क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - ख़ालिद अबराहीम बेताला

पृष्ठ संख्या:close

external-link copy
16 : 33

قُل لَّن يَنفَعَكُمُ ٱلۡفِرَارُ إِن فَرَرۡتُم مِّنَ ٱلۡمَوۡتِ أَوِ ٱلۡقَتۡلِ وَإِذٗا لَّا تُمَتَّعُونَ إِلَّا قَلِيلٗا

Nena: “Kuthawa sikungakuthandizeni ngati mukuthawa imfa kapena kuphedwa; choncho (kuthawa kwanuku) simusangalatsidwa (nako) koma pang’ono basi. (Kenako ikatha nthawi ya moyo wanu, mukufa).” info
التفاسير:

external-link copy
17 : 33

قُلۡ مَن ذَا ٱلَّذِي يَعۡصِمُكُم مِّنَ ٱللَّهِ إِنۡ أَرَادَ بِكُمۡ سُوٓءًا أَوۡ أَرَادَ بِكُمۡ رَحۡمَةٗۚ وَلَا يَجِدُونَ لَهُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا

Nena: “Kodi ndani amene angakutetezeni kwa Allah, ngati atafuna kukuchitirani choipa; kapena atafuna kukuchitirani chifundo?” Ndipo sadzapeza mthandizi ndi mtetezi kupatula Allah. info
التفاسير:

external-link copy
18 : 33

۞ قَدۡ يَعۡلَمُ ٱللَّهُ ٱلۡمُعَوِّقِينَ مِنكُمۡ وَٱلۡقَآئِلِينَ لِإِخۡوَٰنِهِمۡ هَلُمَّ إِلَيۡنَاۖ وَلَا يَأۡتُونَ ٱلۡبَأۡسَ إِلَّا قَلِيلًا

Ndithu Allah akuwadziwa amene akudziletsa mwa inu (kupita ku nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kuletsanso anthu ena), ndi amene akuuza abale awo: “Bwerani kwa ife; (m’thaweni Muhammad {s.a.w}).” Ndiponso sapita ku nkhondo koma pang’ono pokha. info
التفاسير:

external-link copy
19 : 33

أَشِحَّةً عَلَيۡكُمۡۖ فَإِذَا جَآءَ ٱلۡخَوۡفُ رَأَيۡتَهُمۡ يَنظُرُونَ إِلَيۡكَ تَدُورُ أَعۡيُنُهُمۡ كَٱلَّذِي يُغۡشَىٰ عَلَيۡهِ مِنَ ٱلۡمَوۡتِۖ فَإِذَا ذَهَبَ ٱلۡخَوۡفُ سَلَقُوكُم بِأَلۡسِنَةٍ حِدَادٍ أَشِحَّةً عَلَى ٱلۡخَيۡرِۚ أُوْلَٰٓئِكَ لَمۡ يُؤۡمِنُواْ فَأَحۡبَطَ ٱللَّهُ أَعۡمَٰلَهُمۡۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا

Okuchitirani inu umbombo (pa chikondi ndi pa chifundo; sakufunirani zabwino). Koma mantha akadza uwaona akukuyang’ana, uku maso awo akutembenuka (mophethiraphethira) monga a amene wakomoledwa ndi imfa. Koma mantha akachoka, akukupatsani masautso ndi malirime awo akuthwa; mbombo pa chabwino chilichonse. Iwowo sadakhulupirire ndipo choncho Allah wagwetsa malipiro a zochita zawo. Zimenezo nzosavuta kwa Allah. info
التفاسير:

external-link copy
20 : 33

يَحۡسَبُونَ ٱلۡأَحۡزَابَ لَمۡ يَذۡهَبُواْۖ وَإِن يَأۡتِ ٱلۡأَحۡزَابُ يَوَدُّواْ لَوۡ أَنَّهُم بَادُونَ فِي ٱلۡأَعۡرَابِ يَسۡـَٔلُونَ عَنۡ أَنۢبَآئِكُمۡۖ وَلَوۡ كَانُواْ فِيكُم مَّا قَٰتَلُوٓاْ إِلَّا قَلِيلٗا

(Kufikira tsopano chifukwa cha mantha awo) akuganiza kuti magulu a nkhondo (adani) sadapitebe; ndipo magulu amenewo akadadzanso, akadalakalaka akadakhala kuchipululu pamodzi ndi arabu a kuchimidzi ndi kuti azikangofunsa za nkhani zanu. Akadakhala pamodzi ndi inu sadakamenyana (ndi adani) koma pang’ono pokha.[319] info

[319] Kuyambira ndime 12 mpaka 20, Allah akufotokoza makhalidwe a anthu ena amene adangolowa m’Chisilamu ndi lirime lokha pomwe mitima yawo siidakhulupirire. Nthawi zambiri ankamchitira Mtumiki (s.a.w) zachinyengo. Mtumiki (s.a.w) akalamula lamulo loti akalimbane ndi adani achipembedzo cha Chisilamu, iwo amagwetsa ulesi anthu kuti asapite ku nkhondoko. Nthawi zambiri samawafunira Asilamu zabwino. Akangouzidwa kuti tiyeni ku nkhondo, amagwidwa ndi mantha.

التفاسير:

external-link copy
21 : 33

لَّقَدۡ كَانَ لَكُمۡ فِي رَسُولِ ٱللَّهِ أُسۡوَةٌ حَسَنَةٞ لِّمَن كَانَ يَرۡجُواْ ٱللَّهَ وَٱلۡيَوۡمَ ٱلۡأٓخِرَ وَذَكَرَ ٱللَّهَ كَثِيرٗا

Ndithu muli nacho chitsanzo chabwino mwa Mthenga wa Allah (m’kudzipereka kwake ndi khama lake pa njira ya Allah, ndi kupirira kwake ndi masautso) kwa yemwe akuopa Allah ndi tsiku lachimaliziro, namatchula Allah kwambiri. info
التفاسير:

external-link copy
22 : 33

وَلَمَّا رَءَا ٱلۡمُؤۡمِنُونَ ٱلۡأَحۡزَابَ قَالُواْ هَٰذَا مَا وَعَدَنَا ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥ وَصَدَقَ ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥۚ وَمَا زَادَهُمۡ إِلَّآ إِيمَٰنٗا وَتَسۡلِيمٗا

Ndipo pamene okhulupirira adaona magulu a nkhondo (a adani atawazinga mbali zonse), adati: “Ichi ndichimene Allah ndi Mtumiki Wake adatilonjeza (kuti tidzapeza masautso, kenako nkupambana), ndipo Allah ndi Mtumiki Wake adanena zoona.” Ndipo (ichi) sichidawaonjezere china, koma chikhulupiliro (mwa Allah) ndi kudzipereka. info
التفاسير: