Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ

Numéro de la page:close

external-link copy
58 : 7

وَٱلۡبَلَدُ ٱلطَّيِّبُ يَخۡرُجُ نَبَاتُهُۥ بِإِذۡنِ رَبِّهِۦۖ وَٱلَّذِي خَبُثَ لَا يَخۡرُجُ إِلَّا نَكِدٗاۚ كَذَٰلِكَ نُصَرِّفُ ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يَشۡكُرُونَ

Ndipo m’nthaka yabwino umatuluka mmera wake (mwachangu) mwachilolezo cha Mbuye wake. Ndipo nthaka yomwe ili yoipa siitulutsa (mmera wake) koma movutikira. M’menemo ndi momwe Tikuchifotokozera chivumbulutso momveka kwa anthu oyamika.[186] info

[186] Mmene ilili nthaka yopanda chonde pomeretsa mmera movutikira nchimodzimodzi ndi anthu oipa. Nkovuta kuwaika pa njira yabwino. Koma tisatope ndi kutaya mtima nawo. Tiyesetsebe kuwakokera ku njira yabwino.

التفاسير:

external-link copy
59 : 7

لَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا نُوحًا إِلَىٰ قَوۡمِهِۦ فَقَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥٓ إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ

Ndithudi, tidamtumiza Nuh kwa anthu ake. (Iye) adati: “E inu anthu anga! Pembedzani Allah. Inu mulibe mulungu wina koma Iye. Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.” info
التفاسير:

external-link copy
60 : 7

قَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِهِۦٓ إِنَّا لَنَرَىٰكَ فِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ

Akuluakulu a mwa anthu ake adati: “Ndithu ife tikukuona kuti uli m’kusokera koonekera (potiletsa izi zomwe tidawapeza nazo makolo athu).” info
التفاسير:

external-link copy
61 : 7

قَالَ يَٰقَوۡمِ لَيۡسَ بِي ضَلَٰلَةٞ وَلَٰكِنِّي رَسُولٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ

(Iye) adati: “E anthu anga! Palibe kusokera mwa ine. Koma ine ndine Mtumiki wochokera kwa Mbuye wa zolengedwa!” info
التفاسير:

external-link copy
62 : 7

أُبَلِّغُكُمۡ رِسَٰلَٰتِ رَبِّي وَأَنصَحُ لَكُمۡ وَأَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ

“Ndikufikitsa kwa inu uthenga wa Mbuye wanga. Ndiponso ndikukulangizani; ndipo ndikudziwa zochokera kwa Allah zomwe inu simukuzidziwa.” info
التفاسير:

external-link copy
63 : 7

أَوَعَجِبۡتُمۡ أَن جَآءَكُمۡ ذِكۡرٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَلَىٰ رَجُلٖ مِّنكُمۡ لِيُنذِرَكُمۡ وَلِتَتَّقُواْ وَلَعَلَّكُمۡ تُرۡحَمُونَ

“Kodi mukudabwa kukudzerani ulaliki wochokera kwa Mbuye wanu kudzera mwa munthu wa mwa inu, (yemwe wadza) kuti akuchenjezeni ndi kuti muope (Allah), ndikutinso muchitiridwe chifundo?” info
التفاسير:

external-link copy
64 : 7

فَكَذَّبُوهُ فَأَنجَيۡنَٰهُ وَٱلَّذِينَ مَعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ وَأَغۡرَقۡنَا ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَآۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَوۡمًا عَمِينَ

Koma adamtsutsa. Choncho, tidampulumutsa iye ndi amene adali naye pamodzi m’chombo. Ndipo tidawamiza aja adatsutsa zizindikiro Zathu. Ndithudi, iwo adali anthu akhungu.[187] info

[187] Nkhani ya Mneneri Nuh paliponse akuifotokoza motalikitsa. Koma m’sura iyi aifotokoza mwachidule. Ndipo Nuh ndimneneri wakale kwabasi. Iye adali kuwalalikira anthu a ku Iraq. Ndipo m’nthawi imeneyo pafupifupi dziko lonse lapansi chitukuko chidali ku Iraq monga momwe tikuwerengera m’mabuku ambiri yakale.

التفاسير:

external-link copy
65 : 7

۞ وَإِلَىٰ عَادٍ أَخَاهُمۡ هُودٗاۚ قَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥٓۚ أَفَلَا تَتَّقُونَ

Ndipo kwa Âdi (tidaatumizira) m’bale wawo Hûd. Adati: “E inu Anthu anga! Mpembedzeni Allah. Mulibe mulungu wina koma Iye basi. Kodi simungaope?” info
التفاسير:

external-link copy
66 : 7

قَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦٓ إِنَّا لَنَرَىٰكَ فِي سَفَاهَةٖ وَإِنَّا لَنَظُنُّكَ مِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ

Akuluakulu a mwa anthu ake omwe sadakhulupirire adanena: “Ife tili kukuona kuti uli mu uchidzete, ndipo ife tikukuganizira kuti ndiwe m’modzi wa a bodza.” info
التفاسير:

external-link copy
67 : 7

قَالَ يَٰقَوۡمِ لَيۡسَ بِي سَفَاهَةٞ وَلَٰكِنِّي رَسُولٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ

(Iye) adati: “E inu anthu anga! Palibe uchidzete mwa ine. Koma ine ndine Mtumiki wochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.” info
التفاسير: