[112] Apa akufotokoza za kagawidwe ka chuma chamasiye (mirath).
a) Ngati munthu wamwalira nkusiya ana amuna ndi akazi tero mwana wamwamuna adzapeza magawo awiri ndipo wamkazi adzapeza gawo limodzi.
b) Munthu akafa nkusiya ana akazi okha, awiri kapena ochulukirapo, anawo adzatenga magawo awiri achumacho. Ndipo onsewo alandire mofanana. Pasapezeke wotenga zochuluka kuposa wina.
Tsono gawo lomwe latsala lidzaperekedwa kwa ena oti awagawire ngati alipo. Ngati palibe, ndiye kuti gawolo lidzaperekedwanso kwa ana akaziwo.
N.B Magawo awiri m’magawo atatu (2/3), apa akutanthauza kuti chuma chonsecho amachigawa m’magawo atatu ofanana. Ndipo akaziwo nkulandira magawo awiri mwa magawo atatuwo.
c) Ngati munthu atamwalira nkusiya mwana mmodzi wamkazi, ndiye kuti chumacho achigawe magawo awiri ofanana. Gawo limodzi mwa magawo awiri aja alipereke kwa mwana wamkaziyo. Ndipo gawo lotsalalo alipereke kwa ena ofunika kuwagawira ngati alipo. Ngati palibe, aliperekenso kwa mwana yemweyo. Lamulo la adzukulu likufanana ndi lamulo la ana ngati wakufayo adalibe ana koma adzukulu ake okha.
d) Munthu akafa nkusiya ana ndi makolo ake, (tate ndi mayi), tero tate adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) a chumacho. Nayenso mayi adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo chuma chotsalacho adzalandira ndi ana kapena adzukulu a muntnu wakufayo.
e) Munthu akafa nkusiya tate wake ndi mayi wake basi, popanda ana ndi adzukulu choncho apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo atatu a chumacho. Ndipo tate adzatenga magawo awiri.
f) Munthu akafa nkusiya mayi wake yekha ndi abale ake obadwa nawo kwa mayi ndi bambo mmodzi, kapena akumbali ya kwabambo okha kapena akumbali yamayi okha, apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi a chumacho. Anthu oyenera kuwagawira chuma chamasiye asawagawire msanga chumacho mpaka ngongole zonse za wakufayo atazibweza. Ndiponso mpaka apereke chilawo (wasiya) chomwe wakufayo adanena kuti chidzachitike. Owagawira chumawo asakhale anthu osusuka ndi chumacho. choyamba aonetsetse kuti izi zonse zakwaniritsidwa. Komatu chilawocho chisapyole pagawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho. Chikapyolera pamenepa ndiye kuti choonjezerapocho sichivomerezedwa.