[31] Apa akufotokoza kuti masautso ndi mavuto omwe mowa ndi njuga zimadzetsa ngaakulu zedi kuposa ubwino wake. Mowa umamchotsa munthu nzeru pomwe nzeru ndidalitso lalikulu kuposa chilichonse. Ndipo mowa umamuonongera munthu chuma ndi kumdzetsera matenda m’thupi mwake. Nayonso njuga nchimodzimodzi. Imawononga chuma ndi kuyambitsa chidani pakati pa anthu. Zonsezi zimadzetsa chisokonezo ku mtundu wa munthu.