho nditumeni (kuti ndikakufunireni tanthauzo lake).” info
التفاسير:

external-link copy
46 : 12

يُوسُفُ أَيُّهَا ٱلصِّدِّيقُ أَفۡتِنَا فِي سَبۡعِ بَقَرَٰتٖ سِمَانٖ يَأۡكُلُهُنَّ سَبۡعٌ عِجَافٞ وَسَبۡعِ سُنۢبُلَٰتٍ خُضۡرٖ وَأُخَرَ يَابِسَٰتٖ لَّعَلِّيٓ أَرۡجِعُ إِلَى ٱلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَعۡلَمُونَ

(Adanka kundende ndikumpempha Yûsuf chikhululuko chifukwa cha kuiwala kwake. Ndipo adati): “Yûsuf! E iwe woona! Tiuze za ng’ombe zisanu ndi ziwiri zonenepa zikudyedwa ndi zisanu ndi ziwiri zoonda, ndi ngala zisanu ndi ziwiri zaziwisi ndi zina zouma; kuti ine ndibwelere kwa anthu kuti akadziwe.” info
التفاسير:

external-link copy
47 : 12

قَالَ تَزۡرَعُونَ سَبۡعَ سِنِينَ دَأَبٗا فَمَا حَصَدتُّمۡ فَذَرُوهُ فِي سُنۢبُلِهِۦٓ إِلَّا قَلِيلٗا مِّمَّا تَأۡكُلُونَ

(Yûsuf) adati: “Mudzalima zaka zisanu ndi ziwiri mondondozana ndi mwakhama ndipo zimene mwakolola zisiyeni m’ngala zake, kupatula zochepa zimene muzidzadya (kuti zam’ngalazo mudzadye mzaka zanjala).” info
التفاسير:

external-link copy
48 : 12

ثُمَّ يَأۡتِي مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ سَبۡعٞ شِدَادٞ يَأۡكُلۡنَ مَا قَدَّمۡتُمۡ لَهُنَّ إِلَّا قَلِيلٗا مِّمَّا تُحۡصِنُونَ

“Kenako pambuyo pake zidzadza zaka zisanu ndi ziwiri za masautso zomwe zidzadya zimene mudasunga m’mbuyo, kupatula zochepa zimene muzidzazisunga (mobisa kuti zidzakhale mbewu.)” info
التفاسير:

external-link copy
49 : 12

ثُمَّ يَأۡتِي مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ عَامٞ فِيهِ يُغَاثُ ٱلنَّاسُ وَفِيهِ يَعۡصِرُونَ

“Kenako pambuyo pa izi chidzadza chaka chomwe anthu m’menemo adzapulumutsidwa (ndi Allah), ndipo m’menemo adzafinya (zakumwa).” info
التفاسير:

external-link copy
50 : 12

وَقَالَ ٱلۡمَلِكُ ٱئۡتُونِي بِهِۦۖ فَلَمَّا جَآءَهُ ٱلرَّسُولُ قَالَ ٱرۡجِعۡ إِلَىٰ رَبِّكَ فَسۡـَٔلۡهُ مَا بَالُ ٱلنِّسۡوَةِ ٱلَّٰتِي قَطَّعۡنَ أَيۡدِيَهُنَّۚ إِنَّ رَبِّي بِكَيۡدِهِنَّ عَلِيمٞ

Ndipo mfumu idati: “M’bweretseni iye kwa ine.” Koma pamene mthenga (wa Mfumu) adamfika (Yûsuf, iye) adati: “Bwerera kwa bwana wako ndipo ukamfunse nkhani ya akazi omwe ankadzicheka manja awo. Ndithu Mbuye wanga akudziwa bwino ndale zawo. (Koma ndikufuna Mfumu kuti idziwe za kuyera kwanga kuti andiyeretsere maganizo ndipo asandiope).” info
التفاسير:

external-link copy
51 : 12

قَالَ مَا خَطۡبُكُنَّ إِذۡ رَٰوَدتُّنَّ يُوسُفَ عَن نَّفۡسِهِۦۚ قُلۡنَ حَٰشَ لِلَّهِ مَا عَلِمۡنَا عَلَيۡهِ مِن سُوٓءٖۚ قَالَتِ ٱمۡرَأَتُ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡـَٰٔنَ حَصۡحَصَ ٱلۡحَقُّ أَنَا۠ رَٰوَدتُّهُۥ عَن نَّفۡسِهِۦ وَإِنَّهُۥ لَمِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ

(Mfumu idasonkhanitsa akazi aja ndipo) idati: “Kodi nkhani yanu njotani pamene mudamulakalaka Yûsuf pomwe iye sakufuna?” Adati: “Hasha Lillah! (Tikudzitchinjiriza kwa Allah)! Ife sitidadziwe choipa chilichonse kwa iye. (Tidayesayesa kuti achite nafe choipa koma sadalole).” (Nayenso) mkazi wa nduna adati: “Tsopano choonadi chatsimikizika; ine ndine amene ndidamulakalaka pomwe iye sakufuna. Ndithu iye ndi mmodzi mwa owona.” info
التفاسير:

external-link copy
52 : 12

ذَٰلِكَ لِيَعۡلَمَ أَنِّي لَمۡ أَخُنۡهُ بِٱلۡغَيۡبِ وَأَنَّ ٱللَّهَ لَا يَهۡدِي كَيۡدَ ٱلۡخَآئِنِينَ

(Yûsuf adati): “Zimenezo (zofuna kuti afunsidwe chonchi) n’chifukwa chakuti (nduna) idziwe kuti ine sindidaichitire zoipa iyo kulibe, ndi kuti Allah saongolera ndale za anthu achinyengo (kuti zipambane).” info
التفاسير: