Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala

Número de página:close

external-link copy
38 : 4

وَٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ رِئَآءَ ٱلنَّاسِ وَلَا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَلَا بِٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۗ وَمَن يَكُنِ ٱلشَّيۡطَٰنُ لَهُۥ قَرِينٗا فَسَآءَ قَرِينٗا

Ndi omwe akupereka chuma chawo modzionetsera kwa anthu ndipo sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Ndiponso yemwe satana angakhale bwenzi lake, ndithudi ali ndi bwenzi loipa. info
التفاسير:

external-link copy
39 : 4

وَمَاذَا عَلَيۡهِمۡ لَوۡ ءَامَنُواْ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَأَنفَقُواْ مِمَّا رَزَقَهُمُ ٱللَّهُۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِهِمۡ عَلِيمًا

Kodi pakadakhala vuto lanji kwa iwo ngati akadakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro napereka zina mwa zomwe Allah wawapatsa? Ndipo Allah ali Wodziwa bwino za iwo. info
التفاسير:

external-link copy
40 : 4

إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَظۡلِمُ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖۖ وَإِن تَكُ حَسَنَةٗ يُضَٰعِفۡهَا وَيُؤۡتِ مِن لَّدُنۡهُ أَجۡرًا عَظِيمٗا

Ndithudi, Allah sachitira (anthu) zosalungama ngakhale kanthu kolemera ngati kanyelere; ngati kanthuko kali kabwino amakachulukitsa ndi kupereka malipiro aakulu kuchokera kwa Iye. info
التفاسير:

external-link copy
41 : 4

فَكَيۡفَ إِذَا جِئۡنَا مِن كُلِّ أُمَّةِۭ بِشَهِيدٖ وَجِئۡنَا بِكَ عَلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِ شَهِيدٗا

Nanga zidzakhala bwanji tikadzabweretsa mboni pa m’badwo uliwonse ndikukubweretsa iwe (Mneneri Muhammad{s.a.w}) kuti ukhale mboni pa m’badwo uwu. info
التفاسير:

external-link copy
42 : 4

يَوۡمَئِذٖ يَوَدُّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَعَصَوُاْ ٱلرَّسُولَ لَوۡ تُسَوَّىٰ بِهِمُ ٱلۡأَرۡضُ وَلَا يَكۡتُمُونَ ٱللَّهَ حَدِيثٗا

Tsiku limenelo aja omwe sadakhulupirire namunyoza Mtumiki, adzakhumba kuti nthaka ikadafafanizidwa pa iwo (akwiliridwe, asaukitsidwe). Ndipo sadzatha kum’bisira Allah nkhani iliyonse (m’zomwe adachita m’moyo wa pa dziko). info
التفاسير:

external-link copy
43 : 4

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَقۡرَبُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَأَنتُمۡ سُكَٰرَىٰ حَتَّىٰ تَعۡلَمُواْ مَا تَقُولُونَ وَلَا جُنُبًا إِلَّا عَابِرِي سَبِيلٍ حَتَّىٰ تَغۡتَسِلُواْۚ وَإِن كُنتُم مَّرۡضَىٰٓ أَوۡ عَلَىٰ سَفَرٍ أَوۡ جَآءَ أَحَدٞ مِّنكُم مِّنَ ٱلۡغَآئِطِ أَوۡ لَٰمَسۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ فَلَمۡ تَجِدُواْ مَآءٗ فَتَيَمَّمُواْ صَعِيدٗا طَيِّبٗا فَٱمۡسَحُواْ بِوُجُوهِكُمۡ وَأَيۡدِيكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَفُوًّا غَفُورًا

E inu amene mwakhulupirira! Musayandikire Swala uku muli oledzera, mpaka mudziwe chimene mukunena; ngakhalenso pamene muli ndi janaba (musapemphere kufikira mutasamba) kupatula amene ali pa ulendo (achite Tayammam). Ndipo ngati muli odwala, kapena muli pa ulendo, kapena m’modzi wanu wadza kuchokera kuchimbudzi, kapena mwakhudza akazi (m’njira ya ukwati) ndipo simunapeze madzi (osamba) chitani Tayammam ndi dothi labwino; lipakeni kunkhope kwanu ndi m’mikono mwanu. Ndithudi, Allah Ngofafaniza machimo, Ngokhululuka kwambiri. info
التفاسير:

external-link copy
44 : 4

أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ نَصِيبٗا مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ يَشۡتَرُونَ ٱلضَّلَٰلَةَ وَيُرِيدُونَ أَن تَضِلُّواْ ٱلسَّبِيلَ

Kodi sukuwaona omwe adapatsidwa gawo la (nzeru zozindikira) buku (la Allah, omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu), akudzisankhira kusokera ndiponso akufuna mutasokera kusiya njira (yabwino).[125] info

[125] (Ndime 44-46) Apa akutchula kuipa kwina kwa Ayuda ndi Akhrisitu. Iwo adali kusintha mawu omwe adali m’mabuku a Taurat ndi Injil, makamaka mawu amene adali kusonyeza za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Kapena adali kuwatanthauzira m’njira zina zogwirizana ndi zolinga zawo. Pamene adali kudza kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) makamaka Ayuda, akawalalikira mawu achipembedzo, ankati: “Tamva, titsatira,” pomwe m’mitima mwawo akuti “Sititsatira zonse zomwe ukunena. Koma tikungokunyenga chabe.” Amati akadza nkumva momwe maswahaba amanenera ndi Mtumiki (s.a.w), Mtumiki akawalalikira, amati: “Ismaa ghayra musma’” monga mwa chizolowezi cha Arabu akauzidwa mawu ofunika. Tanthuzo lake nkuti, “Imva siumvanso choipa kuchokera kwa ife ngati Allah afuna.” Naonso Ayuda adali kumnenera Mtumiki mawu omwewa, koma m’mitima mwawo akulinga tanthauzo lina. M’mitima mwawo amalinga kuti, “Siumva zabwino kuchokera kwa ife ngati Allah afuna, koma zokusowetsa mtendere zokhazokha.” Ndipo amati akabweranso Ayudawo nkumva maswahaba akumuuza Mtumiki kuti; “Raa’ina”. Kutanthauza kuti, “Tiyang’ane ndi diso lachifundo,” iwonso amayankhula mawu omwewa, koma mokhotetsa pang’ono mpaka kusinthika tanthauzo lake. M’chiyankhulo cha chiyuda limatanthauza kuti “E iwe mbutuma!” Ndipo iwo m’kunena kwawo amalinga tanthauzo limeneli. Choncho Asilamu anawauza kuti azigwiritsira ntchito mawu oti “Undhurna.” Ndipo mawuwa tanthauzo lake ndilofanana. Koma mawu awa Ayuda sakadatha kuwakhotetsa.

التفاسير: