د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا

external-link copy
102 : 3

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ حَقَّ تُقَاتِهِۦ وَلَا تَمُوتُنَّ إِلَّا وَأَنتُم مُّسۡلِمُونَ

E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah; kuopa kwenikweni. Ndipo musafe pokhapokha mutakhala Asilamu (ogonjera).[76] info

[76] Pa ndime iyi akulangiza kuti nthawi iliyonse munthu akhale m’chikhalidwe cha Chisilamu chokwanira popewa zoletsedwa ndi kumachita zimene alamulidwa kuchita mmene angathere, chifukwa chakuti munthu sangadziwe nthawi imene imfa ingamufikire.

التفاسير: