Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala

external-link copy
4 : 85

قُتِلَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡأُخۡدُودِ

Atembeleredwa eni ngalande zamoto (zomwe adali kuwazunzira okhulupirira Allah, achimuna ndi achikazi).[413] info

[413] Pamene Ayuda a ku Najrani adalowa m’Chikhristu, (Chisilamu chisadafike ndiponso Chikhristu chisadaonongeke), idamufika nkhaniyi mfumu yawo dzina lake Dhu-Nuwas; adabwera ku Najrani ndi gulu lankhondo lalikulu; adawakakamizira anthu ku Chiyuda koma iwo adakana. Nayamba kuwapha anthu okhulupilirawo powaponya m’ngalande za moto.

التفاسير: