[193] Pamene nkhondo idayaka moto, Mtumiki (s.a.w) adatapa mchenga naufumbata m’manja mwake naupemphelera. Kenako adaumwaza kumbali ya adani. Ndipo mchengawo udalowa m’maso mwa aliyense wa adaniwo. Pa nkhondoyi anthu osakhulupilira Allah adali ambiri kuposa Asilamu. Koma ngakhale zidali choncho, Asilamu adagonjetsa adaniwo kwathunthu. Ambiri adaphedwa, ndipo ambirinso adagwidwa monga akaidi.