വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ

പേജ് നമ്പർ:close

external-link copy
203 : 2

۞ وَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ فِيٓ أَيَّامٖ مَّعۡدُودَٰتٖۚ فَمَن تَعَجَّلَ فِي يَوۡمَيۡنِ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِ وَمَن تَأَخَّرَ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِۖ لِمَنِ ٱتَّقَىٰۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ إِلَيۡهِ تُحۡشَرُونَ

Ndipo mtamandeni Allah m’masiku owerengeka. Koma amene wachita changu pa masiku awiri okha (nabwerera kwawo) palibe tchimo pa iye. Ndipo amene wachedwerapo palibenso tchimo pa iye kwa amene akuopa Allah. Choncho opani Allah, ndipo dziwani kuti kwa Iye nkumene mudzasonkhanitsidwa. info
التفاسير:

external-link copy
204 : 2

وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يُعۡجِبُكَ قَوۡلُهُۥ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَيُشۡهِدُ ٱللَّهَ عَلَىٰ مَا فِي قَلۡبِهِۦ وَهُوَ أَلَدُّ ٱلۡخِصَامِ

Ndipo mwa anthu alipo amene zoyankhula zake zikukondweretsa (iwe) pano pa dziko la pansi, (koma tsiku lachimaliziro kuipa kwake kudzadziwika). Ndipo iye akutsimikizira Allah kuti akhale mboni pa zomwe zili mu mtima mwake pomwe iye ndi wa makani kwambiri.[25] info

[25] Tanthauzo lake nkuti alipo ena mwa anthu omwe angakukometsere zoyankhula zawo ndi kuthwa kwa lirime lawo pomwe iwo chikhalirecho akungoyankhula kuti apeze zinthu za m’dziko.
Ndimeyi ikufotokoza za Al-Akhnas bun Sharik yemwe amati akakumana ndi Mtumiki (s.a.w), amatamanda ndi kusonyeza chikhulupiliro chabodza. Koma akachoka pamaso pa mtumiki (s.a.w) amayenda pa dziko ncholinga choononga.
Umo ndi momwe alili makhalidwe a anthu ena, amangokometsa mawu pomwe zochita zawo nzauve. Tero tichenjere ndi anthu otere.

التفاسير:

external-link copy
205 : 2

وَإِذَا تَوَلَّىٰ سَعَىٰ فِي ٱلۡأَرۡضِ لِيُفۡسِدَ فِيهَا وَيُهۡلِكَ ٱلۡحَرۡثَ وَٱلنَّسۡلَۚ وَٱللَّهُ لَا يُحِبُّ ٱلۡفَسَادَ

Koma akachoka (kwa iwe) akuyenda pa dziko (uku ndi uku) ncholinga chofuna kuyipitsapo ndi kuononga zomera ndi miyoyo. Komatu Allah sakonda kuononga. info
التفاسير:

external-link copy
206 : 2

وَإِذَا قِيلَ لَهُ ٱتَّقِ ٱللَّهَ أَخَذَتۡهُ ٱلۡعِزَّةُ بِٱلۡإِثۡمِۚ فَحَسۡبُهُۥ جَهَنَّمُۖ وَلَبِئۡسَ ٱلۡمِهَادُ

Ndipo akauzidwa kuti: “Opa Allah”, Akugwidwa ndi mwano womupititsa ku machimo, choncho Jahannam ikukwana kwa iye (kuwuchotsa mwano wakewo). Taonani kuipa kwa malo wokakhazikikamo! info
التفاسير:

external-link copy
207 : 2

وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يَشۡرِي نَفۡسَهُ ٱبۡتِغَآءَ مَرۡضَاتِ ٱللَّهِۚ وَٱللَّهُ رَءُوفُۢ بِٱلۡعِبَادِ

Ndipo pali wina mwa anthu amene akugulitsa mzimu wake chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah; ndipo Allah Ngodekha kwa akapolo ake.[26] info

[26] Ndimeyi idavumbulutsidwa pankhani yokhudzana ndi wophunzira wina wa Mtumiki (s.a.w) dzina lake Suhaib Al-Rumi. Iyeyu pamene anafuna kusamuka ku Makka kupita ku Madina ma Quraish anamutsekereza, ndipo adamuuza kuti ngati akufuna kusamuka asiye chuma chake chonse, kupanda kutero sangasamuke. Choncho adalolera kusiya chuma chake chonse pofuna kudzipulumutsa yekha kuti asamukire ku Madina. Allah anakondwera nayo nkhaniyi ndipo adavumbulutsa ndimeyi.

التفاسير:

external-link copy
208 : 2

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱدۡخُلُواْ فِي ٱلسِّلۡمِ كَآفَّةٗ وَلَا تَتَّبِعُواْ خُطُوَٰتِ ٱلشَّيۡطَٰنِۚ إِنَّهُۥ لَكُمۡ عَدُوّٞ مُّبِينٞ

E inu amene mwakhulupirira! Lowani m’Chisilamu chonse ndipo musatsatire mapazi a satana. Ndithu iye ndi mdani wanu woonekera poyera.[27] info

[27] E inu amene mwakhulupilira! Inu eni mabuku, gonjerani Allah. Ndipo lowani m’Chisilamu kwathunthu posachisokoneza ndi chinachache. Mawuwa adanenedwa pamene Abdullahi bun Salaami adalowa m’Chisilamu yemwe adali mkulu wachiyuda. lye adapempha chilolezo kwa mtumiki (s.a.w) kuti aziliremekezabe tsiku la Sabata (la chiweru) ndi kuti aziwerenga mawu a m’Taurati mu Swala zake zausiku.

التفاسير:

external-link copy
209 : 2

فَإِن زَلَلۡتُم مِّنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡكُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٌ

Ndipo ngati mutaterezuka (kuchimwa) pambuyo pokudzerani zisonyezo (za Allah) zoonekera poyera, dziwani kuti Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya. info
التفاسير:

external-link copy
210 : 2

هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّآ أَن يَأۡتِيَهُمُ ٱللَّهُ فِي ظُلَلٖ مِّنَ ٱلۡغَمَامِ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَقُضِيَ ٱلۡأَمۡرُۚ وَإِلَى ٱللَّهِ تُرۡجَعُ ٱلۡأُمُورُ

Kodi pali china chimene akuyembekeza posakhala kuwadzera Allah m’mithunzi ya mitambo ndi (kuwadzera) angelo; nkuweruzidwa chilamulo (chakuonongeka kwawo)? Komatu zinthu zonse zimabwezedwa kwa Allah. info
التفاسير: