Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - Çevaca Tercüme - Halid İbrahim Pitala

external-link copy
63 : 12

فَلَمَّا رَجَعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيهِمۡ قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا مُنِعَ مِنَّا ٱلۡكَيۡلُ فَأَرۡسِلۡ مَعَنَآ أَخَانَا نَكۡتَلۡ وَإِنَّا لَهُۥ لَحَٰفِظُونَ

Ndipo pamene adabwerera kwa bambo wawo, adati: “E bambo wathu! Tikamanidwa muyeso wa chakudya (pa ulendo wachiwiri pokhapokha titsagane ndi m’bale wathuyu). Choncho mtumizeni m’bale wathu pamodzi ndi ife kuti akatipimire (mlingo wokwana); ndithu ife tikamsunga.” info
التفاسير: