Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala

Broj stranice:close

external-link copy
23 : 33

مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ رِجَالٞ صَدَقُواْ مَا عَٰهَدُواْ ٱللَّهَ عَلَيۡهِۖ فَمِنۡهُم مَّن قَضَىٰ نَحۡبَهُۥ وَمِنۡهُم مَّن يَنتَظِرُۖ وَمَا بَدَّلُواْ تَبۡدِيلٗا

Mwa okhulupirira alipo amuna ena amene adakwaniritsa zomwe adamlonjeza Allah (kuti sadzathawa pa nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w), ena mwa iwo adamaliza moyo wawo (nakwaniritsa lonjezo lawo pofera pa njira ya Allah). Ndipo ena mwa iwo akuyembekezerabe (kufera pa njira ya Allah). Ndipo sadasinthe konse (lonjezo lawo).[320] info

[320] Imamu Ibnu Jarir Taburiyu adalemba m’buku lake kuti Anasi Bun Malik adati:- M’bale wa bambo anga, Anasi bun Nadhari sadakhale nawo pa nkhondo ya Badri, ndipo adati: “Sindidakhale pamodzi ndi Mtumiki pa nkhondo yoyamba. Ngati Allah atandifikitsa pa nkhondo ina Allah adzaona zimene ndidzachita pomenya nkhondo modzipereka.” Pa tsiku la nkhondo ya Uhud, pamene Asilamu adabalalikana kuthawa ndipo iye adati:- “E Allah! Ine ndikudzipatula ku zomwe achita awa, osakhulupilira. Ndiponso ndikudandaula mzimene achita awa, Asilamu amene athawa.” Kenako adayenda ndi lupanga lake nakumana ndi Saad bun Muadhi, nati: “E iwe Saad! Ine ndikumva fungo la ku Munda wa mtendere pafupi ndi phiri ili la Uhud.” Kenako adachita nkhondo kufikira adaphedwa. Ndipo Saad adati: “E iwe Mtumiki wa Allah! Sindinathe kuchita chimene iye adachita.” Anasi bun Malik adati: “Tidampeza ali m’gulu lophedwa uku ali ndi mabala okwanira 80, ena otemedwa ndi malupanga, ndipo ena olasidwa ndi mikondo ndi mipaliro. Sitidamzindikire kufikira pamene adadza mlongo wake naamzindikira kupyolera m’nsonga za zala zake.” Ndipo Anasi adatinso: “Tidali kukambirana kuti ndime iyi ikukamba za iye.”

التفاسير:

external-link copy
24 : 33

لِّيَجۡزِيَ ٱللَّهُ ٱلصَّٰدِقِينَ بِصِدۡقِهِمۡ وَيُعَذِّبَ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ إِن شَآءَ أَوۡ يَتُوبَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا

Kuti Allah awalipire owona chifukwa cha kuona kwawo; ndi kuti awalange achiphamaso ngati atafuna, kapena kuwalandira kulapa kwawo (ngati atalapa). Ndithu Allah Ngokhululuka kwabasi Ngwachisoni chosatha. info
التفاسير:

external-link copy
25 : 33

وَرَدَّ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِغَيۡظِهِمۡ لَمۡ يَنَالُواْ خَيۡرٗاۚ وَكَفَى ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ ٱلۡقِتَالَۚ وَكَانَ ٱللَّهُ قَوِيًّا عَزِيزٗا

Ndipo Allah adawabweza amene sadakhulupirire uku ali odzazidwa ndi mkwiyo m’mitima mwawo; sadapeze chabwino; (sadagonjetse Asilamu ndi kupeza zimene ankaziyembekezera monga zotola za pa nkhondo). Ndipo Allah adawakwaniritsira okhulupirira nkhondo (powatumizira adani mphepo yamkuntho ndi angelo). Ndipo, Allah Ngwamphamvu, Ngopambana, (sapambanidwa ndi chilichonse). info
التفاسير:

external-link copy
26 : 33

وَأَنزَلَ ٱلَّذِينَ ظَٰهَرُوهُم مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ مِن صَيَاصِيهِمۡ وَقَذَفَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلرُّعۡبَ فَرِيقٗا تَقۡتُلُونَ وَتَأۡسِرُونَ فَرِيقٗا

Ndipo adawatsitsa m’malinga mwawo amene adathandiza adaniwo mwa anthu a buku (Ayuda). Ndipo adathira mantha m’mitima mwawo. Ena mumawapha; ndipo ena mumawagwira.[321] info

[321] Awa ndi Ayuda amene adasakanikirana ndi osakhulupilira (akafiri) a Chiarabu ochokera mu mtundu wa Banu Quraidhwa omwe adali ndi mapangano ndi Mtumiki (s.a.w) okhalirana mwa mtendere. Koma pamene adaswa mapangano pothandizana ndi adani a Mtumiki kuthira nkhondo Asilamu Mtumiki Muhammad (s.a.w) adawapitira ku malinga awo. Ndipo ena adawapha, pomwe ena adawagwira monga akaidi a pankhondo.

التفاسير:

external-link copy
27 : 33

وَأَوۡرَثَكُمۡ أَرۡضَهُمۡ وَدِيَٰرَهُمۡ وَأَمۡوَٰلَهُمۡ وَأَرۡضٗا لَّمۡ تَطَـُٔوهَاۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٗا

Ndipo adakupatsani dziko lawo, nyumba zawo, chuma chawo, ndi nthaka imene simudaipondepo. Allah Ngokhoza chilichonse. info
التفاسير:

external-link copy
28 : 33

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ قُل لِّأَزۡوَٰجِكَ إِن كُنتُنَّ تُرِدۡنَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا وَزِينَتَهَا فَتَعَالَيۡنَ أُمَتِّعۡكُنَّ وَأُسَرِّحۡكُنَّ سَرَاحٗا جَمِيلٗا

E iwe Mneneri! Nena kwa akazi ako (m’njira yowalangiza): “Ngati mufuna moyo wa dziko lapansi ndi zosangalatsa zake (ine ndilibe zosangalatsa za m’dziko, ndipo sindingakukakamizeni kuti mukhale ndi ine mu moyo wa umphawi; ngati mufuna) bwerani ndikupatsani cholekanira, chokusangalatsani, kenako ndikusiyeni kusiyana kwabwino (kopanda masautso).” info
التفاسير:

external-link copy
29 : 33

وَإِن كُنتُنَّ تُرِدۡنَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَٱلدَّارَ ٱلۡأٓخِرَةَ فَإِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلۡمُحۡسِنَٰتِ مِنكُنَّ أَجۡرًا عَظِيمٗا

“Ndipo ngati mukufuna Allah ndi Mtumiki Wake, ndi nyumba yomaliza, ndithu Allah wawakonzera ochita zabwino mwa inu malipiro aakulu.” info
التفاسير:

external-link copy
30 : 33

يَٰنِسَآءَ ٱلنَّبِيِّ مَن يَأۡتِ مِنكُنَّ بِفَٰحِشَةٖ مُّبَيِّنَةٖ يُضَٰعَفۡ لَهَا ٱلۡعَذَابُ ضِعۡفَيۡنِۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا

E inu akazi a Mneneri! Amene achite choipa choonekera mwa inu, amuonjezera chilango kawiri; ndipo zimenezi nzosavuta kwa Allah. [322] info

[322] Mu Ayah imeneyi, akazi a Mtumiki (s.a.w) akuuzidwa kuti iwo akachimwa, Allah adzawalanga chilango chachikulu kuposa momwe akadalangidwira akazi ena omwe sali akazi a Mtumiki (s.a.w). Izi nchifukwa chakuti, iwo ndi atsogoleri; chilichonse chomwe iwo achita, choipa kapena chabwino, chidzatsatidwa ndi ena. Akachita chabwino, Allah adzawapatsa malipiro aakulu. Ndipo akachita choipa, adzawalanga ndi chilango chachikulu. Choncho aliyense amene ndi mtsogoleri, aonetsetse kuti akuchita zolungama zokhazokha.

التفاسير: