[95] Gulu la adani lija lidabwerera kwawo. Koma ena mwa Asilamu achinyengo omwe adali m’gulu la Asilamu omwe sadathawe pomwe anzawo amathawa, sadakhulupirire kuti adaniwo abwerera kwawo, chifukwa choopa; amangoganiza kuti akadalipobe ndipo mwina awathiranso nkhondo kachiwiri. Tero adadzazidwa mantha m’mitima mwawo ndipo tulo tidawasowa. Koma Asilamu enieni sadalabadire chilichonse. Amangodya ndi kugona ngati kuti zopweteka sizinawakhudze.