Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Khaled Ibrahim Batyala

Page Number:close

external-link copy
66 : 4

وَلَوۡ أَنَّا كَتَبۡنَا عَلَيۡهِمۡ أَنِ ٱقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡ أَوِ ٱخۡرُجُواْ مِن دِيَٰرِكُم مَّا فَعَلُوهُ إِلَّا قَلِيلٞ مِّنۡهُمۡۖ وَلَوۡ أَنَّهُمۡ فَعَلُواْ مَا يُوعَظُونَ بِهِۦ لَكَانَ خَيۡرٗا لَّهُمۡ وَأَشَدَّ تَثۡبِيتٗا

Ndipo ngati tikadawalamula kuti: “Dzipheni nokha,” kapena: “Tulukani m’nyumba zanu; (mupite kunkhondo kapena musamuke),” sakadachita zimenezo kupatula ochepa mwa iwo. Koma akadachita zomwe auzidwa, zikadakhala zabwino kwa iwo. Ndipo zikadawalimbikitsa kwambiri (Chisilamu chawo). info
التفاسير:

external-link copy
67 : 4

وَإِذٗا لَّأٓتَيۡنَٰهُم مِّن لَّدُنَّآ أَجۡرًا عَظِيمٗا

Ndipo zikadatero, tikadawapatsa malipiro aakulu ochokera kwa Ife. info
التفاسير:

external-link copy
68 : 4

وَلَهَدَيۡنَٰهُمۡ صِرَٰطٗا مُّسۡتَقِيمٗا

Ndiponso tikadawatsogolera ku njira yoongoka (yokawafikitsa ku Munda wamtendere). info
التفاسير:

external-link copy
69 : 4

وَمَن يُطِعِ ٱللَّهَ وَٱلرَّسُولَ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَعَ ٱلَّذِينَ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلنَّبِيِّـۧنَ وَٱلصِّدِّيقِينَ وَٱلشُّهَدَآءِ وَٱلصَّٰلِحِينَۚ وَحَسُنَ أُوْلَٰٓئِكَ رَفِيقٗا

Ndipo amene angamvere Allah ndi Mtumiki wake, iwowo ndi omwe adzakhale pamodzi ndi omwe Allah adawadalitsa, kuyambira aneneri, olungama, mashahidi (asilamu ofela ku nkhondo) ndi anthu abwino. Taonani ubwino wokhala nawo pamodzi iwowo! info
التفاسير:

external-link copy
70 : 4

ذَٰلِكَ ٱلۡفَضۡلُ مِنَ ٱللَّهِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ عَلِيمٗا

Umenewo ndiubwino wochokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa mokwanira. info
التفاسير:

external-link copy
71 : 4

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ خُذُواْ حِذۡرَكُمۡ فَٱنفِرُواْ ثُبَاتٍ أَوِ ٱنفِرُواْ جَمِيعٗا

E inu amene mwakhulupirira! Khalani ochenjera (ndi adani anu; musanyengedwe nawo). Pitani (kunkhondo) gulu limodzilimodzi, kapena pitaniko nonsenu pamodzi (monga momwe Mtumiki angakulangizireni). info
التفاسير:

external-link copy
72 : 4

وَإِنَّ مِنكُمۡ لَمَن لَّيُبَطِّئَنَّ فَإِنۡ أَصَٰبَتۡكُم مُّصِيبَةٞ قَالَ قَدۡ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيَّ إِذۡ لَمۡ أَكُن مَّعَهُمۡ شَهِيدٗا

Ndipo ndithu alipo ena mwa inu otsalira m’mbuyo sapita ku nkhondo, (ndiponso amaletsa anzawo). Ngati vuto litakupezani, (yense wa iwo) amanena: “Allah wandichitira chisomo posakhala m’gulu lawo kumeneko.” info
التفاسير:

external-link copy
73 : 4

وَلَئِنۡ أَصَٰبَكُمۡ فَضۡلٞ مِّنَ ٱللَّهِ لَيَقُولَنَّ كَأَن لَّمۡ تَكُنۢ بَيۡنَكُمۡ وَبَيۡنَهُۥ مَوَدَّةٞ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ مَعَهُمۡ فَأَفُوزَ فَوۡزًا عَظِيمٗا

Koma ngati utakupezani ubwino wochokera kwa Allah (monga kupeza chuma chambiri chosiidwa ndi adani, kapena kupambana kumene) amanena ngati kuti padalibe chikondi pakati panu ndi pakati pake: “Kalanga ine! Ndikadakhala nawo pamodzi pa nkhondo imeneyi, (ndiye kuti) ndikadapambana; kupambana kwakukulu.” info
التفاسير:

external-link copy
74 : 4

۞ فَلۡيُقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ٱلَّذِينَ يَشۡرُونَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا بِٱلۡأٓخِرَةِۚ وَمَن يُقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَيُقۡتَلۡ أَوۡ يَغۡلِبۡ فَسَوۡفَ نُؤۡتِيهِ أَجۡرًا عَظِيمٗا

Choncho, amenye nkhondo pa njira ya Allah omwe akugulitsa moyo (wawo) wadziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo amene angamenye nkhondo pa njira ya Allah, kenako ndikuphedwa kapena kupambana tidzampatsa malipiro aakulu. info
التفاسير: