Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Al-Muddathir   Versículo:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
Os Tafssir em língua árabe:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
Os Tafssir em língua árabe:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
Os Tafssir em língua árabe:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
Os Tafssir em língua árabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
Os Tafssir em língua árabe:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
Os Tafssir em língua árabe:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
Os Tafssir em língua árabe:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
Os Tafssir em língua árabe:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
Os Tafssir em língua árabe:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
Os Tafssir em língua árabe:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
Os Tafssir em língua árabe:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
Os Tafssir em língua árabe:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
Os Tafssir em língua árabe:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
Os Tafssir em língua árabe:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
Os Tafssir em língua árabe:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
Os Tafssir em língua árabe:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
Os Tafssir em língua árabe:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
Os Tafssir em língua árabe:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
Os Tafssir em língua árabe:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
Os Tafssir em língua árabe:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Al-Muddathir
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala - Índice de tradução

Tradução por Khaled Ibrahim Bitala.

Fechar