[172] Allah sapereka chilango kwa anthu asanawatumizire Mtumiki. Ndiponso sangawalange pa zinthu zomwe nzosatheka kuzizindikira, pokhapokha Mtumiki atawaphunzitsa, monga kupemphera Swala, kusala m’mwezi wa Ramadan. Koma angawalange pazomwe iwo angathe kuzizindikira kuti nzoipa; monga munthu kumchenjelera mnzake ndi zina zotero.