قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا

Al-Qamar

external-link copy
1 : 54

ٱقۡتَرَبَتِ ٱلسَّاعَةُ وَٱنشَقَّ ٱلۡقَمَرُ

Nthawi ya chimaliziro (Qiyâma) yayandikira ndipo mwezi wagawikana. info
التفاسير:

external-link copy
2 : 54

وَإِن يَرَوۡاْ ءَايَةٗ يُعۡرِضُواْ وَيَقُولُواْ سِحۡرٞ مُّسۡتَمِرّٞ

Koma akaona chozizwitsa akunyoza ndi kunena kuti: “Awa ndi matsenga womkeramkera patsogolo.” info
التفاسير:

external-link copy
3 : 54

وَكَذَّبُواْ وَٱتَّبَعُوٓاْ أَهۡوَآءَهُمۡۚ وَكُلُّ أَمۡرٖ مُّسۡتَقِرّٞ

Ndipo adatsutsa (choonadi) ndi kutsatira zilakolako (zawo zoipa) koma chinthu chilichonse (cha Allah) nchokhazikika. info
التفاسير:

external-link copy
4 : 54

وَلَقَدۡ جَآءَهُم مِّنَ ٱلۡأَنۢبَآءِ مَا فِيهِ مُزۡدَجَرٌ

Ndipo ndithu zidawafika nkhani zomwe zili zokwanira kuwaopseza. info
التفاسير:

external-link copy
5 : 54

حِكۡمَةُۢ بَٰلِغَةٞۖ فَمَا تُغۡنِ ٱلنُّذُرُ

Nzeru zokwana koma machenjezo (kwa iwo) sanawathandize. info
التفاسير:

external-link copy
6 : 54

فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡۘ يَوۡمَ يَدۡعُ ٱلدَّاعِ إِلَىٰ شَيۡءٖ نُّكُرٍ

Choncho, apewe (iwe Mtumiki) osakhulupirira, (yembekezani) tsiku loitana woitana (wa Allah) ku chinthu chovuta kwambiri, (chodedwa ndi mitima). info
التفاسير: