വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ

പേജ് നമ്പർ: 247:235 close

external-link copy
104 : 12

وَمَا تَسۡـَٔلُهُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۚ إِنۡ هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ

Ndipo sukuwapempha malipiro pa zimenezi. Sichina izi (zimene wadza nazo), koma ndi ulaliki kwa zolengedwa zonse. info
التفاسير:

external-link copy
105 : 12

وَكَأَيِّن مِّنۡ ءَايَةٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ يَمُرُّونَ عَلَيۡهَا وَهُمۡ عَنۡهَا مُعۡرِضُونَ

Ndipo ndi zisonyezo zingati (zosonyeza kuti Allah alipo) kumwamba ndi pansi zomwe akuzidutsa pamene iwo sakuzilabadira.[233] info

[233] Apa tanthauzo lake nkuti zilipo zisonyezo zambiri zosonyeza kuti Allah alipo zomwe iwo akuziona ali pamudzi ndiponso akuzidutsa akakhala pa maulendo awo monga thambo, nthaka, dzuwa, mwezi, nyenyezi, mapiri ndi zina zambiri zododometsa zimene zikupezeka kumwamba ndi pansi. Akuziona m’mawa ndi madzulo koma iwo saziganizira.

التفاسير:

external-link copy
106 : 12

وَمَا يُؤۡمِنُ أَكۡثَرُهُم بِٱللَّهِ إِلَّا وَهُم مُّشۡرِكُونَ

Ndipo ambiri a iwo sakhulupirira Allah koma momphatikiza. [234] info

[234] Apa akutanthauza kuti ambiri a iwo amamphatikiza Allah ndi milungu yabodza. Iwo amavomereza kuti Allah ndiye Mlengi wopatsa zonse. Koma kuonjezera pachikhulupiliro choterechi, amapembedzanso mafano. Ndipo zoterezi masiku ano zikumachitika ndi Asilamu ena amene amafuulira mizimu ya anthu akufa kuti iwathangate pa mavuto amene awagwera, komwe nkumuphatikiza Allah ndi mizimu ya anthu akufa.

التفاسير:

external-link copy
107 : 12

أَفَأَمِنُوٓاْ أَن تَأۡتِيَهُمۡ غَٰشِيَةٞ مِّنۡ عَذَابِ ٱللَّهِ أَوۡ تَأۡتِيَهُمُ ٱلسَّاعَةُ بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ

Kodi akudziika pachitetezo kuti silingawadzere tsoka lachilango cha Allah, kapena kuti siingawadzere Qiyâma mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira? info
التفاسير:

external-link copy
108 : 12

قُلۡ هَٰذِهِۦ سَبِيلِيٓ أَدۡعُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِۚ عَلَىٰ بَصِيرَةٍ أَنَا۠ وَمَنِ ٱتَّبَعَنِيۖ وَسُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ وَمَآ أَنَا۠ مِنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ

Nena: “Iyi ndi njira yanga. Ndikuitanira kwa Allah mwa nzeru zokwanira, ine ndi omwe akunditsata. Ndithu Allah wapatukana (ndi mbiri zopunguka). Ndipo ine sindili mwa ophatikiza (Allah ndi zinthu zina).”[235] info

[235] Apa Mtumiki (s.a.w) akuuzidwa kuti awauze anthu kuti iye pamodzi ndi amene akumutsata kuti amalalikira Chisilamu kwa anthu popereka kwa anthuwo mitsutso yanzeru, ndikuperekanso zisonyezo ndi maumboni amphamvu. Sibwino Msilamu kutsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino. Qur’an ikunenetsa kuti osatsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino pokhapokha chinthucho chitanenedwa ndi Allah kapena Mtumiki Wake.

التفاسير:

external-link copy
109 : 12

وَمَآ أَرۡسَلۡنَا مِن قَبۡلِكَ إِلَّا رِجَالٗا نُّوحِيٓ إِلَيۡهِم مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡقُرَىٰٓۗ أَفَلَمۡ يَسِيرُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَيَنظُرُواْ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡۗ وَلَدَارُ ٱلۡأٓخِرَةِ خَيۡرٞ لِّلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ

Ndipo sitidatume (mtumiki aliyense) patsogolo pako koma adali amuna amene tidawavumbulutsira (chivumbulutso); ochokera mwa anthu a m’mizinda. Kodi sadayende (iwo osakhulupirira) pa dziko nkuona momwe mathero a oipa omwe adalipo patsogolo pawo (momwe adalili)? Ndipo nyumba ya tsiku la chimaliziro njabwino kwa owopa Allah. Kodi mulibe nzeru? info
التفاسير:

external-link copy
110 : 12

حَتَّىٰٓ إِذَا ٱسۡتَيۡـَٔسَ ٱلرُّسُلُ وَظَنُّوٓاْ أَنَّهُمۡ قَدۡ كُذِبُواْ جَآءَهُمۡ نَصۡرُنَا فَنُجِّيَ مَن نَّشَآءُۖ وَلَا يُرَدُّ بَأۡسُنَا عَنِ ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ

Mpaka pamene atumiki adataya mtima (za anthu awo) nkuganiza kuti ayesedwa onama, chithandizo chathu chidawadzera, ndipo amene tidawafuna adapulumuka. Koma chilango chathu sichibwezedwa kwa anthu oipa. info
التفاسير:

external-link copy
111 : 12

لَقَدۡ كَانَ فِي قَصَصِهِمۡ عِبۡرَةٞ لِّأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِۗ مَا كَانَ حَدِيثٗا يُفۡتَرَىٰ وَلَٰكِن تَصۡدِيقَ ٱلَّذِي بَيۡنَ يَدَيۡهِ وَتَفۡصِيلَ كُلِّ شَيۡءٖ وَهُدٗى وَرَحۡمَةٗ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ

Ndithu m’nkhani zawo izi muli phunziro kwa eni nzeru. (Qur’aniyi) simawu opekedwa, koma (iyi Qur’an) ndi chitsimikizo cha zomwe zidalipo patsogolo pake (m’mabuku ena a Allah), ndi kumasulira kwa tsatanetsatane pa chilichonse ndiponso chiongoko ndi mtendere kwa anthu okhulupirira. info
التفاسير: