[58] Apa akunena kuti ngati anthu ali pamalo pomwe palibe wodziwa kulemba ndipo akukongozana, wokongozedwayo apereke chikole kwa wokongoza kuti achisunge wokongozayo. Ndipo adzabwezera akadzabweza ngongoleyo. Ngati atalephera kubweza ngongoleyo chikolecho chigulitsidwe ndi muweruzi nkumpatsa wokongozayo ndalama zolingana nzomwe adamkongoza. Zotsalira pa chinthu chogulitsidwacho azipereke kwa mwini chikolecho. Uwu ndiwo ubwino wachikole pa malamulo a Chisilamu. Akalephera kubweza ngongoleyo chinthucho chimagulitsidwa ndi boma ndikumpatsa mwini ngongoleyo choyenerana naye pomwe chotsaliracho amachipereka kwa mwini wake. Kwa amene wagwirizira chikolecho saloledwa kuchita nacho chilichonse. Ngati akuchita nacho ntchito nkumachidyelera ndiye kuti akuchita machitidwe akatapira omwe ali oletsedwa. Koma chinthucho angochisunga.