[90] Pamene Asilamu adamva ubwino waukulu umene angaupeze akafera pa nkhondoyo monga “Shahidi”, aliyense wa iwo adakhumba akadafera pa nkhondo yoteroyo, kuti akapeze ulemelerowo. Choncho Asilamu makumi asanu ndi awiri (70) adaphedwa pa nkhondo ya Uhudi mwa anthu mazana asanu ndi awiri (700) omwe adaima mwamphamvu kulimbana ndi anthu osakhulupilira omwe adalipo zikwi zitatu (3,000).