[96] (Ndime 156-157) Apa Asilamu akuwapepesa kuti asaganizire kuti imfayo yawapeza anzawo chifukwa chopita ku nkhondo nkuti akadapanda kupitako sakadafa. Koma akuwauza kuti adafa chifukwa nthawi yawo yomwe Allah adawalembera kuti akhale pa dziko lapansi idatha. Ndipo ngakhale akadakhala m’nyumba zawo imfa ikadawapezabe. Ndipo akuwauzanso kuti imfa yofera ku nkhondo yoyera njabwino kuposa yofera pakhomo.